Ezekieli 26:1-21

  • Ulosi wokhudza Turo (1-21)

    • “Malo oyanikapo makoka” (5, 14)

    • Miyala komanso dothi zinaponyedwa mʼmadzi (12)

26  Mʼchaka cha 11, pa tsiku loyamba la mwezi, Yehova analankhula nane kuti:  “Iwe mwana wa munthu, Turo wanena Yerusalemu+ kuti, ‘Eyaa! Zakhala bwino. Mzinda umene unkakopa anthu a mitundu ina wathyoledwa.+ Tsopano zinthu zindiyendera bwino ndipo ndilemera chifukwa mzindawo wawonongedwa.’  Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Ine ndikuukira iwe Turo ndipo ndikutumizira mayiko ambiri kuti adzamenyane nawe. Iwo adzabwera ngati mafunde amʼnyanja.  Mayikowo adzagwetsa mipanda ya Turo komanso kugumula nsanja zake.+ Ine ndidzapala dothi lake nʼkumusandutsa thanthwe losalala lopanda kanthu.  Iye adzakhala malo oyanikapo makoka pakati pa nyanja.’+ ‘Ine ndanena ndipo anthu a mitundu ina adzalanda zinthu zake,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.  ‘Anthu amʼmidzi yake imene ili* kunja kwa mzindawo adzaphedwa ndi lupanga ndipo anthu adzadziwa kuti ine ndine Yehova.’  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Ine ndikutumiza Nebukadinezara* mfumu ya Babulo, mfumu ya mafumu,+ kuchokera kumpoto+ kuti akaukire Turo. Iye adzapita ndi mahatchi,+ magaleta ankhondo,+ asilikali apamahatchi ndi gulu la asilikali ambiri.  Anthu omwe akukhala mʼmidzi yako imene ili kunja kwa mzindawu adzawapha ndi lupanga. Iye adzamanga mpanda womenyerapo nkhondo komanso malo okwera omenyerapo nkhondo kuti amenyane nawe ndipo adzakuukira ndi chishango chachikulu.  Mfumuyo idzagumula mpanda wako ndi chida chogumulira,* ndipo idzagwetsa nsanja zako pogwiritsa ntchito nkhwangwa zake.* 10  Mahatchi ake adzakhala ambiri moti adzakukwirira ndi fumbi. Phokoso la asilikali apamahatchi, mawilo ake ndi magaleta zidzachititsa kuti mpanda wako unjenjemere akamadzalowa pamageti ako ngati anthu amene akulowa mumzinda umene mpanda wake ndi wogumuka kuti augonjetse. 11  Ziboda za mahatchi ake zidzapondaponda mʼmisewu yako yonse.+ Iye adzapha anthu ako ndi lupanga ndipo zipilala zako zikuluzikulu zidzagwa. 12  Iwo adzakulanda chuma chako ndi malonda ako.+ Adzagwetsa mpanda wako ndi nyumba zako zabwino kwambiri. Kenako miyala yako, zinthu zako zamatabwa komanso dothi lako adzaziponya mʼmadzi.’ 13  ‘Ndidzathetsa phokoso la nyimbo zako ndipo phokoso la azeze ako silidzamvekanso.+ 14  Ndidzakusandutsa thanthwe losalala lopanda kanthu ndipo udzakhala malo oyanikapo makoka.+ Mzinda wako sudzamangidwanso chifukwa ine Yehova ndanena,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 15  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wauza mzinda wa Turo kuti: ‘Kodi zilumba sizidzagwedezeka chifukwa cha phokoso la kugwa kwako, kubuula kwa anthu amene avulazidwa koopsa* komanso chifukwa cha kuphedwa kwa anthu ako ambiri?+ 16  Akalonga* onse akunyanja adzatsika mʼmipando yawo yachifumu nʼkuvula mikanjo yawo* komanso zovala zawo za nsalu yopeta. Iwo azidzanjenjemera chifukwa cha mantha. Adzakhala padothi ndipo nthawi zonse azidzanjenjemera nʼkumakuyangʼanitsitsa modabwa.+ 17  Iwo adzakuimbira nyimbo yoimba polira.+ Azidzati: “Iwe mzinda wotamandika, zoona wawonongekadi!+ Mwa iwe munkakhala anthu ochokera kunyanja.Iwe ndi anthu ako munali amphamvu panyanja,+Munkachititsa mantha anthu onse okhala padziko lapansi. 18  Pa tsiku limene udzagwe, zilumba zidzanjenjemera,Zilumba zamʼnyanja zidzasokonezeka iweyo ukadzawonongedwa.”’+ 19  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Ndikadzakuwononga ngati mizinda imene simukukhala anthu, ndikadzakubweretsera madzi ambiri, ndipo madzi amphamvu akadzakumiza,+ 20  ndidzakutsitsira mʼdzenje* limodzi ndi anthu enanso amene akutsikira mʼmanda momwe muli anthu amene anafa kalekale. Ndidzakuchititsa kuti ukhale mʼmalo otsika kwambiri mofanana ndi malo ena akalekale amene anawonongedwa. Udzakhala kumeneko pamodzi ndi ena onse amene akutsikira kumanda+ kuti anthu asadzakhalenso mwa iwe. Kenako ndidzalemekeza* dziko la anthu amoyo. 21  Ndidzakugwetsera zoopsa modzidzimutsa ndipo sudzakhalaponso.+ Anthu adzakufunafuna koma sudzapezeka mpaka kalekale,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Ana ake aakazi amene ali.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Kapena kuti, “chida chake chankhondo.”
Kapena kuti, “malupanga ake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “anthu amene akufa.”
Kapena kuti, “Atsogoleri.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “malaya odula manja.”
Kapena kuti, “mʼmanda.”
Kapena kuti, “ndidzakongoletsa.”