Deuteronomo 29:1-29

  • Anachita pangano ndi Aisiraeli ku Mowabu (1-13)

  • Anawachenjeza kuti apewe kusamvera (14-29)

    • Zinthu zobisika, zinthu zoululidwa (29)

29  Awa ndi mawu a pangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisiraeli mʼdziko la Mowabu, kuwonjezera pa pangano limene anachita nawo ku Horebe.+  Choncho Mose anaitana Aisiraeli onse nʼkuwauza kuti: “Inu munaona ndi maso anu mʼdziko la Iguputo zonse zimene Yehova anachitira Farao, atumiki ake onse ndi dziko lake lonse,+  ziweruzo zamphamvu zimene* maso anu anaona, kapena kuti zizindikiro zazikulu komanso zodabwitsa.+  Koma Yehova sanakupatseni mtima woti muthe kumvetsa zinthu, maso oti muthe kuona ndi makutu oti muthe kumva, mpaka lero.+  ‘Pamene ndinkakutsogolerani kwa zaka 40 mʼchipululu,+ zovala zanu sizinathe ndiponso nsapato zanu sizinathe kumapazi anu.+  Simunadye mkate, simunamwe vinyo kapena zakumwa zina zoledzeretsa, kuti mudziwe kuti ine ndine Yehova Mulungu wanu.’  Ndiyeno munafika pamalo ano, ndipo Sihoni mfumu ya Hesiboni+ ndi Ogi mfumu ya Basana+ anabwera kudzamenyana nafe, koma tinawagonjetsa.+  Kenako tinatenga dziko lawo nʼkulipereka ngati cholowa kwa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi hafu ya fuko la Manase.+  Choncho muzisunga mawu a pangano ili komanso kuwamvera kuti zonse zimene muzichita zizikuyenderani bwino.+ 10  Nonsenu mwaima pano lero pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu atsogoleri a mafuko, akulu anu, atsogoleri anu, mwamuna aliyense wa mu Isiraeli, 11  ana anu, akazi anu,+ mlendo+ amene akukhala mumsasa wanu, kuyambira amene amakutolerani nkhuni mpaka amene amakutungirani madzi. 12  Inu muli pano kuti mulumbire nʼkuchita pangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova Mulungu wanu akuchita nanu lero.+ 13  Cholinga chake nʼchakuti lero akupangeni kuti mukhale anthu ake+ komanso kuti iye akhale Mulungu wanu,+ mogwirizana ndi zimene anakulonjezani ndiponso mogwirizana ndi zimene analumbira kwa makolo anu, Abulahamu,+ Isaki+ ndi Yakobo.+ 14  Tsopano sindikuchita pangano ili komanso kulumbiritsa inu nokha ayi, 15  koma ndikuchitanso zimenezi ndi anthu amene aimirira ndi ife pano lero pamaso pa Yehova Mulungu wathu, komanso ndi anthu amene sitili nawo pano lero. 16  (Pakuti inu mukudziwa bwino mmene tinkakhalira mʼdziko la Iguputo komanso mmene tinadutsira pakati pa anthu a mitundu ina pa ulendo wathuwu.+ 17  Inu munkaona zinthu zawo zonyansa ndi mafano awo onyansa*+ amtengo ndi amwala, asiliva ndi agolide amene anali pakati pawo.) 18  Samalani kuti pakati panu lero pasapezeke mwamuna, mkazi, banja kapena fuko limene mtima wake wapatuka kusiya Yehova Mulungu wathu nʼkupita kukatumikira milungu ya mitundu inayo,+ kuti pakati panu pasapezeke muzu wotulutsa chipatso chapoizoni komanso chitsamba chowawa.+ 19  Koma ngati wina wamva mawu a lumbiro ili nʼkulankhula modzitama mumtima mwake kuti, ‘Ndikhala ndi mtendere ngakhale kuti ndikuyendabe motsatira zofuna za mtima wanga,’ zimene zidzachititse kuti aliyense woyandikana naye* awonongedwe, 20  Yehova sadzafuna kukhululukira munthu woteroyo.+ Mʼmalomwake, mkwiyo waukulu wa Yehova udzamuyakira, ndipo matemberero onse amene alembedwa mʼbuku ili adzamugwera,+ ndipo Yehova adzachotseratu dzina la munthuyo pansi pa thambo. 21  Kenako Yehova adzamupatula pa mafuko onse a Isiraeli kuti amubweretsere tsoka, mogwirizana ndi matemberero onse amene adzagwere anthu ophwanya pangano limene lalembedwa mʼbuku la Chilamulo ili. 22  Mʼbadwo wa mʼtsogolo wa ana anu ndiponso mlendo wochokera kudziko lakutali, akadzaona miliri ndi matenda amene Yehova wabweretsa mʼdzikoli—* 23  akadzaona kuti dziko lonse lawonongedwa ndi sulufule, mchere ndi kutentha, moti mʼdzikomo simungadzalidwe mbewu, simungaphuke kalikonse ndipo simungamere chomera chilichonse, ndipo likuoneka ngati Sodomu ndi Gomora,+ Adima ndi Zeboyimu,+ mizinda imene Yehova anaiwononga ndi ukali komanso mkwiyo wake—* 24  ana anu ndi alendo komanso mitundu yonse adzanena kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachitira dzikoli zimenezi?+ Nʼchiyani chachititsa kuti mkwiyo wake uyake kwambiri chonchi?’ 25  Ndiyeno iwo adzanena kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti anaphwanya pangano la Yehova,+ Mulungu wa makolo awo, limene anapangana nawo pamene ankawatulutsa mʼdziko la Iguputo.+ 26  Koma iwo anapita kukatumikira milungu ina ndi kuigwadira, milungu imene sankaidziwa komanso imene sanawalole kuti aziilambira.+ 27  Zitatero mkwiyo wa Yehova unayakira dziko limeneli ndipo analibweretsera matemberero onse amene analembedwa mʼbuku ili.+ 28  Choncho Yehova anawazula mʼdziko lawo atapsa mtima,+ ali ndi ukali ndiponso mkwiyo waukulu nʼkuwapititsa kudziko lina, kumene ali lero.’+ 29  Yehova Mulungu wathu+ amadziwa zinthu zonse zobisika, koma amaulula zinthu kwa ifeyo komanso kwa zidzukulu zathu ku mibadwomibadwo, kuti titsatire mawu onse a Chilamulo ichi.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mayesero amphamvu amene.”
Mawu a Chiheberi ali ndi tanthauzo lofanana ndi mawu akuti “ndowe” ndipo amagwiritsidwa ntchito posonyeza kuipidwa.
Mʼchilankhulo choyambirira, “kuti wothiriridwa bwino limodzi ndi wouma.”
Kamzere kameneka kakusonyeza kuti mawuwa anathera mʼmalere.
Kamzere kameneka kakusonyeza kuti mawuwa anathera mʼmalere.