Ezekieli 38:1-23

  • Gogi adzaukira Isiraeli (1-16)

  • Yehova adzakwiyira Gogi (17-23)

    • ‘Mitundu ya anthu idzadziwa kuti ine ndine Yehova’ (23)

38  Yehova anandiuzanso kuti:  “Iwe mwana wa munthu, yangʼana Gogi wa kudziko la Magogi,+ mtsogoleri wamkulu* wa Meseki ndi Tubala+ ndipo ulosere zoipa zimene zidzamuchitikire.+  Unene kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndikupatsa chilango iwe Gogi, mtsogoleri wamkulu* wa Meseki ndi Tubala.  Ine ndidzakubweza nʼkukukola chibwano ndi ngowe.+ Kenako ndidzakupititsa kunkhondo limodzi ndi asilikali ako onse,+ mahatchi ako ndi amuna okwera pamahatchi ndipo onsewo adzavala mwaulemerero. Iwo adzakhala gulu lalikulu lonyamula zishango zazikulu ndi zazingʼono, ndipo onsewo ndi aluso lomenya nkhondo pogwiritsa ntchito malupanga.  Udzabwera limodzi ndi asilikali a ku Perisiya, Itiyopiya ndi Puti.+ Onsewa adzanyamula zishango zazingʼono ndipo adzavala zipewa.  Udzabweranso ndi Gomeri ndi magulu ake onse a asilikali, komanso ana a Togarima+ ochokera kumadera akutali kwambiri akumpoto. Iwo adzabwera ndi magulu awo onse a asilikali. Choncho iwe udzabwera ndi mitundu yambiri ya anthu.+  Khala wokonzeka, konzekera kumenya nkhondo, iweyo limodzi ndi asilikali ako onse amene asonkhana ndi iwe. Iweyo ukhala mtsogoleri* wawo.  Pakapita masiku ambiri, iwe udzaitanidwa. Ndiye pakadzapita zaka zambiri, udzalowa mʼdziko la anthu amene anabwerera kwawo. Anthu amenewa anapulumuka, lupanga litawononga dziko lawo. Kenako anasonkhanitsidwa pamodzi kuchokera kumitundu ina ya anthu nʼkukakhala kumapiri a ku Isiraeli amene anakhala ali owonongeka kwa nthawi yaitali. Anthu amene akukhala mʼdzikoli anawabwezeretsa kwawo kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Onsewo akukhala mʼdzikoli motetezeka.+  Iwe udzabwera mʼdzikolo ngati mphepo yamkuntho kudzawaukira. Iweyo, magulu a asilikali ako onse, pamodzi ndi anthu ambiri a mitundu ina, mudzaphimba dzikolo ngati mitambo.”’ 10  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Pa tsiku limenelo, maganizo adzakubwerera mumtima mwako ndipo udzakonza chiwembu choipa kwambiri. 11  Udzanena kuti: “Ndikalowa mʼdziko limene midzi yake ndi yosatetezeka.+ Ndikaukira anthu amene akukhala mwabata, popanda chowasokoneza. Ndikaukira anthu onsewo amene akukhala mʼmidzi yopanda mipanda ndipo alibe zotsekera ndiponso mageti.” 12  Udzapita kumeneko kuti ukalande komanso kutengako zinthu zambiri, ndiponso kuti ukaukire malo owonongedwa amene tsopano mukukhala anthu.+ Udzapita kukaukira anthu amene anasonkhanitsidwanso pamodzi kuchokera kumitundu ina,+ amene akusonkhanitsa chuma ndi katundu,+ komanso amene akukhala pakatikati pa dziko lapansi. 13  Sheba+ ndi Dedani,+ amalonda a ku Tarisi+ ndi asilikali ake onse* adzakufunsa kuti: “Kodi walowa mʼdzikoli kuti ukalande zinthu zambiri? Kodi wasonkhanitsa asilikali ako kuti ukatenge siliva, golide, chuma ndi katundu? Kodi ukufuna ukalande zinthu zambiri zamʼdzikoli?”’ 14  Choncho losera, iwe mwana wa munthu, ndipo uuze Gogi kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Pa tsiku limenelo, anthu anga Aisiraeli akamadzakhala mwabata, ndithu iwe udzadziwa zimenezo.+ 15  Udzabwera kuchokera kumalo ako, kumadera akutali kwambiri akumpoto.+ Udzabwera ndi mitundu yambiri ya anthu. Anthuwo adzakhala gulu lalikulu, adzakhala chigulu chachikulu cha asilikali. Onsewo adzabwera atakwera pamahatchi.+ 16  Mofanana ndi mitambo imene yaphimba dziko, iwe udzabwera kudzaukira anthu anga Aisiraeli. Mʼmasiku otsiriza, ine ndidzakubweretsa kuti uukire dziko langa+ nʼcholinga choti anthu a mitundu ina adzandidziwe ndikamadzadziyeretsa pamaso pawo, kudzera mwa iwe Gogi.”’+ 17  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Kodi kale lija sindinkanena zokhudza iwe kudzera mwa atumiki anga, aneneri a Isiraeli? Aneneriwo analosera kwa zaka zambiri kuti ndidzakutumiza kwa iwo kuti ukawaukire.’ 18  ‘Pa tsiku limenelo, tsiku limene Gogi adzalowe mʼdziko la Isiraeli, ndidzakhala ndi mkwiyo waukulu,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 19  ‘Ine ndidzalankhula mwaukali wanga woyaka moto komanso nditakwiya kwambiri. Ndipo pa tsiku limenelo mʼdziko la Isiraeli mudzachitika chivomerezi chachikulu. 20  Chifukwa cha ine, nsomba zamʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zilombo zakutchire, nyama zonse zimene zimakwawa panthaka ndiponso anthu onse apadziko lapansi, zidzanjenjemera. Mapiri adzagwa,+ malo otsetsereka adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwera pansi.’ 21  ‘Ndidzamuyambitsira nkhondo mʼmapiri anga onse kuti amuwononge,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. ‘Aliyense adzapha mʼbale wake ndi lupanga.+ 22  Ine ndidzamuweruza pomubweretsera mliri+ ndipo anthu ambiri adzafa. Ndidzamugwetsera mvula yamphamvu, matalala,+ moto+ ndi sulufule.+ Ndidzagwetsa zinthu zimenezi pa iyeyo, magulu a asilikali ake ndi mitundu yambiri ya anthu amene adzakhale kumbali yake.+ 23  Ndithu ndidzasonyeza mphamvu zanga, komanso ndidzasonyeza kuti ndine Mulungu woyera ndipo ndidzachititsa kuti anthu ambiri a mitundu ina andidziwe. Iwo adzadziwa kuti ine ndine Yehova.’”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “kalonga wamkulu.”
Kapena kuti, “kalonga wamkulu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mlonda.”
Kapena kuti, “mikango yamphamvu yamanyenje.”