Ezekieli 10:1-22

  • Anatenga moto kuchokera pakati pa mawilo (1-8)

  • Anafotokoza zokhudza akerubi komanso mawilo (9-17)

  • Ulemerero wa Yehova unachoka pakachisi (18-22)

10  Pamene ndinkaona masomphenyawo, ndinaona kuti pamwamba pa thambo limene linali pamwamba pa mitu ya akerubi, panali chinachake chooneka ngati mwala wa safiro. Chinthucho chinkaoneka ngati mpando wachifumu.+  Kenako Mulungu anauza munthu amene anavala zovala zansalu uja+ kuti: “Pita pakati pa mawilo,+ pansi pa akerubi. Ukatengepo makala amoto+ odzaza manja ako onse awiri kuchokera pakati pa akerubiwo, ndipo ukawaponye pamzindawo.”+ Choncho iye anapitadi ine ndikuona.  Pamene munthuyo anapita pakati pawo, akerubiwo anali ataima mbali yakumanja kwa nyumba yopatulika ndipo mtambo unadzaza bwalo lonse lamkati.  Ndiyeno ulemerero wa Yehova+ unachoka pa akerubi nʼkupita pakhomo la nyumba yopatulika ndipo mtambo unayamba kudzaza nyumbayo pangʼonopangʼono.+ Komanso ulemerero wowala wa Yehova unadzaza mʼbwalo lonse la nyumbayo.  Phokoso la mapiko a akerubiwo linkamveka mʼbwalo lakunja ndipo linkamveka ngati mmene mawu a Mulungu Wamphamvuyonse amamvekera akamalankhula.+  Kenako Mulungu analamula munthu amene anavala zovala zansalu uja kuti: “Tenga moto pakati pa mawilo, pakati pa akerubi.” Ndipo munthuyo anapita nʼkukaima pambali pa wilo.  Ndiyeno mmodzi wa akerubiwo anatambasulira dzanja lake pamoto umene unali pakati pa akerubiwo.+ Iye anatenga motowo pangʼono nʼkuuika mʼmanja mwa munthu amene anavala zovala zansalu uja+ ndipo munthuyo anautenga nʼkuchoka.  Pansi pa mapiko a akerubiwo panali chinachake chooneka ngati manja a munthu.+  Pamene ndinkaona masomphenyawo, ndinaona kuti pambali pa akerubiwo panali mawilo 4. Pambali pa kerubi aliyense panali wilo limodzi ndipo mawilowo ankaoneka kuti akuwala ngati mwala wa kulusolito.+ 10  Mawilo 4 onsewo ankaoneka mofanana. Ankaoneka ngati wilo lina lili pakati pa wilo linzake. 11  Mawilowo akamayenda ankatha kulowera kumbali iliyonse pa mbali zonse 4 popanda kutembenuka chifukwa ankatha kupita kumene mitu ya akerubiwo yayangʼana popanda kutembenuka. 12  Mʼmatupi onse a akerubiwo, kumsana kwawo, mʼmanja mwawo, mʼmapiko awo ndiponso mʼmawilo a akerubi onse 4 munali maso paliponse.+ 13  Kenako ndinamva mawu akuitana mawilowo kuti, “Mawilo inu!” 14  Kerubi aliyense anali ndi nkhope 4. Nkhope yoyamba inali ya kerubi. Nkhope yachiwiri inali ya munthu. Nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope ya 4 inali ya chiwombankhanga.+ 15  Akerubiwo anali angelo omwe aja amene ndinawaona kumtsinje wa Kebara.+ Akerubiwo akanyamuka kukwera mʼmwamba 16  kapena akamayenda, mawilo aja ankayenda nawo limodzi ali pambali pawo. Akerubiwo akakweza mapiko awo kuti akwere mʼmwamba, mawilowo sankatembenuka kapena kuchoka pambali pawo.+ 17  Akerubiwo akaima, mawilonso ankaima. Akerubiwo akakwera mʼmwamba, mawilonso ankakwera nawo limodzi, chifukwa mzimu womwe unkatsogolera angelowo unkatsogoleranso mawilowo. 18  Kenako ulemerero wa Yehova+ unachoka pakhomo la nyumba yopatulika nʼkukaima pamwamba pa akerubiwo.+ 19  Tsopano akerubi aja anakweza mʼmwamba mapiko awo nʼkunyamuka kuchoka pansi ine ndikuona. Pamene amanyamuka, mawilo aja anali pambali pawo. Kenako iwo anakaima pakhomo lakumʼmawa la geti la nyumba ya Yehova ndipo ulemerero wa Mulungu wa Isiraeli unali pamwamba pawo.+ 20  Amenewa anali angelo amene ndinawaona pansi pa mpando wachifumu wa Mulungu wa Isiraeli kumtsinje wa Kebara,+ choncho ndinadziwa kuti anali akerubi. 21  Angelo onse 4 anali ndi nkhope 4 komanso mapiko 4. Ndipo pansi pa mapiko awo panali chinachake chooneka ngati manja a munthu.+ 22  Maonekedwe a nkhope zawo anali ofanana ndi a nkhope zimene ndinaziona mʼmphepete mwa mtsinje wa Kebara.+ Mngelo aliyense ankapita kutsogolo basi.+

Mawu a M'munsi