Ezekieli 34:1-31

  • Ulosi wokhudza abusa a Isiraeli (1-10)

  • Yehova amasamalira nkhosa zake (11-31)

    • “Mtumiki wanga Davide” adzakhala mʼbusa wawo (23)

    • “Pangano la mtendere” (25)

34  Yehova anandiuzanso kuti:  “Iwe mwana wa munthu, losera zoipa zimene zidzachitikire abusa a Isiraeli. Losera ndipo uuze abusawo kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Tsoka abusa a Isiraeli,+ amene akhala akungodzidyetsa okha! Kodi abusa ntchito yawo si kudyetsa nkhosa?+  Inu mukudya mafuta, ndipo mukuvala zovala zaubweya wa nkhosa. Mukupha nyama zonenepa kwambiri,+ koma nkhosa simukuzidyetsa.+  Nkhosa zofooka simunazilimbitse ndipo zodwala simunazichiritse. Zovulala simunazimange. Nkhosa zosochera simunazibweze ndipo zimene zasowa simunazifufuze.+ Koma munkazilamulira mwankhanza komanso mopondereza.+  Choncho zinamwazikana chifukwa zinalibe mʼbusa+ ndipo zinakhala chakudya cha zilombo zonse zakutchire.  Nkhosa zanga zinasochera mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zitalizitali. Nkhosa zanga zinabalalika padziko lonse lapansi ndipo panalibe amene ankazifufuza kapena kuziyangʼanayangʼana.  Choncho abusa inu, imvani mawu a Yehova:  ‘“Pali ine Mulungu wamoyo,” akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, “nkhosa zanga zagwidwa ndipo zakhala chakudya cha zilombo zonse zakutchire chifukwa panalibe mʼbusa ndipo abusa anga sanazifunefune. Koma ankangodzidyetsa okha, osadyetsa nkhosa zanga.”’  Choncho abusa inu, imvani mawu a Yehova. 10  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Ine nditsutsa abusawo ndipo ndiwauza kuti andibwezere nkhosa zanga. Ndiwaletsa kuti asamadyetse* nkhosa zanga+ ndipo abusawo sadzadzidyetsanso okha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga mʼkamwa mwawo ndipo sizidzakhalanso chakudya chawo.’” 11  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndilipo ndipo ndidzafunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.+ 12  Ndidzasamalira nkhosa zanga ngati mʼbusa amene wapeza nkhosa zake zimene zinabalalika ndipo akuzidyetsa.+ Ndidzazipulumutsa mʼmalo onse amene zinabalalikira pa tsiku la mitambo ndi mdima wandiweyani.+ 13  Nkhosa zanga ndidzazitulutsa pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzazisonkhanitsa pamodzi kuchokera mʼmayiko ena nʼkuzibweretsa mʼdziko lawo. Ndidzazidyetsa mʼmapiri a ku Isiraeli,+ mʼmphepete mwa mitsinje komanso pafupi ndi malo onse amʼdzikolo kumene kumakhala anthu. 14  Nkhosazo ndidzazidyetsera mʼmalo a msipu wabwino ndipo malo amene zizidzadya msipu adzakhala kumapiri ataliatali a ku Isiraeli.+ Kumeneko zizidzagona pansi mʼmalo abwino kwambiri odyetserako ziweto+ ndipo zizidzadya msipu wabwino kwambiri mʼmapiri a ku Isiraeli. 15  Ine ndidzadyetsa nkhosa zanga+ ndipo ndidzazipatsa malo oti zigone,”+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 16  “Nkhosa imene yasowa ndidzaifunafuna,+ imene yasochera ndidzaibweza. Imene yavulala ndidzaimanga povulalapo ndipo imene ili yofooka ndidzailimbitsa, koma yonenepa ndi yamphamvu ndidzaiwononga. Ndidzaipatsa chiweruzo kuti chikhale chakudya chake.” 17  Ponena za inu nkhosa zanga, Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndatsala pangʼono kuweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa inzake komanso pakati pa nkhosa zamphongo ndi mbuzi zamphongo.+ 18  Kodi kudya msipu wabwino kwambiri si kokwanira kwa inu? Kodi mukuyeneranso kumapondaponda msipu wotsala ndi mapazi anu? Ndipo mukamaliza kumwa madzi oyera, kodi mukuyenera kuwadetsa powapondaponda ndi mapazi anu? 19  Kodi nkhosa zanga zizidya msipu umene inu mwaupondaponda ndi mapazi anu komanso kumwa madzi amene mwawadetsa powapondaponda ndi mapazi anu?” 20  Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wauza nkhosazo kuti: “Ine ndilipo ndipo ndidzapereka chiweruzo pakati pa nkhosa yonenepa ndi nkhosa yowonda. 21  Ndidzachita zimenezi chifukwa chakuti munkakankha nkhosa ndi nthiti zanu ndiponso mapewa anu. Ndipo munkagunda ndi nyanga zanu nkhosa zonse zodwala mpaka kuzibalalitsira kutali. 22  Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sizidzagwidwanso ndi zilombo.+ Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa inzake. 23  Ndidzazipatsa mʼbusa mmodzi+ amene ndi mtumiki wanga Davide,+ ndipo adzazidyetsa. Iye adzakhala mʼbusa wawo ndipo azidzazidyetsa.+ 24  Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wawo,+ ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mtsogoleri pakati pawo.+ Ine Yehova ndanena zimenezi. 25  Ine ndidzachita pangano lamtendere ndi nkhosazo.+ Ndipo ndidzachotsa zilombo zolusa mʼdzikomo+ nʼcholinga choti nkhosazo zizidzakhala mʼchipululu zili zotetezeka ndipo zizidzagona munkhalango.+ 26  Nkhosazo komanso malo ozungulira phiri langa adzalandira madalitso+ ndipo ndidzachititsa kuti mvula igwe pa nthawi yake. Madalitso adzagwa ambiri ngati mvula.+ 27  Mitengo yamʼdzikomo idzabereka zipatso ndipo nthaka idzatulutsa zokolola zake.+ Iwo adzakhala mʼdzikolo motetezeka ndipo adzadziwa kuti ine ndine Yehova ndikadzathyola goli lawo+ nʼkuwapulumutsa kwa anthu amene anawagwira kuti akhale akapolo awo. 28  Anthu a mitundu ina sadzawagwiranso ndipo zilombo zolusa sizidzawadya. Iwo azidzakhala motetezeka popanda aliyense wowaopseza.+ 29  Ndidzawapatsa munda umene udzakhale wotchuka* chifukwa cha mbewu zake ndipo anthu sadzafanso ndi njala mʼdzikomo+ komanso anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.+ 30  ‘Zikadzatero, iwo adzadziwa kuti ine, Yehova Mulungu wawo, ndili nawo limodzi ndiponso kuti iwowo, a nyumba ya Isiraeli ndi anthu anga,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”’ 31  ‘Koma inu nkhosa zanga,+ nkhosa zimene ndikuzisamalira, ndinu anthu basi ndipo ine ndine Mulungu wanu,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “asamawete.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “umene dzina lake lidzatchuka.”