Ezekieli 32:1-32

  • Nyimbo yoimba polira yokhudza Farao ndi Iguputo (1-16)

  • Iguputo adzaikidwa mʼmanda limodzi ndi anthu osadulidwa (17-32)

32  Mʼchaka cha 12, mʼmwezi wa 12, pa tsiku loyamba la mweziwo, Yehova anandiuzanso kuti:  “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yoimba polira yokhudza Farao, mfumu ya Iguputo ndipo umuuze kuti,‘Iwe unali ngati mkango waungʼono wamphamvu* wa mitundu ina ya anthu,Koma wakhalitsidwa chete. Unali ngati chilombo chamʼnyanja+ chimene chimavundula madzi mwamphamvu mʼmitsinje yakoNʼkumadetsa madzi ndi mapazi ako ndiponso kuipitsa mitsinjeyo.’   Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Ndidzakuphimba ndi ukonde wanga pogwiritsa ntchito anthu a mitundu ina amene asonkhana pamodzi,Ndipo iwo adzakukoka ndi khoka langa.   Ndidzakusiya pamtundaNdiponso ndidzakuponya pabwalo. Ndidzachititsa kuti mbalame zonse zouluka mumlengalenga zitere pa iwe,Ndipo ndidzakhutitsa zilombo zapadziko lonse lapansi ndi nyama yako.+   Ndidzaponya mnofu wako mʼmapiri,Ndipo mʼzigwa ndidzadzazamo mtembo wako.+   Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi amene akutuluka mwamphamvu mʼthupi mwako mpaka kumapiri,Ndipo adzadzaza mitsinje.   Ndikadzakuzimitsa, ndidzaphimba kumwamba nʼkuchititsa mdima nyenyezi zake. Dzuwa ndidzaliphimba ndi mitambo,Ndipo mwezi sudzaonetsa kuwala kwake.+   Zounikira zonse zakumwamba ndidzazichititsa mdima chifukwa cha iwe,Ndipo ndidzagwetsa mdima mʼdziko lako,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.   ‘Ndidzachititsa kuti mitima ya anthu ambiri ikhale ndi nkhawa ndikadzatenga anthu ako ogwidwa ukapolo nʼkuwapititsa kwa anthu a mitundu ina,Kumayiko amene sukuwadziwa.+ 10  Ndidzachititsa mantha anthu ambiri a mitundu ina,Ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha chifukwa cha iwe ndikadzawaloza ndi lupanga langa. Iwo azidzanjenjemera mosalekeza chifukwa choopa kufa,Pa tsiku limene udzaphedwe.’ 11  Chifukwa Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Lupanga la mfumu ya Babulo lidzakuukira.+ 12  Ndidzachititsa kuti gulu la anthu amene amakutsatira aphedwe ndi malupanga a asilikali amphamvu.Onsewo ndi anthu a mitundu ina omwe ndi ankhanza kwambiri.+ Iwo adzawononga zinthu zimene Iguputo amazinyadira ndipo anthu ambiri amene amamutsatira adzaphedwa.+ 13  Ndidzawononga ziweto zake zonse zimene zili mʼmbali mwa madzi ambiri.+Ndipo phazi la munthu kapena ziboda za ziweto sizidzadetsanso madziwo.+ 14  Pa nthawi imeneyo ndidzayeretsa madzi awo,Ndipo ndidzachititsa kuti madzi amʼmitsinje yawo ayende ngati mafuta,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 15  ‘Ndikadzachititsa kuti dziko la Iguputo likhale bwinja, dziko limene zinthu zake zonse zalandidwa,+Ndikadzapha anthu onse amene akukhala mʼdzikolo,Iwo adzadziwa kuti ine ndine Yehova.+ 16  Imeneyi ndi nyimbo yoimba polira ndipo anthu adzaiimba.Ana aakazi a mitundu ina ya anthu adzaiimba. Nyimbo imeneyi adzaimbira Iguputo ndi gulu la anthu onse amene amamutsatira,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.” 17  Kenako mʼchaka cha 12, pa tsiku la 15 la mwezi, Yehova anandiuzanso kuti: 18  “Iwe mwana wa munthu, lirira gulu la anthu onse a ku Iguputo ndipo utsitsire dzikolo kumanda. Utsitsire kumanda dzikolo ndi ana aakazi a mitundu yamphamvu limodzi ndi amene akutsikira kudzenje.* 19  ‘Kodi ndiwe wokongola kuposa ndani? Tsikira kumanda ndipo ukagone limodzi ndi anthu osadulidwa. 20  Iguputo adzaphedwa pamodzi ndi anthu amene aphedwa ndi lupanga.+ Iye adzaphedwa ndi lupanga. Mukokereni kutali limodzi ndi gulu la anthu ake onse amene amamutsatira. 21  Ali pansi pa Manda,* asilikali amphamvu kwambiri adzalankhula ndi iyeyo komanso amene ankamuthandiza. Onsewo adzatsikira kumanda ndipo adzagona limodzi ndi anthu osadulidwa, ataphedwa ndi lupanga. 22  Asuri ali kumeneko limodzi ndi gulu lake lonse. Manda a anthu a ku Asuri ali mozungulira mfumu yawo. Onsewo anaphedwa ndi lupanga.+ 23  Manda a Asuri ali pakatikati pa dzenje ndipo gulu lake lonse lazungulira manda akewo. Onsewo anaphedwa ndi lupanga chifukwa anachititsa kuti anthu amene akukhala mʼdziko la anthu amoyo azikhala mwamantha. 24  Elamu+ ali kumandako limodzi ndi gulu la anthu ake onse amene ankamutsatira ndipo anthuwo azungulira manda ake. Onsewo anaphedwa ndi lupanga. Iwo anatsikira kunthaka ali osadulidwa. Anthu amenewa anachititsa kuti anthu amene akukhala mʼdziko la anthu amoyo azikhala mwamantha. Tsopano anthu amenewa adzachita manyazi limodzi ndi anthu amene akutsikira kudzenje.* 25  Iwo amupangira bedi pakati pa anthu amene aphedwa limodzi ndi gulu la anthu ake onse amene ankamutsatira, onse azungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osadulidwa, amene aphedwa ndi lupanga chifukwa anachititsa kuti anthu amene akukhala mʼdziko la anthu amoyo azikhala mwamantha. Iwo adzachita manyazi limodzi ndi anthu amene akutsikira kudzenje.* Iye waikidwa mʼmanda pakati pa anthu ophedwa. 26  Kumeneko nʼkumene kuli Meseki ndi Tubala+ limodzi ndi magulu a anthu awo onse amene ankawatsatira. Manda awo ali mozungulira mfumu yawo. Onsewa ndi anthu osadulidwa, anthu amene anabaidwa ndi lupanga chifukwa anachititsa kuti anthu amene akukhala mʼdziko la anthu amoyo azikhala mwamantha. 27  Kodi amenewa sadzagona limodzi ndi asilikali amphamvu osadulidwa amene anaphedwa, amene anatsikira ku Manda* limodzi ndi zida zawo zankhondo? Iwo adzaika malupanga awo pansi pa mitu yawo* ndipo machimo awo adzawaika pamafupa awo chifukwa asilikali amphamvuwo anawononga dziko la anthu amoyo. 28  Koma iwe udzaphwanyidwa pakati pa anthu osadulidwa ndipo udzagona limodzi ndi anthu amene anaphedwa ndi lupanga. 29  Edomu+ ali kumeneko. Kulinso mafumu ake ndi atsogoleri ake onse amene ngakhale kuti anali amphamvu, anaikidwa mʼmanda limodzi ndi anthu amene anaphedwa ndi lupanga. Anthu amenewanso adzagona limodzi ndi anthu osadulidwa+ komanso anthu amene akutsikira kudzenje.* 30  Kumeneko kuli akalonga* onse akumpoto limodzi ndi Asidoni onse+ amene anatsikira kumanda ali amanyazi. Anatsikira kumeneko limodzi ndi anthu amene anaphedwa, ngakhale kuti anali ochititsa mantha chifukwa cha mphamvu zawo. Adzagona mʼmanda ali osadulidwa limodzi ndi anthu amene anaphedwa ndi lupanga ndipo adzachita manyazi limodzi ndi anthu amene akutsikira kudzenje.* 31  Farao adzaona zinthu zonsezi ndipo mtima wake udzakhala mʼmalo chifukwa cha zonse zimene zinachitikira gulu la anthu amene ankamutsatira.+ Farao ndi asilikali ake onse adzaphedwa ndi lupanga,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 32  ‘Chifukwa anachititsa kuti anthu amene akukhala mʼdziko la anthu amoyo azikhala mwamantha, Farao ndi gulu lonse la anthu amene ankamutsatira adzaikidwa mʼmanda limodzi ndi anthu osadulidwa. Adzaikidwa mʼmanda pamodzi ndi anthu amene anaphedwa ndi lupanga,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mkango waungʼono wamanyenje.”
Kapena kuti, “kumanda.”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti, “kumanda.”
Kapena kuti, “kumanda.”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Nʼkutheka kuti akunena za asilikali amene anaikidwa mʼmanda limodzi ndi malupanga awo, potsatira mwambo wachisilikali.
Kapena kuti, “kumanda.”
Kapena kuti, “atsogoleri.”
Kapena kuti, “kumanda.”