Ezekieli 39:1-29

  • Gogi ndi magulu ake a asilikali adzawonongedwa (1-10)

  • Adzaikidwa mʼmanda mʼChigwa cha Hamoni-Gogi (11-20)

  • Isiraeli adzabwereranso mwakale (21-29)

    • Mulungu anatsanulira mzimu wake pa Isiraeli (29)

39  “Iwe mwana wa munthu, losera zoipa zimene zidzachitikire Gogi+ ndipo umuuze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndikupatsa chilango iwe Gogi, mtsogoleri wamkulu* wa Meseki ndi Tubala.+  Ndidzakubweza nʼkukutsogolera kuti uchoke kumadera akutali kwambiri akumpoto+ ndipo ndidzakubweretsa kumapiri a ku Isiraeli.  Ndidzakuphumitsa uta mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzachititsa kuti mivi yako igwe pansi kuchoka mʼdzanja lako lamanja.  Iwe udzafera mʼmapiri a ku Isiraeli+ limodzi ndi magulu ako onse a asilikali ndi anthu a mitundu ina amene adzakhale nawe. Ndidzakuperekani kwa mbalame zamitundumitundu zodya nyama ndi zilombo zakutchire kuti mukhale chakudya chawo.”’+  ‘Iweyo udzafera pamtetete,+ chifukwa ine ndanena zimenezi,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.  ‘Ndidzatumiza moto kuti ukawononge Magogi komanso anthu amene akukhala motetezeka mʼzilumba,+ ndipo anthu adzadziwa kuti ine ndine Yehova.  Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Aisiraeli. Sindidzalolanso kuti dzina langa loyera lidetsedwe, ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti ine ndine Yehova,+ Mulungu Woyera mu Isiraeli.’+  ‘Inde, zimene ulosiwu ukunena zidzachitika ndipo zidzakwaniritsidwa,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. ‘Tsiku limene ndakhala ndikunena lija ndi limeneli.  Anthu amene akukhala mʼmizinda ya Isiraeli adzapita kukakoleza moto pogwiritsa ntchito zida zankhondo. Zida zake ndi zishango zazingʼono ndi zishango zazikulu, mauta ndi mivi, zibonga* ndi mikondo ingʼonoingʼono. Iwo adzagwiritsa ntchito zida zimenezi kwa zaka 7 pokoleza moto.+ 10  Iwo sadzafunika kunyamula mitengo kutchire kapena kutola nkhuni kunkhalango chifukwa chakuti adzagwiritsa ntchito zida zankhondozo pokoleza moto.’ ‘Adzalanda zinthu za anthu amene anawalanda zinthu zawo ndipo adzatenga katundu wa anthu amene anatenga katundu wawo,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 11  ‘Pa tsiku limenelo Gogi+ ndidzamupatsa malo kuti akhale manda ake ku Isiraeli komweko, mʼchigwa chimene anthu amene amapita kumʼmawa kwa nyanja amadutsa, ndipo chigwacho chidzatseka njira imene anthu amadutsa. Kumeneko nʼkumene adzaike mʼmanda Gogi limodzi ndi magulu onse a anthu amene ankamutsatira ndipo adzalitchula kuti Chigwa cha Hamoni-Gogi.*+ 12  A nyumba ya Isiraeli adzatenga miyezi 7 akuika mʼmanda Gogi ndi gulu lake kuti ayeretse dzikolo.+ 13  Anthu onse amʼdzikolo adzagwira ntchito yoika mʼmanda anthuwo. Iwo adzatchuka chifukwa cha ntchito imeneyi pa tsiku limene ine ndidzalemekezeke,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 14  ‘Anthu adzapatsidwa ntchito yoti azidzazungulira mʼdzikomo nthawi zonse nʼkumakwirira mitembo imene yatsala pamtunda kuti ayeretse dziko. Iwo adzakhala akufunafuna mitembo kwa miyezi 7. 15  Anthu amene akungodutsa mʼdzikolo akaona fupa la munthu, azidzaika chizindikiro pafupi ndi fupalo. Kenako anthu amene anapatsidwa ntchito yokwirira mitembo aja adzalikwirira mʼChigwa cha Hamoni-Gogi.+ 16  Kumeneko kudzakhalanso mzinda wotchedwa Hamona.* Ndipo anthu adzayeretsa dzikolo.’+ 17  Koma iwe mwana wa munthu, Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Uza mbalame zamtundu uliwonse ndi zilombo zonse zakutchire kuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere kuno. Zungulirani nsembe yanga imene ndikukukonzerani. Imeneyi ndi nsembe yaikulu mʼmapiri a ku Isiraeli.+ Mukabwera mudzadya nyama ndi kumwa magazi.+ 18  Mudzadya mnofu wa anthu amphamvu komanso kumwa magazi a atsogoleri a dziko lapansi, omwe ndi nkhosa zamphongo, ana a nkhosa amphongo, mbuzi ndi ngʼombe zamphongo, nyama zonse zonenepa za ku Basana. 19  Inu mudzadya mafuta mosusuka ndipo mudzamwa magazi mpaka mutaledzera ndi nsembe imene ndidzakukonzereni.”’ 20  ‘Patebulo langa mudzadya nʼkukhuta nyama ya mahatchi, ya okwera magaleta, ya anthu amphamvu ndi asilikali osiyanasiyana,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. 21  ‘Ndidzasonyeza ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina ndipo mitundu yonse ya anthu idzaona chiweruzo chimene ndapereka komanso mphamvu zimene* ndasonyeza pakati pawo.+ 22  Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo, a nyumba ya Isiraeli adzadziwa kuti ine ndine Yehova, Mulungu wawo. 23  Anthu a mitundu ina adzadziwa kuti a nyumba ya Isiraeli anatengedwa kupita ku ukapolo chifukwa cha zolakwa zawo, popeza anandichitira zinthu mosakhulupirika.+ Choncho ine ndinawabisira nkhope yanga+ nʼkuwapereka kwa adani awo+ ndipo onse anaphedwa ndi lupanga. 24  Ndinawachitira zinthu mogwirizana ndi zonyansa zimene anachita komanso chifukwa chakuti anaphwanya malamulo, moti ndinawabisira nkhope yanga.’ 25  Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Ndidzabwezeretsa ana a Yakobo+ omwe anatengedwa kupita kumayiko ena ndipo ndidzachitira chifundo nyumba yonse ya Isiraeli.+ Ndi mphamvu zanga zonse, ndidzateteza dzina langa loyera.*+ 26  Akadzachititsidwa manyazi chifukwa cha zinthu zonse zosakhulupirika zimene anandichitira,+ adzakhala mʼdziko lawo motetezeka, popanda wowaopseza.+ 27  Ndikadzawabweretsa kuchokera kumitundu ina ya anthu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi kuchokera kumayiko a adani awo,+ ndidzadziyeretsa pakati pawo pamaso pa mitundu yambiri ya anthu.’+ 28  ‘Iwo adzadziwa kuti ine ndine Yehova Mulungu wawo, ndikadzawapititsa ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina, kenako nʼkuwabwezeretsa kudziko lawo osasiyako wina aliyense.+ 29  Sindidzawabisiranso nkhope yanga+ chifukwa panyumba ya Isiraeli ndidzatsanulirapo mzimu wanga,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “kalonga wamkulu.”
Mabaibulo ena amati, “zobayira.” Zimenezi ndi zida zokhala ndi nsonga zakuthwa.
Kapena kuti, “Chigwa cha Magulu a Anthu Amene Ankatsatira Gogi.”
Kutanthauza, “Magulu a Anthu Otsatira Gogi.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “dzanja limene.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndidzadzipereka kwambiri chifukwa cha dzina langa loyera.”