2 Samueli 7:1-29

  • Davide anamuletsa kumanga kachisi (1-7)

  • Pangano la ufumu ndi Davide (8-17)

  • Pemphero la Davide loyamikira (18-29)

7  Mfumu inkakhala mʼnyumba yake*+ ndipo Yehova anachititsa kuti izikhala mwamtendere komanso isamavutitsidwe ndi adani ake onse.  Ndiyeno mfumuyo inauza mneneri Natani+ kuti: “Ine ndikukhala mʼnyumba ya mitengo ya mkungudza,+ pamene Likasa la Mulungu woona likukhala mutenti.”+  Natani anauza mfumu kuti: “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukufuna, chifukwa Yehova ali nanu.”+  Usiku wa tsiku lomwelo, Yehova analankhula ndi Natani kuti:  “Pita ukauze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Kodi iwe uyenera kundimangira nyumba yoti ine ndikhalemo?+  Kuchokera tsiku limene ndinatulutsa Aisiraeli mu Iguputo mpaka lero,+ sindinakhalepo mʼnyumba koma nthawi zonse ndinkayendayenda ndili mutenti.+  Pa nthawi yonse imene ndinkayenda ndi Aisiraeli,* kodi ndinayamba ndafunsapo atsogoleri a mafuko a Isiraeli amene ndinawasankha kuti azitsogolera anthu anga Aisiraeli kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”’  Tsopano mtumiki wanga Davide ukamuuze kuti, ‘Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti: “Ine ndinakutenga kubusa kumene unkaweta nkhosa+ kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga.+  Ine ndidzakhala nawe kulikonse kumene ungapite,+ ndipo ndidzagonjetsa adani ako onse pamaso pako.+ Ndidzachititsa kuti dzina lako lidziwike+ ngati mmene zimakhalira ndi anthu otchuka mʼdzikoli. 10  Anthu anga Aisiraeli ndidzawasankhira malo nʼkuwakhazika pamalowo. Iwo adzakhala pamenepo ndipo sadzasokonezedwanso. Anthu oipa sadzawaponderezanso ngati mmene ankachitira kale,+ 11  pa nthawi imene ndinasankha oweruza+ kuti azitsogolera anthu anga Aisiraeli. Ndidzachititsa kuti uzikhala mwamtendere osavutitsidwa ndi adani ako.+ Komanso Yehova wakuuza kuti, Yehova adzakukhazikitsira nyumba.*+ 12  Ukadzamwalira+ nʼkugona mʼmanda ndi makolo ako, ndidzachititsa kuti mbadwa* yako, mwana wako weniweni, akhale mfumu ndipo ndidzachititsa kuti ufumu wake ukhazikike.+ 13  Iye ndi amene adzamangire dzina langa nyumba,+ ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake wachifumu mpaka kalekale.+ 14  Ine ndidzakhala bambo ake ndipo iye adzakhala mwana wanga.+ Akalakwitsa zinthu zina, ine ndidzamudzudzula ndi ndodo ya anthu ndi zikoti za ana a anthu.*+ 15  Ndipo chikondi changa chokhulupirika sichidzachoka pa iye ngati mmene ndinachichotsera pa Sauli,+ amene ndinamʼchotsa pamaso pako. 16  Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhalapobe mpaka kalekale. Mpando wako wachifumu udzakhazikika mpaka kalekale.”’”+ 17  Natani anauza Davide mawu onsewa ndiponso masomphenya onse amene anaona.+ 18  Kenako Mfumu Davide anakhala pansi pamaso pa Yehova ndipo anati: “Ndine ndani ine, Yehova Ambuye Wamkulu Koposa? Ndipo banja lathu* nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndili pano?+ 19  Inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa, kuwonjezeranso pamenepa, mwanena kuti nyumba ya mtumiki wanu idzakhazikika mpaka mʼtsogolo kwambiri. Amenewa ndi malangizo* amene mwapereka kwa anthu onse, inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa. 20  Ndiyeno ine mtumiki wanu Davide ndinganenenso chiyani kwa inu pomwe mukundidziwa bwino kwambiri,+ inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa? 21  Inu mwachita zazikulu zonsezi chifukwa cha mawu anu komanso mogwirizana ndi zimene zili mumtima mwanu* ndipo mwandidziwitsa ine mtumiki wanu.+ 22  Nʼchifukwa chake ndinudi wodabwitsa,+ inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa. Palibe amene angafanane ndi inu+ komanso palibe Mulungu wina koma inu nokha.+ Zonse zimene tamva zikutsimikizira zimenezi. 23  Ndi mtundu uti padziko lapansi umene ungafanane ndi mtundu wa anthu anu Aisiraeli?+ Inu Mulungu munapita kukawawombola anthu anu+ ndipo munadzipangira dzina+ pamene munawachitira zinthu zazikulu ndi zochititsa mantha.+ Munathamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo chifukwa cha anthu anu amene munawawombola ku Iguputo. 24  Munachititsa Aisiraeli kuti akhale anthu anu mpaka kalekale.+ Ndipo inu Yehova mwakhala Mulungu wawo.+ 25  Choncho inu Yehova Mulungu, chitani zimene mwalonjeza zokhudza mtumiki wanu ndi nyumba yake ndipo muchite zimenezi mpaka kalekale. Muchite mogwirizana ndi zimene mwalonjeza.+ 26  Dzina lanu likwezeke mpaka kalekale+ kuti anthu anene kuti, ‘Yehova wa magulu ankhondo akumwamba ndi Mulungu wa Isiraeli,’ ndipo nyumba ya ine mtumiki wanu Davide ikhazikike pamaso panu.+ 27  Chifukwa inu Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, mwandiululira ine mtumiki wanu kuti, ‘Ndidzakumangira nyumba.’*+ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera kwa inu pempheroli. 28  Inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa, ndinu Mulungu woona ndipo mawu anu ndi oona,+ komanso mwandilonjeza ine mtumiki wanu zinthu zabwinozi. 29  Choncho dalitsani nyumba ya mtumiki wanu kuti ikhazikike pamaso panu mpaka kalekale.+ Inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa mwalonjeza ndipo madalitso anu akhale panyumba ya mtumiki wanu mpaka kalekale.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mʼnyumba yake yachifumu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ana a Isiraeli.”
Kapena kuti, “mzere wa mafumu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”
Mabaibulo ena amati “ana a Adamu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “nyumba yanga.”
Kapena kuti, “malamulo.”
Kapena kuti, “mogwirizana ndi cholinga chanu.”
Kapena kuti, “mzere wa mafumu.”