Hoseya 1:1-11

  • Mkazi wa Hoseya ndiponso ana amene anabereka (1-9)

    • Yezereeli (4), Lo-ruhama (6), ndi Lo-ami (9)

  • Chiyembekezo cha kubwezeretsa komanso mgwirizano (10, 11)

1  Yehova analankhula ndi Hoseya* mwana wa Beeri mʼmasiku a Uziya,+ Yotamu,+ Ahazi+ ndi Hezekiya+ mafumu a Yuda,+ ndiponso mʼmasiku a Yerobowamu+ mwana wa Yowasi+ mfumu ya Isiraeli.  Yehova atayamba kulankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anauza Hoseya kuti: “Pita ukakwatire mkazi amene azidzachita uhule* ndipo ukakhale ndi ana ochokera kwa hule. Chifukwa dzikoli lasiyiratu kutsatira Yehova chifukwa cha uhule.”+  Choncho Hoseya anapita nʼkukakwatira Gomeri, mwana wa Dibulaimu. Kenako Gomeri anakhala ndi pakati ndipo anamuberekera mwana wamwamuna.  Ndiyeno Yehova anauza Hoseya kuti: “Mwanayo umupatse dzina lakuti Yezereeli,* popeza kwatsala nthawi yochepa kuti ndiimbe mlandu nyumba ya Yehu+ chifukwa cha magazi amene Yezereeli anakhetsa. Ndipo ndidzathetsa ufumu wa nyumba ya Isiraeli.+  Mʼmasiku amenewo ndidzathyola uta wa Isiraeli mʼchigwa cha Yezereeli.”  Kenako Gomeri anakhalanso ndi pakati nʼkubereka mwana wamkazi. Ndiyeno Mulungu anauza Hoseya kuti: “Mwanayo umupatse dzina lakuti Lo-ruhama,* chifukwa sindidzachitiranso chifundo+ anthu a mʼnyumba ya Isiraeli, chifukwa ndidzawathamangitsa.+  Koma ndidzachitira chifundo anthu a mʼnyumba ya Yuda+ ndipo Ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.+ Sindidzawapulumutsa ndi nkhondo, uta, lupanga, mahatchi* kapenanso amuna okwera pamahatchi.”+  Gomeri atamusiyitsa mwana wake Lo-ruhama kuyamwa, anakhalanso ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna.  Ndiyeno Mulungu anati: “Mwanayo umupatse dzina lakuti Lo-ami,* chifukwa inu siinu anthu anga ndipo ine sindidzakhala Mulungu wanu. 10  Ndipo Aisiraeli* adzachuluka ngati mchenga wakunyanja umene munthu sangathe kuuyeza kapena kuuwerenga.+ Ndipo kumene ankauzidwa kuti, ‘Siinu anthu anga,’+ adzauzidwa kuti, ‘Ndinu ana a Mulungu wamoyo.’+ 11  Ayuda ndi Aisiraeli adzasonkhanitsidwa pamodzi ndipo adzakhala ogwirizana.+ Iwo adzasankha mtsogoleri mmodzi nʼkutuluka mʼdzikolo chifukwa tsiku limeneli lidzakhala lofunika kwambiri kwa Yezereeli.”+

Mawu a M'munsi

Chidule cha dzina lakuti Hoshaiya limene limatanthauza, “Wopulumutsidwa ndi Ya; Ya Wapulumutsa.”
Kapena kuti, “chiwerewere.”
Kutanthauza “Mulungu Adzadzala Mbewu.”
Kutanthauza “Wosasonyezedwa Chifundo.”
Ena amati “mahosi.”
Kutanthauza, “Si Anthu Anga.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ana a Isiraeli.”