Ezekieli 33:1-33

  • Ntchito za mlonda (1-20)

  • Nkhani yokhudza kuwonongedwa kwa Yerusalemu (21, 22)

  • Uthenga wopita kwa anthu okhala mʼmabwinja a ku Yerusalemu (23-29)

  • Anthu atamva uthengawo, sanachite chilichonse (30-33)

    • Ezekieli ali ngati “nyimbo yachikondi” (32)

    • “Pakati pawo panali mneneri” (33)

33  Yehova anandiuza kuti:  “Iwe mwana wa munthu, lankhula ndi anthu a mtundu wako+ ndipo uwauze kuti,‘Tiyerekeze kuti ndabweretsa lupanga mʼdziko,+ ndiyeno anthu onse amʼdzikolo asankha munthu kuti akhale mlonda wawo,  ndiye mlondayo waona lupanga likubwera kudzaukira dzikolo, nʼkuliza lipenga la nyanga ya nkhosa kuchenjeza anthu.+  Ngati munthu wamva kulira kwa lipenga koma osamvera chenjezolo,+ lupanga nʼkubwera ndi kumupha, magazi ake adzakhala pamutu pake.+  Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanamvere chenjezolo. Magazi ake adzakhala pamutu pake. Akanamvera chenjezolo, akanapulumutsa moyo wake.  Ngati mlondayo waona lupanga likubwera, koma iye osaliza lipenga,+ anthu osamva chenjezo lililonse, lupangalo nʼkufika ndi kupha munthu, munthuyo adzafa chifukwa cha zolakwa zake, koma mlondayo ndidzamuimba mlandu chifukwa cha imfa ya munthuyo.’*+  Koma iwe mwana wa munthu, ine ndakuika kuti ukhale mlonda wa nyumba ya Isiraeli. Choncho ukamva mawu ochokera pakamwa panga ukuyenera kuwachenjeza.+  Ndikauza munthu woipa kuti, ‘Munthu woipa iwe, udzafa ndithu,’+ koma iwe osanena chilichonse pochenjeza woipayo kuti asinthe zochita zake, iyeyo adzafa monga munthu woipa chifukwa cha zolakwa zake,+ koma iwe ndidzakuimba mlandu chifukwa cha magazi ake.*  Koma iwe ukachenjeza munthu woipa kuti asiye zinthu zoipa zimene akuchita, iye nʼkukana kusiya zoipazo, munthuyo adzafa chifukwa cha zolakwa zake,+ koma iweyo udzapulumutsa moyo wako ndithu.+ 10  Ndiye iwe mwana wa munthu, uza nyumba ya Isiraeli kuti, ‘Inu mwanena kuti: “Kupanduka kwathu komanso machimo athu zikutilemera kwambiri, nʼkutichititsa kuti titope kwambiri.+ Ndiye tingapitirize bwanji kukhala ndi moyo?”’+ 11  Auze kuti, ‘“Pali ine Mulungu wamoyo,” akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, “Ine sindisangalala ndi imfa ya munthu woipa,+ koma ndimafuna kuti munthu woipa asinthe zochita zake+ nʼkupitiriza kukhala ndi moyo.+ Bwererani! Bwererani nʼkusiya zinthu zoipa zimene mukuchita.+ Muferenji inu a nyumba ya Isiraeli?”’+ 12  Iwe mwana wa munthu, uza anthu a mtundu wako kuti, ‘Munthu wolungama akapanduka, zinthu zolungama zimene ankachita, sizidzamupulumutsa.+ Munthu woipa akasiya zoipa zakezo, zoipazo sizidzachititsa kuti apunthwe.+ Komanso pa tsiku limene munthu wolungama wachimwa, zinthu zolungama zimene ankachita zija sizidzamuthandiza kuti apitirize kukhala ndi moyo.+ 13  Ndikauza munthu wolungama kuti: “Ndithu, iwe udzapitiriza kukhala ndi moyo,” ndiyeno iyeyo nʼkuyamba kukhulupirira kuti zinthu zolungama zimene anachita mʼmbuyo zidzamupulumutsa nʼkuchita zinthu zoipa,*+ zinthu zonse zolungama zimene anachita zija sizidzakumbukiridwa. Iye adzafa chifukwa cha zinthu zoipa zimene wachita.+ 14  Ndikauza munthu woipa kuti: “Udzafa ndithu,” ndiyeno iyeyo nʼkusiya machimo akewo, nʼkuyamba kuchita zinthu motsatira malamulo ndiponso mwachilungamo,+ 15  komanso munthu woipayo akabweza chinthu chimene anatenga kwa munthu amene anakongola zinthu zake,+ akabweza zinthu zimene analanda mwauchifwamba,+ nʼkuyamba kuyenda motsatira malamulo opatsa moyo popewa kuchita zinthu zoipa, ndithu munthuyo adzapitiriza kukhala ndi moyo.+ Iye sadzafa. 16  Sadzapatsidwa chilango chifukwa cha machimo amene anachitawo.+ Adzapitiriza kukhala ndi moyo chifukwa chochita zinthu motsatira malamulo ndiponso mwachilungamo.’+ 17  Koma anthu a mtundu wako anena kuti, ‘Njira za Yehova nʼzopanda chilungamo,’ pamene njira zawo ndi zimene zili zopanda chilungamo. 18  Munthu amene amachita zinthu zabwino akasiya kuchita zabwinozo nʼkumachita zoipa,* akuyenera kufa chifukwa cha zochita zakezo.+ 19  Koma munthu woipa akasiya kuchita zinthu zoipa nʼkuyamba kuchita zinthu motsatira malamulo ndiponso mwachilungamo, adzapitiriza kukhala ndi moyo chifukwa chochita zimenezi.+ 20  Koma inu mwanena kuti, ‘Njira za Yehova nʼzopanda chilungamo.’+ Inu a nyumba ya Isiraeli, ine ndidzaweruza aliyense wa inu mogwirizana ndi zochita zake.” 21  Patapita nthawi, mʼchaka cha 12, mʼmwezi wa 10, tsiku la 5 la mweziwo, kuchokera pamene tinatengedwa kupita ku ukapolo, munthu wina amene anathawa ku Yerusalemu anabwera kwa ine+ nʼkundiuza kuti: “Mzinda uja wawonongedwa!”+ 22  Ndiyeno madzulo, munthu amene anathawa uja asanafike, dzanja la Yehova linandikhudza ndipo Mulungu anatsegula pakamwa panga munthu uja asanafike mʼmawa. Choncho pakamwa panga panatseguka ndipo ndinayambanso kulankhula.+ 23  Kenako Yehova anandiuza kuti: 24  “Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmabwinjawa+ akulankhula zokhudza dziko la Isiraeli kuti, ‘Abulahamu anali munthu mmodzi, koma anatenga dzikoli kukhala lake.+ Ife tilipo ambiri, choncho dzikoli laperekedwa kwa ife kuti likhale lathu.’ 25  Choncho auze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Inu mukudya nyama limodzi ndi magazi ake,+ mumadalira* mafano anu onyansa* ndipo mukupitiriza kukhetsa magazi.+ Ndiye pamenepa ndinu oyenera kutenga dzikoli kuti likhale lanu? 26  Inu mukudalira lupanga lanu,+ mukuchita zinthu zonyansa ndipo aliyense wa inu akugona ndi mkazi wa mnzake.+ Ndiye kodi pamenepa ndinu oyenera kutenga dzikoli kuti likhale lanu?”’+ 27  Uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Pali ine Mulungu wamoyo, anthu amene akukhala mʼmabwinja adzaphedwa ndi lupanga. Amene ali kutchire ndidzawapereka kwa zilombo zolusa kuti akhale chakudya chawo. Ndipo amene ali mʼmalo otetezeka komanso mʼmapanga adzafa ndi matenda.+ 28  Ndidzachititsa kuti dzikolo likhale bwinja lowonongeka kwambiri.+ Ndidzathetsa kudzikuza komanso kunyada kwake ndipo mapiri a mu Isiraeli adzawonongedwa+ moti sipadzapezeka wodutsamo. 29  Ndikadzachititsa kuti dzikolo likhale bwinja lowonongeka kwambiri+ chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene achita, iwo adzadziwa kuti ine ndine Yehova.”’+ 30  Koma iwe mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akukambirana za iwe mʼmbali mwa mpanda komanso mʼmakomo a nyumba.+ Aliyense akuuza mʼbale wake kuti, ‘Bwerani tidzamve mawu ochokera kwa Yehova.’ 31  Iwo adzasonkhana nʼkukhala pamaso pako ngati anthu anga. Adzamva mawu ako koma sadzawatsatira.+ Chifukwa ndi pakamwa pawo, amakuuza zongofuna kukusangalatsa,* koma mtima wawo ukungofuna kupeza phindu mwachinyengo. 32  Kwa iwo uli ngati nyimbo yachikondi imene yaimbidwa mwaluso ndi choimbira cha zingwe komanso ndi mawu anthetemya. Iwo adzamva mawu ako, koma palibe amene adzawatsatire. 33  Koma mawu ako akadzakwaniritsidwa, chifukwa adzakwaniritsidwa ndithu, iwo adzadziwa kuti pakati pawo panali mneneri.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “koma ndidzafunsa mlondayo za magazi a munthuyo.”
Kapena kuti, “koma magazi ake ndidzawafuna kuchokera kwa iwe.”
Kapena kuti, “zopanda chilungamo.”
Kapena kuti, “nʼkumachita zopanda chilungamo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mumakweza maso anu nʼkuyangʼana.”
Mawu a Chiheberi ali ndi tanthauzo lofanana ndi mawu akuti “ndowe” ndipo amagwiritsidwa ntchito posonyeza kuipidwa.
Kapena kuti, “amalankhula mokopa.”