Ezekieli 14:1-23

  • Olambira mafano adzalangidwa (1-11)

  • Chiweruzo cha Yerusalemu nʼchosapeweka (12-23)

    • Nowa, Danieli ndi Yobu anali olungama (14, 20)

14  Ndiyeno ena mwa akuluakulu a Isiraeli anabwera nʼkudzakhala pamaso panga.+  Kenako Yehova anandiuza kuti:  “Iwe mwana wa munthu, amuna awa atsimikiza mumtima mwawo kuti azitsatira mafano awo onyansa,* ndipo aika chinthu chopunthwitsa chimene chimachititsa kuti anthu azichimwa. Kodi ndiwayankhe iwo akamandifunsa?+  Choncho ulankhule nawo ndipo uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ngati munthu aliyense mu Isiraeli watsimikiza mumtima mwake kuti azitsatira mafano ake onyansa nʼkuika chinthu chopunthwitsa chimene chachititsa kuti anthu achite tchimo kenako nʼkukafunsira kwa mneneri, ine Yehova ndidzamuyankha moyenera, mogwirizana ndi kuchuluka kwa mafano ake onyansa.  Ndidzachititsa mantha mitima ya anthu a nyumba ya Isiraeli,* chifukwa chakuti onsewo achoka kwa ine nʼkuyamba kutsatira mafano awo onyansawo.”’+  Choncho uza nyumba ya Isiraeli kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Bwererani, musiye kutsatira mafano anu onyansa ndipo musiye zinthu zonse zonyansa zimene mukuchita.+  Ngati munthu aliyense amene akukhala mu Isiraeli, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, wasiya kunditsatira ndipo watsimikiza mumtima mwake kuti azitsatira mafano ake onyansa nʼkuika chinthu chopunthwitsa chimene chachititsa kuti anthu achite tchimo kenako nʼkukafunsira kwa mneneri wanga,+ ine Yehova ndidzamuyankha ndekha.  Ine ndidzadana naye munthuyo nʼkumuika kuti akhale chenjezo ndi mwambi ndipo ndidzamupha kuti asakhalenso pakati pa anthu anga,+ moti mudzadziwa kuti ine ndine Yehova.”’  ‘Koma ngati mneneri wapusitsidwa nʼkupereka yankho, ineyo Yehova ndi amene ndapusitsa mneneriyo.+ Choncho ndidzatambasula dzanja langa nʼkumuwononga kuti asakhalenso pakati pa anthu anga, Aisiraeli. 10  Iwo adzakumana ndi zotsatira za zolakwa zawo. Zolakwa za munthu wofunsira kwa mneneri zidzakhala zofanana ndi za mneneriyo, 11  kuti a nyumba ya Isiraeli asadzasiyenso kunditsatira nʼkumangoyendayenda ndiponso kuti asiye kudziipitsa ndi zolakwa zawo zonse. Iwo adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.” 12  Yehova anandiuzanso kuti: 13  “Iwe mwana wa munthu, ngati dziko landichimwira pochita zosakhulupirika, ine ndidzatambasula dzanja langa nʼkuwononga njira zimene amapezera chakudya.*+ Choncho ndidzatumiza njala mʼdzikolo+ ndipo ndidzapha anthu ndi ziweto.”+ 14  “‘Ngakhale amuna atatu awa: Nowa,+ Danieli+ ndi Yobu,+ akanakhala mʼdzikolo, iwo okhawo akanatha kupulumutsa miyoyo yawo chifukwa chokhala olungama,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.” 15  “‘Kapena nditati ndichititse zilombo zolusa zakutchire kudutsa mʼdzikolo nʼkupha anthu ambiri, nʼkulichititsa kuti likhale bwinja popanda munthu aliyense wodutsamo chifukwa cha zilombo zolusazo,+ 16  pali ine Mulungu wamoyo,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, ‘ngakhale zikanakhala kuti amuna atatu amenewa ali mʼdzikolo, iwo sakanapulumutsa ana awo aamuna kapena aakazi. Iwo okhawo ndi amene akanapulumuka ndipo dzikolo likanakhala bwinja.’” 17  “‘Kapena nditati ndibweretse lupanga mʼdzikolo,+ nʼkunena kuti: “Mʼdzikolo mudutse lupanga,” ine nʼkuphamo anthu ndi ziweto,+ 18  pali ine Mulungu wamoyo, akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, ‘ngakhale zikanakhala kuti amuna atatu amenewa ali mʼdzikolo, iwo sakanapulumutsa ana awo aamuna kapena aakazi. Iwo okhawo ndi amene akanapulumuka.’” 19  “‘Kapenanso ngati nditatumiza mliri mʼdzikolo,+ nʼkulikhuthulira mkwiyo wanga pokhetsa magazi ambiri komanso kupha anthu ndi ziweto, 20  pali ine Mulungu wamoyo,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, ‘ngakhale zikanakhala kuti Nowa,+ Danieli+ ndi Yobu+ ali mʼdzikolo, iwo sakanapulumutsa ana awo aamuna kapena aakazi. Iwo okhawo ndi amene akanapulumuka chifukwa ndi olungama.’”+ 21  “Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Zidzakhalanso choncho ndikadzabweretsa zilango zanga* 4+ izi: lupanga, njala, zilombo zolusa zakutchire ndi mliri+ kuti zikaphe anthu ndi ziweto mu Yerusalemu.+ 22  Komabe anthu ena amene adzatsale mʼdzikolo adzathawa nʼkupulumuka ndipo adzatulutsidwamo,+ kuphatikizapo ana aamuna ndi aakazi. Iwo akubwera kwa inu, ndipo mukadzaona njira zawo ndi zochita zawo mudzatonthozedwa ndithu pambuyo pa tsoka limene ndinabweretsa pa Yerusalemu ndiponso pambuyo pa zonse zimene ndinachitira mzindawo. 23  Iwo adzakutonthozani mukadzaona njira zawo ndi zochita zawo. Ndipo mudzadziwa kuti zonse zimene ndinachitira mzindawo, sindinazichite popanda chifukwa,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”

Mawu a M'munsi

Mawu a Chiheberi ali ndi tanthauzo lofanana ndi mawu akuti “ndowe” ndipo amagwiritsidwa ntchito posonyeza kuipidwa.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndidzachititsa kuti mantha agwire mitima ya Aisiraeli.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ndidzathyola ndodo za mkate.” Nʼkutheka kuti akutanthauza ndodo zimene ankagwiritsira ntchito posunga mikate.
Kapena kuti, “ziweruzo zanga zowononga.”