Deuteronomo 32:1-52

  • Nyimbo ya Mose (1-47)

    • Yehova ndi Thanthwe (4)

    • Aisiraeli anaiwala Thanthwe lawo (18)

    • “Kubwezera ndi kwanga” (35)

    • “Inu anthu a mitundu ina, sangalalani limodzi ndi anthu ake” (43)

  • Mose akafera mʼphiri la Nebo (48-52)

32  “Tamverani kumwamba inu, ndipo ine ndilankhula,Dziko lapansi limve mawu a pakamwa panga.   Malangizo anga adzagwa ngati mvula,Mawu anga adzatsika ngati mame,Ngati mvula yowaza pa udzu,Ngatinso mvula yamphamvu pazomera.   Chifukwa ndidzalengeza dzina la Yehova.+ Anthu inu, lengezani za ukulu wa Mulungu wathu!+   Iye ndi Thanthwe, ndipo ntchito yake ndi yangwiro,+Njira zake zonse ndi zolungama.+ Mulungu wokhulupirika,+ amene sachita zinthu zopanda chilungamo.+Iye ndi wolungama ndi wowongoka.+   Iwo ndi amene achita zinthu zoipa.+ Iwo si ana ake, ali ndi vuto ndi iwowo.+ Iwo ndi mʼbadwo wopotoka maganizo komanso wachinyengo!+   Kodi Yehova mukuyenera kumuchitira zimenezi,+Anthu opusa ndi opanda nzeru inu?+ Kodi iye si Atate wanu amene anakulengani,+Amene anakupangani ndi kukukhazikitsani monga mtundu?   Kumbukirani masiku akale,Ganizirani zaka za mibadwo ya mʼmbuyo. Funsani bambo anu ndipo akuuzani,+Amuna achikulire pakati panu, ndipo akufotokozerani.   Pamene Wamʼmwambamwamba anapereka cholowa ku mitundu ya anthu,+Pamene analekanitsa ana a Adamu,*+Anaika malire a anthu ena onse+Poganizira chiwerengero cha ana a Isiraeli.+   Pakuti anthu a Yehova ndi gawo lake.+Yakobo ndiye cholowa chake.+ 10  Anamupeza mʼdziko lachipululu,+Mʼchipululu chopanda kanthu, molira zilombo.+ Anamuzungulira kuti amuteteze, anamusamalira,+Ndipo anamuteteza ngati mwana wa diso lake.+ 11  Monga mmene chiwombankhanga chimagwedezera chisa chake,Mmene chimaulukira pamwamba pa ana ake,Mmene chimatambasulira mapiko ake, kuti chitenge anawo,Nʼkuwanyamula pamapiko ake,+ 12  Ndi Yehova yekha amene anapitiriza kumutsogolera,*+Panalibe mulungu wachilendo amene anali naye.+ 13  Anamuyendetsa pamapiri a dziko lapansi,+Moti anadya zokolola za mʼmunda.+ Anamudyetsa uchi wochokera mʼthanthwe,Ndi mafuta ochokera mʼmwala wa nsangalabwi. 14  Anamudyetsanso mafuta a mkaka wa ngʼombe ndi mkaka wa nkhosa,Pamodzi ndi nkhosa zabwino kwambiri,*Komanso nkhosa zamphongo za ku Basana ndi mbuzi zamphongo,Pamodzi ndi tirigu wabwino koposa.*+Ndipo munamwa vinyo wochokera mʼmagazi a mphesa.* 15  Yesuruni* atanenepa, anapandukira mbuye wake. Iwe wanenepa, wakula thupi, wakhuta mopitirira muyezo.+ Choncho iye anasiya Mulungu amene anamupanga,+Ndipo ananyoza Thanthwe la chipulumutso chake. 16  Anamukwiyitsa ndi milungu yachilendo.+Ankamukhumudwitsa ndi zinthu zonyansa.+ 17  Iwo ankapereka nsembe kwa ziwanda, osati kwa Mulungu.+Anapereka nsembe kwa milungu imene sankaidziwa,Kwa milungu yatsopano yongobwera kumene,Komanso kwa milungu imene makolo anu sankaidziwa. 18  Munaiwala Thanthwe+ limene linakuberekani,Ndipo simunakumbukire Mulungu amene anakuberekani.+ 19  Yehova ataona zimenezi anawakana+Chifukwa chakuti ana ake aamuna ndi aakazi anamukhumudwitsa. 20  Choncho iye anati, ‘Ndiwabisira nkhope yanga,+Ndione kuti ziwathera bwanji. Chifukwa iwo ndi mʼbadwo wokonda zoipa,+Ana osakhulupirika.+ 21  Iwo andikwiyitsa* ndi milungu yabodza.+Andikhumudwitsa ndi mafano awo opanda pake.+ Choncho ine ndiwachititsa nsanje ndi anthu opanda pake,+Ndiwakhumudwitsa ndi mtundu wopusa.+ 22  Mkwiyo wanga wayatsa moto+Umene udzayaka mpaka kukafika pansi penipeni pa Manda,*+Ndipo udzapsereza dziko lapansi ndi zokolola zake,Komanso udzayatsa maziko a mapiri. 23  Ndidzawonjezera masoka awo,Mivi yanga yonse ndidzaigwiritsa ntchito pa iwo. 24  Adzalefuka ndi njala+Ndipo adzavutika ndi kutentha thupi koopsa komanso adzawonongedwa nʼkutheratu.+ Ndidzawatumizira zilombo za mano ataliatali+Komanso njoka zapoizoni za mʼfumbi. 25  Kunja, lupanga lidzawasandutsa anamfedwa.+Mʼnyumba, anthu adzagwidwa ndi mantha+Zimenezi zidzachitikira mnyamata, namwali,Mwana wamngʼono ndi munthu wa imvi.+ 26  Ndikanatha kunena kuti: “Ndidzawabalalitsa,Ndidzachititsa kuti anthu asakumbukirenso za iwo,” 27  Koma ndinkaopa zimene mdani anganene,+Chifukwa adaniwo angaganize molakwika.+ Iwo anganene kuti: “Tapambana chifukwa cha mphamvu zathu,+Si Yehova amene wachita zonsezi.” 28  Chifukwa iwo ndi mtundu wopanda nzeru,*Ndipo ndi osazindikira.+ 29  Zikanakhala bwino ngati akanakhala anzeru,+ chifukwa akanaganizira mozama zimenezi.+ Akanaganizira kuti ziwathera bwanji.+ 30  Kodi munthu mmodzi angathamangitse bwanji anthu 1,000,Kapena anthu awiri angathamangitse bwanji anthu 10,000?+ Nʼzosatheka, pokhapokha Thanthwe lawo litawagulitsa,+Komanso ngati Yehova atawapereka. 31  Chifukwa thanthwe lawo si lofanana ndi Thanthwe lathu,+Ndipo adani athu akudziwa bwino zimenezi.+ 32  Mtengo wawo wa mpesa ndi wochokera ku mtengo wa mpesa wa ku Sodomu,Ndi kuminda ya mʼmapiri a ku Gomora.+ Zipatso zawo za mphesa ndi zapoizoniNdipo ndi zowawa.+ 33  Vinyo wawo ndi poizoni wa njoka,Ndi poizoni woopsa wa mamba. 34  Kodi ine sindinasunge zimenezi,Nʼkuziikira chidindo mʼnyumba yanga yosungira zinthu?+ 35  Kubwezera ndi kwanga, chilangonso ndi changa.+Zimenezi zidzachitika pa nthawi yoikidwiratu phazi lawo likadzaterereka,+Chifukwa tsiku la tsoka lawo layandikira,Ndipo zowagwera zifika mofulumira.’ 36  Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,+Ndipo adzamvera chisoni atumiki ake+Akadzaona kuti mphamvu zawo zatha,Komanso kuti kwangotsala anthu ovutika ndi ofooka. 37  Ndiyeno iye adzanena kuti, ‘Ili kuti milungu yawo,+Thanthwe limene anathawirako, 38  Milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo,*Ndi kumwa vinyo wa nsembe zawo zachakumwa?+ Ibwere kudzakuthandizani. Ikhale malo anu othawirako. 39  Onani tsopano kuti ndine Mulungu,+Ndipo palibe Mulungu wina koma ine ndekha.+ Ndimapha komanso ndimapereka moyo.+ Ndimavulaza,+ ndipo ndidzachiritsa,+Palibe aliyense amene angapulumutse munthu mʼdzanja langa.+ 40  Ndakweza dzanja langa kumwambaNdipo ndikulumbira kuti: “Ine, Mulungu wamuyaya, ndikulumbira pa dzina langa,”+ 41  Ndikanola lupanga langa lonyezimira,Nʼkukonzekeretsa dzanja langa kuti lipereke chiweruzo,+Ndidzabwezera adani anga,+Ndipo ndidzapereka chilango kwa amene amadana nane. 42  Ndidzaledzeretsa mivi yanga ndi magazi,Ndipo lupanga langa lidzadya nyama,Ndi magazi a anthu ophedwa komanso ogwidwa,Ndiponso mitu ya atsogoleri a adani.’ 43  Inu anthu a mitundu ina, sangalalani limodzi ndi anthu ake,+Chifukwa adzabwezera magazi a atumiki ake,+Ndipo adzabwezera chilango kwa adani ake,+Komanso adzaphimba machimo a dziko la anthu ake.”* 44  Ndiyeno Mose anabwera nʼkulankhula mawu onse a nyimbo iyi anthu onse akumva,+ iye pamodzi ndi Hoshiya*+ mwana wa Nuni. 45  Mose atamaliza kulankhula mawu onsewa kwa Aisiraeli onse, 46  anawauza kuti: “Ganizirani mofatsa mawu onse okuchenjezani amene ndikulankhula nanu lero,+ kuti muuze ana anu kuti azionetsetsa kuti akuchita zimene mawu onse a Chilamulo ichi akunena.+ 47  Chifukwa amenewa si mawu opanda pake kwa inu, koma angakuthandizeni kukhala ndi moyo.+ Mukamatsatira mawu amenewa mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukuwoloka Yorodano kuti mukalitenge kukhala lanu.” 48  Yehova analankhula ndi Mose pa tsiku lomweli kuti: 49  “Kwera mʼphiri ili la Abarimu,+ phiri la Nebo,+ limene lili mʼdziko la Mowabu, moyangʼanizana ndi Yeriko, ndipo uone dziko la Kanani limene ndikupereka kwa Aisiraeli kuti likhale lawo.+ 50  Kenako ukafera paphiri limene ukufuna kukwerali nʼkuikidwa mʼmanda ngati mmene anachitira ndi makolo ako,* mofanana ndi Aroni mʼbale wako amene anafera paphiri la Hora+ nʼkuikidwa mʼmanda ngati mmene anachitira ndi makolo ake. 51  Izi zili choncho chifukwa awirinu simunakhale okhulupirika kwa ine pakati pa Aisiraeli kumadzi a pa Meriba+ ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini, chifukwa simunandilemekeze pamaso pa Aisiraeli.+ 52  Iwe udzaona dzikolo uli patali, koma sudzalowa mʼdziko limene ndikupereka kwa Aisiraeli.”+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “mitundu ya anthu.”
Apa akunena Yakobo.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mafuta a nkhosa zamphongo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mafuta apaimpso a tirigu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “madzi a zipatso za mphesa.”
Kutanthauza “Wolungama.” Limeneli ndi dzina laulemu la Isiraeli.
Kapena kuti, “anandichititsa nsanje.”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Mabaibulo ena amati, “wosafuna kumva malangizo.”
Kapena kuti, “imene inkadya nsembe zawo zabwino kwambiri.”
Kapena kuti, “adzayeretsa dziko la anthu ake.”
Dzina lakale la Yoswa. Hoshiya ndi chidule cha dzina lakuti Hoshaiya limene limatanthauza kuti, “Wopulumutsidwa ndi Ya; Ya Wapulumutsa.”
Awa ndi mawu okuluwika otanthauza imfa.