Ezekieli 27:1-36

  • Nyimbo yoimba polira yokhudza sitima yapamadzi ya Turo imene ikumira (1-36)

27  Yehova analankhulanso nane kuti:  “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yoimba polira yokhudza Turo.+  Uimbire Turo kuti,‘Iwe amene ukukhala polowera mʼnyanja,Iwe amene ukuchita malonda ndi anthu amʼzilumba zambiri,Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Iwe Turo wanena kuti, ‘Ine ndine wokongola kwambiri.’+   Madera ako ali mkatikati mwa nyanja,Ndipo amisiri amene anakumanga anakukongoletsa kwambiri.   Anakupanga ndi matabwa a mtengo wa junipa* ochokera ku Seniri,+Ndipo anatenga mkungudza wa ku Lebanoni kuti ukhale mtengo wako womangirirapo chinsalu choyendetsera ngalawa.   Zopalasira zako anazipanga ndi mitengo ikuluikulu ya ku Basana,Ndipo mbali yakutsogolo kwako anaipanga ndi matabwa a paini, nʼkuikongoletsa ndi minyanga yochokera kuzilumba za Kitimu.+   Chinsalu chako choyendetsera ngalawa anachipanga ndi nsalu za mitundu yosiyanasiyana zochokera ku Iguputo,Ndipo pamwamba pako anaphimbapo ndi chinsalu chopangidwa ndi ulusi wabuluu komanso ubweya wa nkhosa wapepo wochokera kuzilumba za Elisha.+   Anthu a ku Sidoni ndi ku Arivadi+ ndi amene ankakupalasa. Iwe Turo, akatswiri ako odziwa kuyendetsa sitima zapamadzi ndi amene ankakuyendetsa.+   Amuna odziwa ntchito* komanso aluso a ku Gebala+ ndi amene ankamata molumikizira matabwa ako.+ Sitima zonse zapanyanja ndi anthu amene ankaziyendetsa ankabwera kwa iwe kudzagulitsa malonda. 10  Amuna a ku Perisiya, ku Ludi ndi ku Puti+ anali mʼgulu lako lankhondo, anali mʼgulu la asilikali ako. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo pamakoma ako ndipo anakubweretsera ulemerero. 11  Amuna a ku Arivadi amene ali mʼgulu la asilikali ako anaima pamwamba pa mpanda wako kuzungulira mzinda wonse,Ndipo amuna olimba mtima ankalondera nsanja zako. Iwo anapachika zishango zawo zozungulira mʼmakoma kuzungulira mpanda wako wonse,Ndipo anachititsa kuti ukhale wokongola kwambiri. 12  Tarisi+ ankachita nawe malonda chifukwa unali ndi chuma chochuluka.+ Anakupatsa siliva, chitsulo, tini ndi mtovu kuti atenge katundu wako.+ 13  Iwe unkachita malonda ndi Yavani, Tubala+ ndi Meseki.+ Iwo ankakupatsa akapolo+ ndi zinthu zakopa kuti iwe uwapatse katundu wako. 14  Ana a Togarima+ anapereka mahatchi ndi nyulu posinthanitsa ndi katundu wako. 15  Anthu a ku Dedani+ ankachita nawe malonda. Iwe unalemba ntchito anthu oti azikuchitira malonda mʼzilumba zambiri. Anthuwo ankakupatsa minyanga+ komanso mitengo ya phingo ngati mphatso.* 16  Edomu ankachita nawe malonda chifukwa chakuti unali ndi katundu wochuluka. Anakupatsa miyala ya nofeki, ubweya wa nkhosa wapepo, nsalu zopeta zamitundu yosiyanasiyana, nsalu zabwino kwambiri, miyala yamtengo wapatali ya korali ndi ya rube posinthanitsa ndi katundu wako. 17  Yuda komanso dziko la Isiraeli linachita nawe malonda. Anakupatsa tirigu wa ku Miniti,+ zakudya zapamwamba, uchi,+ mafuta ndi basamu+ posinthanitsa ndi katundu wako.+ 18  Damasiko+ ankachita nawe malonda chifukwa choti unali ndi katundu komanso chuma chambiri. Ankakupatsa vinyo wa ku Heliboni komanso ubweya wa nkhosa wa ku Zahari posinthanitsa ndi katundu wako. 19  Vedani ndi Yavani akudera la Uzali anakupatsa ziwiya zachitsulo, mitengo ya kasiya* ndi mabango onunkhira posinthanitsa ndi katundu wako. 20  Dedani+ ankachita nawe malonda a nsalu zoika pazishalo za mahatchi. 21  Unalemba ntchito Aluya ndi atsogoleri onse a ku Kedara,+ amene ankagulitsa ana a nkhosa, nkhosa zamphongo ndi mbuzi.+ 22  Unkachita malonda ndi amalonda a ku Sheba ndi ku Raama.+ Iwo anakupatsa mafuta onunkhira abwino kwambiri amitundu yosiyanasiyana, miyala yamtengo wapatali komanso golide posinthanitsa ndi katundu wako.+ 23  Harana,+ Kane, Edeni,+ amalonda a ku Sheba,+ Ashuri+ ndi Kilimadi ankachita nawe malonda. 24  Mʼmisika yako iwo ankachita malonda a zovala zokongola kwambiri, malaya opangidwa ndi nsalu yabuluu komanso nsalu yopeta yamitundu yosiyanasiyana ndi makapeti okhala ndi mitundu yosiyanasiyana. Zinthu zonsezi ankazimanga bwinobwino ndi zingwe. 25  Sitima zapamadzi za ku Tarisi+ zinkanyamula katundu wako wamalonda,Choncho unali ndi chuma chambiri ndipo unalemera* pakati pa nyanja. 26  Anthu okupalasa akupititsa panyanja zozama.Mphepo yakumʼmawa yakuwononga pakatikati pa nyanja. 27  Chuma chako, katundu wako, malonda ako, anthu amene akukuyendetsa, anthu ako oyenda panyanja,anthu omata molumikizira matabwa ako, anthu amene amakugulitsira malonda+ komanso asilikali ako onse,+Gulu lonse la anthu amene ali mwa iwe,*Onsewo adzamira pakati pa nyanja pa tsiku limene udzawonongedwe.+ 28  Anthu ako oyenda panyanja akadzafuula, madera amʼmphepete mwa nyanja adzagwedezeka. 29  Anthu onse opalasa ngalawa, oyendetsa sitima zapamadzi komanso anthu onse amene amagwira ntchito mʼsitima zapamadziAdzatsika mʼsitima zawo nʼkukaima pamtunda. 30  Iwo adzafuula ndipo adzakulirira mopwetekedwa mtima+Uku akudzithira dothi kumutu kwawo komanso kudzigubuduza paphulusa. 31  Adzadzimeta mpala nʼkuvala ziguduliNdipo adzakulirira kwambiri komanso mopwetekedwa mtima. 32  Polira adzaimba nyimbo yoimba polira ndipo adzakuimbira kuti: ‘Ndi ndani angafanane ndi Turo, amene wawonongedwa* pakati pa nyanja?+ 33  Katundu wako atabwera kuchokera pakatikati pa nyanja, unasangalatsa anthu ambiri.+ Chuma chako chochuluka komanso malonda ako zinalemeretsa mafumu apadziko lapansi.+ 34  Tsopano wawonongeka pakatikati pa nyanja, mʼmadzi akuya,+Ndipo katundu wako wamalonda komanso anthu ako amira nawe limodzi.+ 35  Anthu onse amene akukhala mʼzilumba adzakuyangʼanitsitsa modabwa,+Ndipo mafumu awo adzanjenjemera chifukwa cha mantha.+ Nkhope zawo zidzaoneka zankhawa. 36  Amalonda ochokera pakati pa mitundu ina ya anthu adzakuimbira mluzu chifukwa cha zimene zakuchitikira. Mapeto ako adzafika modzidzimutsa ndipo adzakhala owopsa,Moti sudzakhalaponso mpaka kalekale.’”’”+

Mawu a M'munsi

Mtengo wa junipa ndi wofanana ndi mtengo wa mkungudza.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Amuna achikulire.”
Kapena kuti, “msonkho.” Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Mtengo umenewu uli mʼgulu limodzi ndi mtengo wa sinamoni.
Mabaibulo ena amati, “unali ndi ulemerero.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mpingo wonse umene uli mwa iwe.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “wakhala chete.”