Ezekieli 41:1-26

  • Malo opatulika amʼkachisi (1-4)

  • Khoma komanso zipinda zamʼmbali (5-11)

  • Nyumba imene inali kumadzulo (12)

  • Anayeza nyumba zonse (13-15a)

  • Mkati mwa kachisi (15b-26)

41  Kenako munthu uja anandipititsa mʼmalo oyera,* ndipo anayeza zipilala zamʼmbali. Chipilala cha mbali imodzi chinali mikono* 6 mulifupi ndipo cha mbali ina chinalinso mikono 6 mulifupi.  Khomo lolowera linali mikono 10 mulifupi, ndipo makoma apakhomopo anali* mikono 5 mbali imodzi, ndi mikono 5 mbali inayo. Anayeza chipinda chakunja ndipo anapeza kuti chinali mikono 40 mulitali, mulifupi chinali mikono 20.  Kenako analowa mʼchipinda chamkati* nʼkuyeza chipilala chamʼmbali chapakhomo ndipo anapeza kuti kuchindikala kwake chinali mikono iwiri. Anapezanso kuti khomo linali mikono 6 ndipo makoma a khomolo anali* mikono 7.  Kenako anayeza chipinda chimene chinayangʼanizana ndi malo oyera, ndipo anapeza kuti chinali mikono 20 mulitali ndi mikono 20 mulifupi.+ Ndiyeno anandiuza kuti: “Amenewa ndi Malo Oyera Koposa.”+  Kenako anayeza khoma la kachisi ndipo anapeza kuti kuchindikala kwake linali mikono 6. Zipinda zamʼmbali kuzungulira kachisi yenseyo zinali mikono 4 mulifupi.+  Zipinda zamʼmbalizo zinali zosanjikizana katatu ndipo nsanjika iliyonse inali ndi zipinda 30. Kuzungulira khoma la kachisiyo panali timakonde timene tinali ngati maziko a zipinda zamʼmbali moti khoma la zipindazo linaima bwinobwino popanda kubowola khoma la kachisi.+  Mʼmbali zonse za kachisiyo munali masitepe oyenda chozungulira opitira mʼzipinda zamʼmwamba amene ankakulirakulira akamakwera mʼmwamba.+ Zipinda za nsanjika yachitatu zinali zokulirapo kuposa za nsanjika yachiwiri, ndipo zipinda za nsanjika yachiwiri zinali zokulirapo kuposa za nyumba yapansi. Munthu akafuna kupita kuzipinda zamʼmwamba kuchokera kuzipinda zapansi ankadutsa mʼzipinda zapakati.  Ndinaona kuti kachisi yenseyo anamumanga pamaziko okwera. Maziko a zipinda zamʼmbali anali bango lathunthu, yomwe ndi mikono 6, kuchokera pansi kukafika polumikizira.  Khoma lakunja la zipinda zamʼmbali linali lochindikala mikono 5. Panali mpata* kuchokera mʼmphepete mwa maziko kukafika pamene panayambira khoma la zipinda zamʼmbali zimene zinali mbali ya kachisi. 10  Kuchokera pakachisi kukafika kuzipinda zodyera+ panali malo omwe anali mikono 20 mulifupi, kumbali zonse. 11  Pakati pa zipinda zamʼmbali ndi mpata umene unali mbali yakumpoto panali khomo ndipo khomo lina linali mbali yakumʼmwera. Mpatawo unali mikono 5 mulifupi, kuzungulira mbali zonse. 12  Kumadzulo kwa kachisi kunalinso nyumba ina imene inayangʼanizana ndi malo opanda kanthu. Nyumbayi inali mikono 70 mulifupi ndipo mulitali mwake inali mikono 90. Khoma la nyumbayo linali lochindikala mikono 5, kuzungulira nyumba yonseyo. 13  Munthu uja anayeza kachisi nʼkupeza kuti anali mikono 100 mulitali. Ndipo malo opanda kanthu aja, nyumba ija* ndi makoma ake zinalinso mikono 100 mulitali. 14  Mbali yakutsogolo kwa kachisi yomwe inayangʼana kumʼmawa limodzi ndi malo opanda kanthu aja zinali mikono 100 mulifupi. 15  Munthu uja anayeza kumbuyo kwa nyumba yomwe inayangʼanizana ndi malo opanda kanthu aja limodzi ndi timakonde take kumbali zonse ndipo anapeza kuti zinali mikono 100 mulitali. Anayezanso Malo Oyera ndi Malo Oyera Koposa+ komanso makonde a bwalo, 16  malo apafupi ndi khomo, mawindo a mafelemu aakulu mkati koma aangʼono kunja+ ndiponso timakonde timene tinali mʼmalo atatuwo. Pafupi ndi malo apakhomowo anakhomapo matabwa+ kuchokera pansi kufika mʼmawindo, ndipo mawindowo anali otchinga. 17  Anayeza pamwamba pa khomo, kunja ndi mkati mwa kachisi komanso kuzungulira khoma lonse la kachisiyo. 18  Kachisiyo anali ndi zithunzi zojambula mochita kugoba za akerubi+ ndi za mitengo ya kanjedza.+ Mtengo uliwonse wa kanjedza unali pakati pa akerubi awiri ndipo kerubi aliyense anali ndi nkhope ziwiri. 19  Nkhope ya munthu inayangʼana mtengo wa kanjedza kumbali imodzi ndipo nkhope ya mkango* inayangʼana mtengo wa kanjedza kumbali inayo.+ Zithunzizi zinajambulidwa mofanana kuzungulira kachisi yenseyo. 20  Pakhoma la kachisiyo, kuyambira pansi mpaka pamwamba pa khomo, anajambulapo mochita kugoba zithunzi za akerubi ndi za mitengo ya kanjedza. 21  Mafelemu apamakomo a kachisi anali ofanana mbali zonse.*+ Kutsogolo kwa malo oyera* kunali chinachake chooneka ngati 22  guwa lansembe lamatabwa+ limene linali mikono itatu kuchokera pansi kufika pamwamba ndipo mulitali mwake linali mikono iwiri. Guwalo linali ndi zochirikizira mʼmakona ndipo pansi pake* ndiponso mʼmbali mwake munali mwamatabwa. Ndiyeno munthu uja anandiuza kuti: “Ili ndi tebulo limene lili pamaso pa Yehova.”+ 23  Khomo la Malo Oyera linali ndi zitseko ziwiri ndipo khomo la Malo Oyera Koposa linalinso ndi zitseko ziwiri.+ 24  Khomo lililonse linali ndi zitseko ziwiri zimene zinkatheka kuzitsegula. 25  Pazitseko za kachisi panali zithunzi zojambula mochita kugoba za akerubi ndi za mitengo ya kanjedza zofanana ndi zimene zinali mʼmakoma.+ Kutsogolo kwa denga la khonde anakhomako matabwa otulukira kunja. 26  Mʼmbali zonse za khoma lapakhonde komanso mʼzipinda zamʼmbali za kachisi ndi pamatabwawo, munali mawindo a mafelemu aakulu mkati koma aangʼono kunja,+ ndipo anajambulamo zithunzi za mtengo wa kanjedza.

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “kachisi.” Muchaputala 41 ndi 42, mawu amenewa akunena za kunja kwa malo opatulika (Malo Oyera) kapena malo opatulika onsewo (kachisi kuphatikiza Malo Oyera ndi Malo Oyera Koposa).
Imeneyi ndi mikono yaitali. Onani Zakumapeto B14.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmbali mwa khomolo munali.”
Amenewa ndi Malo Oyera Koposa.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mulifupi mwa khomo munali.”
Zikuoneka kuti kameneka kanali kanjira kozungulira kachisiyo.
Imeneyi ndi nyumba imene inali kumʼmawa kwa malo oyera.
Kapena kuti, “mkango wamphamvu wamanyenje.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Felemu lapakhomo la kachisi linali lofanana mbali zonse.” Nʼkutheka kuti akunena za khomo lolowera mʼMalo Oyera.
Nʼkutheka kuti akunena za Malo Oyera Koposa.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mulitali mwake.”