2 Samueli 10:1-19

  • Anagonjetsa Aamoni ndi Asiriya (1-19)

10  Kenako mfumu ya Aamoni+ inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni anayamba kulamulira mʼmalo mwake.+  Zitatero, Davide anati: “Ndimusonyeza Hanuni mwana wa Nahasi chikondi chokhulupirika ngati mmene bambo ake anandisonyezera chikondi chokhulupirika.” Choncho Davide anatumiza atumiki ake kuti akamutonthoze chifukwa cha imfa ya bambo ake. Koma atumiki a Davidewo atangofika mʼdziko la Aamoni,  akalonga a Aamoni anauza Hanuni mbuye wawo kuti: “Kodi mukuganiza kuti Davide watumiza anthu odzakutonthozani chifukwa cholemekeza bambo anu? Kodi iye sanatumize atumiki akewa kuti adzafufuze zokhudza mzindawu nʼcholinga choti adzaulande?”  Choncho Hanuni anatenga atumiki a Davide aja nʼkuwameta ndevu mbali imodzi,+ kenako anadula zovala zawo pakati moti zinalekeza mʼmatako nʼkuwauza kuti azipita.  Davide atamva zimenezi, nthawi yomweyo anatumiza anthu kuti akakumane nawo chifukwa atumiki akewo anali atachititsidwa manyazi kwambiri. Choncho mfumu inawauza kuti: “Mukhalebe ku Yeriko+ mpaka ndevu zanu zitakula, kenako mudzabwere.”  Patapita nthawi, Aamoni anaona kuti akhala ngati chinthu chonunkha kwa Davide. Choncho anatumiza anthu kuti akalembe ganyu Asiriya a ku Beti-rehobu+ ndi Asiriya a ku Zoba+ ndipo onse pamodzi analipo asilikali 20,000 oyenda pansi. Anapitanso kwa mfumu ya ku Maaka+ nʼkulemba ganyu amuna 1,000 komanso ku Isitobu amuna 12,000.+  Davide atamva zimenezi anatumiza Yowabu ndi gulu lonse lankhondo, limodzinso ndi asilikali ake amphamvu.+  Ndiyeno Aamoni anapita kukaima pageti la mzinda atakonzekera kumenya nkhondo. Pomwe Asiriya a ku Zoba, a ku Rehobu, a ku Isitobu ndi a ku Maaka anakayalana kwaokha kutchire.  Yowabu ataona kuti adani ake akubwera kuchokera kutsogolo ndi kumbuyo, anasankha ena mwa magulu a asilikali amphamvu mu Isiraeli nʼkuwakonzekeretsa kuti amenyane ndi Asiriya.+ 10  Anthu ena onse anawapereka kwa mchimwene wake Abisai+ kuti awatsogolere pokamenyana ndi Aamoni.+ 11  Ndiyeno anamuuza kuti: “Ukaona kuti Asiriya akundigonjetsa, ubwere udzandipulumutse. Koma Aamoni akayamba kukugonjetsa, ineyo ndibwera kudzakupulumutsa. 12  Tikuyenera kuchita zinthu mwamphamvu komanso molimba mtima+ chifukwa cha anthu athu ndiponso chifukwa cha mizinda ya Mulungu wathu. Yehova adzachita zimene akuona kuti nʼzabwino kwa iye.”+ 13  Kenako Yowabu ndi amuna amene anali naye anapita kukamenyana ndi Asiriya ndipo Asiriyawo anayamba kuthawa.+ 14  Aamoni ataona kuti Asiriya athawa, nawonso anathawa Abisai nʼkupita mumzinda. Yowabu atamaliza kumenyana ndi Aamoni anabwerera ku Yerusalemu. 15  Asiriya ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisiraeli, anasonkhananso pamodzi.+ 16  Choncho Hadadezeri+ anatuma anthu kuti akatenge Asiriya amene anali mʼdera la ku Mtsinje.*+ Atatero anabwera ku Helamu ndipo Sobaki mkulu wa asilikali a Hadadezeri ndi amene ankawatsogolera. 17  Davide atamva zimenezi, nthawi yomweyo anasonkhanitsa Aisiraeli onse nʼkuwoloka Yorodano kupita ku Helamu. Ndiyeno Asiriya anayalana kuti akumane ndi Davide ndipo anayamba kumenyana naye.+ 18  Koma Asiriyawo anayamba kuthawa Isiraeli ndipo Davide anapha asilikali a Siriya 700 okwera magaleta komanso asilikali 40,000 okwera pamahatchi. Iye anaphanso Sobaki, mtsogoleri wa gulu lankhondo la Siriya.+ 19  Mafumu onse amene anali atumiki a Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisiraeli, nthawi yomweyo anakhazikitsa mtendere ndi Aisiraeli nʼkuyamba kuwatumikira.+ Asiriya anachita mantha kwambiri moti sanayesenso kuthandiza Aamoni.

Mawu a M'munsi

Umenewu ndi mtsinje wa Firate.