Deuteronomo 34:1-12
34 Kenako Mose anachoka mʼchipululu cha Mowabu kupita mʼphiri la Nebo,+ pamwamba pa Pisiga,+ moyangʼanizana ndi Yeriko.+ Ndipo Yehova anamuonetsa dziko lonse, kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.+
2 Anamuonetsanso dziko lonse la Nafitali, dziko la Efuraimu, dziko la Manase komanso dziko lonse la Yuda mpaka kunyanja yakumadzulo.*+
3 Anamuonetsa Negebu+ ndi Chigawo+ cha Yorodano kuphatikizapo chigwa cha Yeriko, mzinda wa mitengo ya kanjedza, mpaka ku Zowari.+
4 Ndiyeno Yehova anamuuza kuti: “Ili ndi dziko limene ndinalumbira kwa Abulahamu, Isaki ndi Yakobo kuti, ‘Ndidzalipereka kwa mbadwa* zanu.’+ Ndakulola kuti ulione ndi maso ako, koma suwoloka kukalowa mʼdzikolo.”+
5 Kenako Mose mtumiki wa Yehova anafera pamenepo mʼdziko la Mowabu, mogwirizana ndi zimene Yehova ananena.+
6 Mulungu anamuika mʼmanda mʼchigwa, mʼdziko la Mowabu moyangʼanizana ndi Beti-peori, ndipo palibe amene akudziwa pamene pali manda ake mpaka lero.+
7 Mose anamwalira ali ndi zaka 120.+ Pa nthawiyo maso ake ankaonabe bwinobwino ndipo anali adakali ndi mphamvu.
8 Aisiraeli analira maliro a Mose kwa masiku 30 mʼchipululu cha Mowabu.+ Kenako masiku onse olira maliro a Mose anatha.
9 Yoswa mwana wa Nuni anali atadzazidwa ndi mzimu wa nzeru, chifukwa Mose anaika manja ake pa iye.+ Aisiraeli anayamba kumumvera ndipo anachita mogwirizana ndi zomwe Yehova analamula Mose.+
10 Koma mu Isiraeli simunakhalenso mneneri aliyense wofanana ndi Mose,+ amene Yehova ankamudziwa bwino kwambiri.*+
11 Iye anachita zizindikiro ndi zodabwitsa zonse zimene Yehova anamutuma kukachita mʼdziko la Iguputo kwa Farao, atumiki ake onse ndi mʼdziko lake lonse.+
12 Mose anachita zimenezi ndi dzanja lamphamvu komanso mphamvu zazikulu pamaso pa Aisiraeli onse.+