Hoseya 10:1-15

  • Aisiraeli, omwe ndi mtengo wa mpesa wowonongeka, adzawonongedwa (1-15)

    • Kufesa ndiponso kukolola (12, 13)

10  “Isiraeli ndi mtengo wa mpesa wowonongeka* umene ukubereka zipatso.+ Pamene zipatso zake zikuchuluka, mʼpamenenso akumanga maguwa ambiri.+Pamene zokolola zikuchuluka mʼdziko lake, mʼpamenenso akumanga zipilala zopatulika zokongola kwambiri.+   Mtima wawo ndi wachinyengo.Tsopano iwo adzapezeka ndi mlandu. Pali wina amene adzagwetse maguwa awo ansembe ndiponso zipilala zawo zopatulika.   Ndiyeno iwo adzanena kuti, ‘Tilibe mfumu+ chifukwa sitinaope Yehova. Ndipo kodi mfumu ingatichitire chiyani?’   Iwo amalankhula mawu opanda nzeru, amalumbira monama+ ndiponso amachita mapangano.Choncho chiweruzo chimene chikubwera chili ngati zomera zapoizoni mʼmunda.+   Anthu a ku Samariya adzachita mantha ndi fano la mwana wa ngʼombe la ku Beti-aveni.+ Anthu ake adzalilirira.Nawonso ansembe a mulungu wachilendo, amene ankasangalala ndi fanolo komanso ulemerero wake, adzalilirira.Chifukwa lidzatengedwa kupita kudziko lina.   Wina adzapita nalo kudziko la Asuri nʼkukalipereka ngati mphatso kwa mfumu yaikulu.+ Efuraimu adzachititsidwa manyazi,Ndipo Isiraeli adzachita manyazi chifukwa cha malangizo amene ankatsatira.+   Samariya pamodzi ndi mfumu yake adzawonongedwa,*+Ngati kanthambi kothyoledwa mumtengo kamene kakuyandama pamadzi.   Malo okwezeka a ku Beti-aveni,+ omwe ndi tchimo la Isiraeli,+ adzawonongedwa.+ Minga ndi zitsamba zobaya zidzamera pamaguwa awo ansembe.+ Anthu adzauza mapiri kuti, ‘Tikwirireni!’ Adzauzanso mapiri angʼonoangʼono kuti, ‘Tigwereni!’+   Inu Aisiraeli, mwakhala mukuchimwa kuyambira pa nthawi ya zochitika za ku Gibeya.+ Kumeneko anthu anapitirizabe kuchimwa. Nkhondo sinawononge anthu onse osalungama ku Gibeya. 10  Ndikadzafuna ndidzawalanga. Anthu a mitundu ina adzasonkhana kuti alimbane nawo,Pamene adzamangiriridwa goli la zolakwa zawo ziwiri.* 11  Efuraimu anali ngʼombe* yophunzitsidwa bwino yokonda kupuntha mbewu,Choncho ine sindinawononge khosi lake lokongola. Koma ndidzachititsa kuti wina akwere pamsana pa Efuraimu.+ Yuda adzalima, Yakobo adzamusalazira zibulumwa za dothi. 12  Dzalani mbewu zachilungamo ndipo kololani chikondi chokhulupirika. Limani munda panthaka yabwino,+Pamene muli ndi nthawi yofunafuna Yehova,+Mpaka iye atabwera nʼkukulangizani mwachilungamo.+ 13  Koma mwalima zoipa,Ndipo mwakolola zosalungama.+Mwadya zipatso za chinyengo chanu.Chifukwa mukudalira njira zanu,Ndiponso kuchuluka kwa asilikali anu. 14  Pakati pa anthu a mtundu wanu padzakhala chisokonezo.Ndipo mizinda yanu yonse yokhala ndi mipanda yolimba idzawonongedwa,+Ngati mmene Salimani anawonongera Beti-aribeliPa tsiku lankhondo, pamene azimayi ndi ana awo anawanyenyanyenya. 15  Inu anthu a ku Beteli, wina adzakuchitaninso zimenezi+ chifukwa ndinu oipa kwambiri. Ndithu, mfumu ya Isiraeli idzawonongedwa* mʼbandakucha.”+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “wotambalala.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “adzakhalitsidwa chete.”
Kutanthauza pamene adzanyamula chilango chawo ngati goli.
Kutanthauza ngʼombe yaikazi yoti sinaberekepo.
Mʼchilankhulo choyambirira, “idzakhalitsidwa chete.”