Ezekieli 7:1-27

  • Mapeto afika (1-27)

    • Tsoka loti silinaonekepo (5)

    • Ndalama zidzatayidwa mʼmisewu (19)

    • Kachisi adzaipitsidwa (22)

7  Yehova anandiuzanso kuti:  “Iwe mwana wa munthu, Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wauza dziko la Isiraeli kuti: ‘Mapeto afika! Mapeto afikira mbali zonse za dzikoli.  Mapeto akufikira, ndipo ndisonyeza mkwiyo wanga wonse pa iwe. Ndidzakuweruza mogwirizana ndi njira zako ndiponso kukulanga chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene umachita.  Diso langa silidzakumvera chisoni ndipo sindidzakuchitira chifundo.+ Ndidzakulanga mogwirizana ndi njira zako, moti udzakumana ndi mavuto chifukwa cha zinthu zonyansa zimene ukuchita.+ Udzadziwa kuti ine ndine Yehova.’+  Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Tsoka likubwera! Kukubwera tsoka loti silinaonekepo.+  Mapeto akubwera ndipo afika ndithu. Akufikira modzidzimutsa. Akubwera ndithu.  Inu anthu amene mukukhala mʼdzikoli, mapeto anu afika.* Nthawi ikubwera, tsiku lake layandikira.+ Mʼmapiri mukumveka phokoso lachisokonezo, osati lachisangalalo.  Ndikukhuthulira mkwiyo wanga posachedwapa,+ ndipo ndisonyeza mkwiyo wanga wonse pa iwe.+ Ndidzakuweruza mogwirizana ndi njira zako ndiponso kukulanga chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene umachita.  Diso langa silidzakumvera chisoni ndipo sindidzakuchitira chifundo.+ Ndidzakulanga mogwirizana ndi njira zako moti udzakumana ndi mavuto chifukwa cha zinthu zonyansa zimene ukuchita. Udzadziwa kuti ine Yehova, ndi amene ndikukulanga.+ 10  Taona, tsikulo likubwera.+ Mapeto anu afika.* Ndodo yachita maluwa ndipo kudzikuza kwaphuka. 11  Chiwawa chasanduka ndodo yolangira zinthu zoipa.+ Kaya ndi anthuwo, chuma chawo, kuchuluka kwawo kapena kutchuka kwawo, palibe chimene chidzapulumuke. 12  Nthawi idzakwana ndipo tsikulo lidzafika. Wogula asasangalale ndipo wogulitsa asalire, chifukwa mkwiyo wa Mulungu wayakira gulu lawo lonselo.*+ 13  Wogulitsa sadzabwerera pamalo amene anagulitsa ngakhale atadzapulumuka, chifukwa zinthu zonse zimene zili mʼmasomphenyawo zidzachitikira anthu onse. Palibe amene adzabwerere, ndipo chifukwa cha zolakwa zake,* palibe amene adzapulumutse moyo wake. 14  Iwo aliza lipenga+ ndipo aliyense wakonzeka, koma palibe amene akupita kunkhondo chifukwa mkwiyo wanga wayakira gulu lonselo.+ 15  Lupanga lidzapha anthu amene ali kunja kwa mzinda+ ndipo mliri ndi njala zidzapha amene ali mkati mwa mzinda. Aliyense amene ali kunja kwa mzinda adzaphedwa ndi lupanga ndipo amene ali mumzinda adzafa ndi njala komanso mliri.+ 16  Anthu awo amene adzapulumuke adzathawira kumapiri ndipo mofanana ndi njiwa zamʼzigwa, aliyense adzalira chifukwa cha zolakwa zake.+ 17  Manja awo onse adzafooka ndipo mawondo awo onse azidzangochucha madzi.*+ 18  Iwo avala ziguduli+ ndipo akungonjenjemera. Aliyense adzachititsidwa manyazi ndipo mitu yawo yonse idzakhala ndi mipala.*+ 19  Siliva wawo adzamutaya mʼmisewu ndipo golide wawo adzanyansidwa naye. Siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku limene Yehova adzasonyeze mkwiyo wake waukulu.+ Golide ndi siliva wawo sadzathetsa njala yawo kapena kuwakhutitsa, chifukwa chumacho chakhala ngati chinthu chopunthwitsa chimene chawachititsa kuti achimwe. 20  Iwo ankanyadira kukongola kwa zinthu zawo zodzikongoletsera. Ndipo pogwiritsa ntchito zinthu zimenezi* anapanga mafano awo onyansa.+ Nʼchifukwa chake ndidzachititse kuti zinthu zimenezi adzanyansidwe nazo. 21  Ndidzazipereka* mʼmanja mwa anthu ochokera mʼmayiko ena komanso kwa anthu oipa apadziko lapansi kuti azitenge, ndipo adzaziipitsa. 22  Ine ndidzayangʼana kumbali kuti ndisawaone+ ndipo adzaipitsa malo anga opatulika.* Akuba adzalowa mʼmalowo nʼkuwaipitsa.+ 23  Panga unyolo+ chifukwa anthu osalakwa amene aweruzidwa mopanda chilungamo akuphedwa mʼdziko lonseli+ ndipo mumzinda mwadzaza chiwawa.+ 24  Ndidzabweretsa anthu oipa kwambiri a mitundu ina+ ndipo adzalanda nyumba zawo.+ Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu ndipo malo awo opatulika adzaipitsidwa.+ 25  Anthu akadzayamba kuvutika, azidzafunafuna mtendere koma sadzaupeza.+ 26  Mʼdzikolo mudzakhala mavuto otsatizanatsatizana ndipo muzidzamveka mauthenga otsatizanatsatizana. Anthu azidzafuna kumva masomphenya kuchokera kwa mneneri.+ Koma wansembe sadzathanso kuphunzitsa malamulo* aphindu ndipo anthu achikulire sadzaperekanso malangizo othandiza.+ 27  Mfumu idzayamba kulira+ ndipo mtsogoleri adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu amʼdzikolo adzanjenjemera chifukwa cha mantha. Ndidzawachitira zinthu zogwirizana ndi njira zawo ndipo ndidzawaweruza mogwirizana ndi mmene ankaweruzira ena. Iwo adzadziwa kuti ine ndine Yehova.’”+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “Inu anthu amene mukukhala mʼdzikoli, nkhata yamaluwa ya tsoka ikubwera.”
Mabaibulo ena amati, “Nkhata yamaluwa ya tsoka ikubwera.”
Apa akutanthauza kuti anthu amene amagula kapena kugulitsa zinthu sadzapindula chifukwa onsewo adzawonongedwa.
Mabaibulo ena amati, “pochita zolakwa.”
Kutanthauza kuti adzakodzedwa chifukwa cha mantha.
Kutanthauza kuti adzametedwa tsitsi chifukwa cha chisoni.
Kutanthauza zinthu zawo zopangidwa ndi golide komanso siliva.
Kutanthauza siliva ndi golide wawo amene anagwiritsa ntchito popanga mafano.
Zikuoneka kuti akunena malo amkati kwambiri a nyumba yopatulika ya Yehova.
Kapena kuti, “malangizo.”