Deuteronomo 31:1-30

  • Mose anali atatsala pangʼono kumwalira (1-8)

  • Kuwerenga Chilamulo pamaso pa anthu (9-13)

  • Yoswa anamuika kuti akhale mtsogoleri (14, 15)

  • Ananeneratu kuti Aisiraeli adzapandukira Mulungu (16-30)

    • Nyimbo yoti aphunzitse Aisiraeli (19, 22, 30)

31  Kenako Mose anapita kukauza Aisiraeli onse mawu awa,  kuti: “Tsopano ndili ndi zaka 120.+ Sindingathenso kukutsogolerani* chifukwa Yehova wandiuza kuti, ‘Suwoloka Yorodano uyu.’+  Yehova Mulungu wanu akuwoloka patsogolo panu kuti akutsogolereni. Iye adzawononga mitundu imeneyi pamaso panu ndipo inu mudzaithamangitsa.+ Yoswa ndi amene akutsogolereni nʼkukuwolotsani,+ mogwirizana ndi zimene Yehova wanena.  Yehova adzachitira mitundu imeneyi zimene anachitira Sihoni+ ndi Ogi,+ mafumu a Aamori, ndiponso zimene anachitira dziko lawo pamene anawawononga.+  Yehova adzakugonjetserani mitundu imeneyi, ndipo mudzaichitire mogwirizana ndi malamulo onse amene ndakupatsani.+  Limbani mtima ndipo muchite zinthu mwamphamvu.+ Musawaope kapena kuchita nawo mantha,+ chifukwa Yehova Mulungu wanu ndi amene akuyenda patsogolo panu. Iye sadzakutayani kapena kukusiyani ngakhale pangʼono.”+  Kenako Mose anaitana Yoswa nʼkumuuza pamaso pa Aisiraeli onse kuti: “Limba mtima ndipo uchite zinthu mwamphamvu,+ chifukwa iwe ndi amene udzalowetse anthu awa mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo awo kuti adzawapatsa. Ndipo iwe ndi amene udzawagawire dzikolo kuti likhale cholowa chawo.+  Yehova ndi amene akuyenda patsogolo panu ndipo apitiriza kuyenda nanu.+ Sadzakutayani kapena kukusiyani ngakhale pangʼono. Choncho musaope kapena kuchita mantha.”+  Kenako Mose analemba Chilamulo+ chimenechi nʼkuchipereka kwa ansembe, omwe ndi Alevi, amene amanyamula likasa la pangano la Yehova, komanso kwa akulu onse a Isiraeli. 10  Ndiyeno Mose anawalamula kuti: “Kumapeto kwa zaka 7 zilizonse, pa nthawi imene inaikidwiratu mʼchaka choti anthu angongole amasuke,+ Pachikondwerero cha Misasa,+ 11  Aisiraeli onse akabwera pamaso pa Yehova+ Mulungu wanu pamalo amene iye adzasankhe, muzidzawerenga Chilamulo ichi pamaso pa Aisiraeli onse kuti achimve.+ 12  Sonkhanitsani anthu,+ amuna, akazi, ana ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu,* kuti amvetsere komanso kuti aphunzire zokhudza Yehova Mulungu wanu, kuti azimuopa ndiponso kuti azitsatira mosamala mawu onse a mʼChilamulo ichi. 13  Akatero ana awo amene sakudziwa Chilamulo ichi adzamvetsera+ ndipo adzaphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu, masiku onse amene mudzakhale mʼdziko limene mukuwoloka Yorodano kukalitenga kuti likhale lanu.”+ 14  Kenako Yehova anauza Mose kuti: “Taona, nthawi yoti ufe yayandikira.+ Itana Yoswa, ndipo mukaime pachihema chokumanako kuti ndikamuike kukhala mtsogoleri.”+ Choncho Mose ndi Yoswa anapita nʼkukaima pachihema chokumanako. 15  Ndiyeno Yehova anaonekera kuchihemako mʼchipilala cha mtambo chimene chinaima pafupi ndi khomo la chihema.+ 16  Tsopano Yehova anauza Mose kuti: “Iweyo watsala pangʼono kufa,* ndipo anthu awa adzakhala osakhulupirika kwa ine ndipo adzayamba kulambira milungu yachilendo imene ili mʼdziko limene akupita.+ Iwo adzandisiya+ nʼkuphwanya pangano limene ndinapangana nawo.+ 17  Pa nthawi imeneyo mkwiyo wanga udzawayakira+ ndipo ndidzawasiya+ nʼkuwabisira nkhope yanga+ mpaka atawonongedwa.+ Ndiyeno akadzakumana ndi masoka komanso mavuto ambiri adzanena kuti, ‘Masoka amenewatu akutigwera chifukwa chakuti Mulungu wathu sali pakati pathu.’+ 18  Koma ine ndidzapitiriza kuwabisira nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoipa zonse zimene achita, potembenukira kwa milungu ina.+ 19  Tsopano mulembe nyimbo iyi+ nʼkuphunzitsa Aisiraeli.+ Muwaphunzitse* nyimbo imeneyi kuti ikhale mboni yanga pamaso pa Aisiraeliwo.+ 20  Ndikadzawalowetsa mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo awo,+ dziko loyenda mkaka ndi uchi,+ ndipo akadzadya nʼkukhuta, zinthu nʼkuyamba kuwayendera bwino,*+ adzatembenukira kwa milungu ina nʼkuyamba kuitumikira. Iwo adzandichitira mwano komanso kuphwanya pangano langa.+ 21  Ndiyeno akadzakumana ndi masoka komanso mavuto ambiri,+ nyimboyi idzawakumbutsa zimene ndinawachenjeza, (chifukwa mbadwa zawo sizikuyenera kuiwala nyimboyi), chifukwa ndikudziwa kale mtima umene ayamba kukhala nawo+ ndisanawalowetse nʼkomwe mʼdziko limene ndinawalumbirira.” 22  Choncho Mose analemba nyimboyi pa tsiku limenelo nʼkuphunzitsa Aisiraeli. 23  Ndiyeno Mulungu anaika Yoswa+ mwana wa Nuni kuti akhale mtsogoleri, ndipo anamuuza kuti: “Limba mtima ndipo uchite zinthu mwamphamvu,+ chifukwa iwe ndi amene udzalowetse Aisiraeli mʼdziko limene ndawalumbirira,+ ndipo ine ndidzapitiriza kukhala ndi iwe.” 24  Mose atangomaliza kulemba mawu onse a Chilamulo ichi mʼbuku,+ 25  Mose analamula Alevi amene amanyamula likasa la pangano la Yehova kuti: 26  “Tengani buku ili la Chilamulo+ ndipo muliike pambali pa likasa+ la pangano la Yehova Mulungu wanu, ndipo lidzakhala mboni ya Mulungu yokutsutsani. 27  Ineyo ndikudziwa bwino khalidwe lanu lopanduka+ ndi kuuma mtima* kwanu.+ Ngati mwakhala mukupandukira Yehova pamene ndili moyo, ndiye kuli bwanji pambuyo pa imfa yanga! 28  Sonkhanitsani akulu onse a mafuko anu ndi atsogoleri anu, kuti amve mawu awa amene ndikufuna kulankhula nawo, ndipo nditenge kumwamba ndi dziko lapansi kuti zikhale mboni zanga pamaso pawo.+ 29  Chifukwa ndikudziwa bwino kuti pambuyo pa imfa yanga, mosakayikira mudzachita zinthu zoipa+ nʼkupatuka kusiya njira imene ndakulamulani. Ndiyeno pamapeto pake tsoka lidzakugwerani,+ chifukwa mudzachita zoipa pamaso pa Yehova ndipo mudzamukhumudwitsa ndi ntchito za manja anu.” 30  Choncho mpingo wonse wa Isiraeli ukumva, Mose anayamba kulankhula mawu a nyimbo iyi, kuchokera poyambirira mpaka kumapeto kuti:+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “kutuluka ndi kulowa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmageti anu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “kugona pamodzi ndi makolo ako.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Muiike mʼkamwa mwawo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “nʼkunenepa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “kuuma khosi.”