Ezekieli 11:1-25

  • Anadzudzula akalonga oipa (1-13)

    • Mzinda anauyerekezera ndi mphika (3-12)

  • Lonjezo lakubwezeretsa (14-21)

    • Kupatsidwa “mzimu watsopano” (19)

  • Ulemerero wa Mulungu unachoka mu Yerusalemu (22, 23)

  • Ezekieli anabwerera ku Kasidi mʼmasomphenya (24, 25)

11  Kenako mzimu unandinyamula nʼkupita nane kugeti la nyumba ya Yehova limene linayangʼana kumʼmawa.+ Pakhomo la getilo ndinaonapo amuna 25 omwe anali akalonga+ ndipo pakati pawo panali Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya.  Ndiyeno Mulungu anandiuza kuti: “Iwe mwana wa munthu, amuna amenewa ndi amene akukonza chiwembu ndiponso amene akupereka malangizo oipa mumzindawu.  Iwo akunena kuti: ‘Ino ndi nthawi yomanga nyumba.+ Mzindawu* uli ngati mphika*+ ndipo ifeyo tili ngati nyama mumphikamo.’  Choncho iweyo ulosere zinthu zoipa zimene zidzawachitikire. Losera, iwe mwana wa munthu.”+  Kenako mzimu wa Yehova unafika pa ine+ ndipo iye anandiuza kuti: “Unene kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Inu anthu a nyumba ya Isiraeli, zimene mwanena ndi zoona ndipo ine ndikudziwa zimene mukuganiza.  Inuyo mwachititsa kuti anthu ambiri afe mumzindawu ndipo mwadzaza misewu yake ndi anthu akufa.”’”+  “Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Anthu akufa amene mwawamwaza mumzindawu ndi amene ali nyama ndipo mzindawu ndi mphika.+ Koma inuyo mudzatulutsidwa mumzindawu.’”  “‘Inu mukuopa lupanga+ koma ine ndidzachititsa kuti muphedwe ndi lupanga,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.  ‘Ine ndidzakutulutsani mumzindawu nʼkukuperekani mʼmanja mwa anthu ochokera kudziko lina ndipo ndidzakulangani.+ 10  Mudzaphedwa ndi lupanga.+ Ndidzakuweruzirani mʼmalire a Isiraeli+ ndipo mudzadziwa kuti ine ndine Yehova.+ 11  Kwa inu, mzindawu sudzakhala mphika ndipo inuyo simudzakhala nyama mkati mwa mphikawo. Ndidzakuweruzirani mʼmalire a Isiraeli. 12  Inuyo mudzadziwa kuti ine ndine Yehova, chifukwa simunasunge malamulo anga ndiponso simunatsatire zigamulo zanga.+ Koma inu munatsatira zigamulo za mitundu ya anthu amene akuzungulirani.’”+ 13  Nditangomaliza kulosera, Pelatiya mwana wa Benaya anamwalira. Choncho ine ndinagwada nʼkuwerama mpaka nkhope yanga pansi, nʼkufuula kuti: “Mayo ine, inu Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa! Kodi mukufuna kuwononga Aisiraeli amene atsalawa?”+ 14  Yehova analankhulanso nane kuti: 15  “Iwe mwana wa munthu, abale ako enieni, azichimwene ako amene ali ndi ufulu wowombola, limodzi ndi nyumba yonse ya Isiraeli, auzidwa ndi anthu amene akukhala ku Yerusalemu kuti, ‘Pitani kutali ndi Yehova. Dzikoli ndi lathu. Laperekedwa kwa ife kuti likhale lathu.’ 16  Choncho uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ngakhale kuti ndawachotsa nʼkuwapititsa kutali kuti azikakhala pakati pa mitundu yosiyanasiyana ya anthu ndipo ndawabalalitsira mʼmayiko osiyanasiyana,+ ine ndidzakhala malo opatulika kwa iwo kwa kanthawi kochepa, kumayiko amene iwo apitako.”’”+ 17  Choncho uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Kuwonjezera pamenepo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kwa anthu a mitundu yosiyanasiyana ndiponso kuchokera mʼmayiko amene ndinakubalalitsiraniko ndipo ndidzakupatsani dziko la Isiraeli.+ 18  Iwo adzabwerera mʼdzikomo ndipo adzachotsamo mafano onse onyansa komanso adzasiya zinthu zonse zonyansa zimene amachita.+ 19  Ndidzawapatsa mtima umodzi+ ndipo ndidzaika mzimu watsopano mwa iwo.+ Ndidzachotsa mtima wamwala mʼmatupi awo+ nʼkuwapatsa mtima wamnofu,*+ 20  kuti azidzatsatira malamulo anga, azidzasunga komanso kumvera zigamulo zanga. Akadzatero adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo.”’ 21  “‘“Koma amene atsimikiza mumtima mwawo kuti apitirize kutsatira mafano awo onyansa komanso kuchita zinthu zonyansa, ndidzawabwezera mogwirizana ndi zochita zawo,” akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.’” 22  Ndiyeno akerubi aja anakweza mapiko awo mʼmwamba ndipo mawilo anali pambali pawo.+ Ulemerero wa Mulungu wa Isiraeli unali pamwamba pawo.+ 23  Kenako ulemerero wa Yehova+ unakwera mʼmwamba kuchoka mumzindawo nʼkukaima pamwamba pa phiri, kumʼmawa kwa mzindawo.+ 24  Ndiyeno mzimu unandinyamula nʼkukandisiya kudziko la Kasidi kumene kunali anthu ogwidwa ukapolo. Zimenezi zinachitika mʼmasomphenya amene ndinaona kudzera mwa mzimu wa Mulungu. Kenako masomphenya amene ndinaonawo anazimiririka. 25  Pambuyo pake, ndinayamba kuuza anthu amene anagwidwa ukapolowo zinthu zonse zimene Yehova anandionetsa.

Mawu a M'munsi

Umenewu ndi mzinda wa Yerusalemu umene Ayuda ankaona ngati azikhalamo motetezeka.
Kapena kuti, “mphika wakukamwa kwakukulu.”
Kutanthauza mtima wofuna kutsogoleredwa ndi Mulungu.