Ezekieli 37:1-28
37 Mphamvu za Yehova zinayamba kugwira ntchito pa ine* moti mzimu wa Yehova unanditenga nʼkukandikhazika pakati pa chigwa+ ndipo mʼchigwamo munali mafupa okhaokha.
2 Iye anandiyendetsa mʼchigwamo kuti ndione mafupa onsewo ndipo ndinaona kuti mʼchigwamo munali mafupa ambiri ndipo anali ouma kwambiri.+
3 Ndiyeno anandifunsa kuti: “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupawa angakhale ndi moyo?” Ine ndinayankha kuti: “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, inu ndi amene mukudziwa zimenezo.”+
4 Ndiye anandiuza kuti: “Losera zokhudza mafupa amenewa ndipo uwauze kuti, ‘Inu mafupa ouma, imvani mawu a Yehova:
5 Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wauza mafupa awa kuti: “Ndichititsa kuti mpweya ulowe mwa inu ndipo mukhala amoyo.+
6 Ndidzakuikirani mitsempha komanso mnofu ndipo ndidzakukutirani ndi khungu nʼkuika mpweya mwa inu ndipo mudzakhala ndi moyo. Choncho mudzadziwa kuti ine ndine Yehova.”’”
7 Choncho ine ndinalosera mogwirizana ndi zimene anandilamula. Nditangolosera, panamveka phokoso la mafupa kuti gobedegobede! Ndipo mafupawo anayamba kubwera pamodzi nʼkumalumikizana.
8 Kenako ndinaona mitsempha ndi mnofu zikukuta mafupawo ndipo khungu linabwera pamwamba pake. Koma mʼmafupawo munalibe mpweya.
9 Kenako anandiuza kuti: “Losera kwa mphepo. Iwe mwana wa munthu, losera ndipo uuze mphepoyo kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Iwe mphepo,* bwera kuchokera kumbali zonse 4 nʼkuwomba anthu amene anaphedwawa kuti akhalenso ndi moyo.”’”
10 Choncho ndinalosera mogwirizana ndi zimene anandilamula ndipo mpweya* unalowa mwa iwo. Iwo anakhala ndi moyo ndipo anaimirira.+ Anali gulu lalikulu kwambiri la asilikali.
11 Kenako anandiuza kuti: “Iwe mwana wa munthu, mafupawa akuimira nyumba yonse ya Isiraeli.+ Iwo akunena kuti, ‘Mafupa athu auma ndipo tilibenso chiyembekezo chilichonse.+ Tatheratu!’
12 Choncho losera, uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndidzatsegula manda anu,+ inu anthu anga ndipo ndidzakutulutsani mʼmandamo nʼkukubweretsani mʼdziko la Isiraeli.+
13 Inu anthu anga, ine ndikadzatsegula manda anu nʼkukutulutsani mʼmandamo, mudzadziwa kuti ine ndine Yehova.”+
14 Ndidzaika mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhala amoyo.+ Ndidzakukhazikani mʼdziko lanu ndipo mudzadziwa kuti ine Yehova ndinanena zimenezi ndipo ndazichita,’ akutero Yehova.”
15 Yehova anandiuzanso kuti:
16 “Koma iwe mwana wa munthu, tenga ndodo nʼkulembapo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisiraeli amene ali naye.’*+ Kenako utengenso ndodo ina nʼkulembapo kuti, ‘Ndodo ya Yosefe yoimira Efuraimu ndi onse amʼnyumba ya Isiraeli amene ali naye.’*+
17 Ndiyeno uziike pamodzi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.+
18 Anthu a mtundu wako* akakufunsa kuti, ‘Kodi sutiuza kuti zinthu zimenezi zikutanthauza chiyani?’
19 Uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine nditenga ndodo ya Yosefe ndi mafuko a Isiraeli amene ali naye. Ndodo imeneyi ili mʼdzanja la Efuraimu. Ndidzaiphatikiza ndi ndodo ya Yuda ndipo idzakhala ndodo imodzi.+ Iwo adzakhala ndodo imodzi mʼdzanja langa.”’
20 Ndodo zimene wazilembazo zikhale mʼdzanja lako kuti azione.
21 Ndiye uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine nditenga Aisiraeli kuchokera kwa anthu a mitundu ina kumene anapita. Ndidzawasonkhanitsa pamodzi kuchokera kumbali zonse ndipo ndidzawabweretsa mʼdziko lawo.+
22 Ndidzawachititsa kuti akhale mtundu umodzi mʼdzikolo+ ndipo azidzakhala mʼmapiri a Isiraeli. Onse azidzalamulidwa ndi mfumu imodzi+ ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawanika nʼkukhala maufumu awiri.+
23 Iwo sadzadziipitsanso ndi mafano awo onyansa,* zochita zawo zonyansa ndi zolakwa zawo zonse.+ Ndidzawapulumutsa ku zochita zawo zosakhulupirika zimene zinachititsa kuti achimwe ndipo ndidzawayeretsa. Iwo adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo.+
24 Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo+ ndipo onsewo adzakhala ndi mʼbusa mmodzi.+ Iwo adzayenda motsatira zigamulo zanga ndiponso kusunga malamulo anga mosamala kwambiri.+
25 Anthu amenewa adzakhala mʼdziko limene ndinapatsa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhala.+ Iwo adzakhala mʼdzikomo ndi ana awo* komanso zidzukulu zawo+ mpaka kalekale.+ Davide mtumiki wanga adzakhala mtsogoleri* wawo mpaka kalekale.+
26 Ndidzachita nawo pangano lamtendere+ ndipo pangano limeneli lidzakhalapo mpaka kalekale. Ine ndidzachititsa kuti akhazikike mʼdzikolo ndipo ndidzawachulukitsa+ komanso ndidzaika malo anga opatulika pakati pawo mpaka kalekale.
27 Tenti yanga idzakhala* pakati pawo.* Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.+
28 Malo anga opatulika akadzakhala pakati pawo mpaka kalekale, anthu a mitundu ina adzadziwa kuti ine Yehova, ndikuyeretsa Isiraeli.”’”+
Mawu a M'munsi
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Dzanja la Yehova linafika pa ine.”
^ Kapena kuti, “mpweya; mzimu.”
^ Kapena kuti, “mzimu.”
^ Kapena kuti, “amene ndi anzake.”
^ Kapena kuti, “amene ndi anzake.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Ana aamuna a anthu ako.”
^ Mawu a Chiheberi ali ndi tanthauzo lofanana ndi mawu akuti “ndowe” ndipo amagwiritsidwa ntchito posonyeza kuipidwa.
^ Kapena kuti, “kalonga.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “ana awo aamuna.”
^ Kapena kuti, “Malo anga okhala adzakhala; Nyumba yanga.”
^ Kapena kuti, “idzawaphimba.”