Ezekieli 15:1-8
-
Yerusalemu ndi mtengo wa mpesa wopanda ntchito (1-8)
15 Yehova analankhulanso nane kuti:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wa mpesa umasiyana bwanji ndi mitengo ina yonse kapena nthambi ya mitengo yamʼnkhalango?
3 Kodi anthu amadula nthambi yake kuti ikhale mtengo wogwiritsa ntchito inayake? Kapena kodi angatenge kamtengo kake nʼkukakhomerera pakhoma kuti azikolowekapo ziwiya zosiyanasiyana?
4 Mtengowo umaponyedwa pamoto kuti ukhale nkhuni ndipo motowo umanyeketsa kutsinde ndi kunsonga kwake. Pakati pa mtengowo pamapsanso. Ndiye kodi ungagwire ntchito iliyonse?
5 Ngakhale pamene mtengowo unali wathunthu sukanagwiritsidwa ntchito iliyonse. Ndiye kuli bwanji ukapsa ndi moto nʼkunyeka, kodi ungagwirenso ntchito iliyonse?”
6 “Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Mofanana ndi mtengo wa mpesa womwe uli pakati pa mitengo yamʼnkhalango, umene ndaupereka kuti ukhale nkhuni, ndidzachitanso chimodzimodzi ndi anthu amene akukhala mu Yerusalemu.+
7 Anthuwo ndawayangʼana mokwiya. Iwo athawa moto, koma moto wina udzawapsereza. Ndipo ndikadzawayangʼana mokwiya, mudzadziwa kuti ine ndine Yehova.+
8 Dziko lawo ndidzalisandutsa bwinja+ chifukwa chakuti iwo achita zosakhulupirika,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”