Habakuku 1:1-17
1 Uwu ndi uthenga umene ine, mneneri Habakuku,* ndinalandira mʼmasomphenya. Ndinati:
2 “Inu Yehova, kodi ndidzalirira thandizo koma inu osandimva mpaka liti?+
Kodi ndidzapempha thandizo kuti mundipulumutse ku chiwawa koma inu osachitapo kanthu mpaka liti?+
3 Nʼchifukwa chiyani mukundichititsa kuona zinthu zoipa?
Nʼchifukwa chiyani mukulekerera kuponderezana?
Nʼchifukwa chiyani kuwononga zinthu komanso chiwawa zikuchitika pamaso panga?
Ndipo nʼchifukwa chiyani mikangano ndi kumenyana zachuluka?
4 Choncho lamulo latha mphamvu,Ndipo anthu sakuchitanso chilungamo.
Oipa akupondereza anthu olungama,Nʼchifukwa chake chilungamo chikupotozedwa.+
5 Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu ndipo muyangʼanitsitse.
Muyangʼane modabwa. Dabwani ndithu.Chifukwa pali zimene zichitike mʼmasiku anu,Zimene simungakhulupirire ngakhale wina atakufotokozerani.+
6 Ine ndikubweretsa Akasidi,+Mtundu wankhanza ndiponso waphuma.
Umene umathamanga mʼmadera ambiri apadziko lapansi,Kukalanda nyumba zimene si zawo.+
7 Mtundu umenewu ndi woopsa ndiponso wochititsa mantha.
Umapanga malamulo akeake ndipo umadzipatsa wokha ulamuliro.+
8 Mahatchi* ake ndi aliwiro kuposa akambuku,Ndi oopsa kuposa mimbulu usiku.+
Mahatchi ake ankhondo amathamanga kwambiri.Mahatchi awo amachokera kutali.
Ndipo amauluka ngati chiwombankhanga chimene chikuthamanga kuti chikapeze chakudya.+
9 Mtunduwo umabwera wonse kuti udzachite chiwawa.+
Ukakumana pamodzi umayenda ngati mphepo yochokera kumʼmawa,+Ndipo anthu amene wagwira umawakokolola ngati mchenga.
10 Mtunduwu umanyodola mafumu,Ndipo umaseka nduna zapamwamba.+
Umasekanso malo alionse okhala ndi mpanda wolimba,+Ndipo umaunjika dothi kenako nʼkulanda malowo.
11 Kenako mtunduwo umayenda ngati mphepo ndipo umadutsa mʼdziko.Koma udzapalamula,+Chifukwa choganiza kuti mulungu wawo ndi amene wawapatsa mphamvu.”*+
12 Inu Yehova, mwakhala mulipo kuyambira kalekale.+
Inu Mulungu wanga, Mulungu wanga Woyera, inu simufa.*+
Inu Yehova, mwasankha Akasidi kuti apereke chiweruzo chanu.Inu Thanthwe langa,+ mwawasankha kuti mupereke chilango.*+
13 Maso anu ndi oyera kwambiri moti simungaonerere zinthu zoipa,Ndipo simungalekerere khalidwe loipa.+
Ndiye nʼchifukwa chiyani mukulekerera anthu achinyengo,+Komanso mukukhala chete pamene munthu woipa akumeza munthu wolungama kuposa iyeyo?+
14 Nʼchifukwa chiyani mukuchititsa munthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja,Ndiponso ngati zokwawa zimene zilibe mtsogoleri?
15 Iye* amakola zonsezi ndi mbedza,
Ndipo amazikokolola ndi khoka lake.Nʼkuzisonkhanitsa muukonde wophera nsomba.
Nʼchifukwa chake iye amasangalala kwambiri.+
16 Nʼchifukwa chake amapereka nsembe kwa khoka lake,Ndipo amapereka nsembe yautsi kwa ukonde wake wophera nsomba.Iye amatero chifukwa khoka ndi ukondewo zimamuthandiza kupeza chakudya chambiri.*Ndipo chakudya chake ndi chapamwamba.
17 Ndiye kodi adzapitirizabe kukhuthula nsomba zamʼkhoka* lake?
Kodi iye adzapitirizabe kupha mitundu ya anthu mopanda chifundo?+
Mawu a M'munsi
^ Nʼkutheka kuti dzinali limatanthauza “Kukumbatira Mwachikondi.”
^ Ena amati “Mahosi.”
^ Mabaibulo ena amati, “mphamvu zawo, ndi mulungu wawo.”
^ Mabaibulo ena amati, “ife sitidzafa.”
^ Kapena kuti, “kuti mutidzudzule.”
^ Amenewa ndi Akasidi omwe ndi mdani.
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “chonona.”
^ Mabaibulo ena amati, “adzapitirizabe kusolola lupanga lake.”