Hoseya 11:1-12

  • Mulungu anakonda Isiraeli kuyambira ali mnyamata (1-12)

    • ‘Ndinaitana mwana wanga kuti atuluke mu Iguputo’ (1)

11  “Isiraeli ali mnyamata ndinamukonda,+Ndipo ndinaitana mwana wangayu kuti atuluke mu Iguputo.+   Pamene iwo* ankawaitana kwambiri,Mʼpamenenso iwo ankawathawa kwambiri.+ Ankapereka nsembe kwa zifaniziro za Baala,+Ndipo nsembezo ankaziperekanso kwa zifaniziro zogoba.+   Koma ndine amene ndinaphunzitsa Efuraimu kuyenda,+ ndipo ndinkamunyamula mʼmanja mwanga+Koma iye sanavomereze kuti ndinamuchiritsa.   Ndinkawakoka mokoma mtima ndiponso mwachikondi,*+Kwa iwo ndinali ngati wochotsa goli mʼkhosi* mwawo,Ndipo mwachikondi ndinkabweretsera aliyense chakudya.   Iwo sadzabwerera kudziko la Iguputo, koma Asuri adzakhala mfumu yawo,+Chifukwa anakana kubwerera kwa ine.+   Lupanga lidzazungulira mʼmizinda yake+Ndipo lidzawononga mipiringidzo nʼkupha anthu chifukwa cha zoipa zimene ankafuna kuchita.+   Anthu anga atsimikiza kuti akhale osakhulupirika kwa ine.+ Ngakhale kuti anawaitanira kumwamba,* palibe amene anaimirira.   Kodi ndikusiye chifukwa chiyani iwe Efuraimu?+ Kodi ndikupereke kwa adani chifukwa chiyani iwe Isiraeli? Kodi ndikuchitire zinthu ngati Adima chifukwa chiyani? Kodi ndikusinthirenji kukhala ngati Zeboyimu?+ Koma ndasintha maganizoNdipo ndayamba kukumvera chisoni.+   Sindidzasonyeza mkwiyo wanga woyaka moto. Sindidzawononganso Efuraimu+Chifukwa ndine Mulungu, osati munthu.Ndine Woyera pakati panu,Ndipo sindidzabwera kwa inu nditakwiya. 10  Iwo adzatsatira Yehova ndipo iye adzabangula ngati mkango.+Ndipo akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.+ 11  Iwo adzabwera akunjenjemera ngati mbalame akamadzachokera ku Iguputo.Adzabwera ngati njiwa kuchokera kudziko la Asuri.+Ndipo ndidzawachititsa kukhazikika mʼnyumba zawo,” watero Yehova.+ 12  “Efuraimu amandiuza mabodza okhaokha.Kulikonse kumene ndingayangʼane, ndikuona chinyengo cha Isiraeli.+ Koma Yuda akuyendabe ndi Mulungu,Ndipo iye ndi wokhulupirika kwa Woyera Koposa.”+

Mawu a M'munsi

Kutanthauza aneneri ndi anthu ena amene ankatumidwa kuti akalangize Aisiraeli.
Kapena kuti, “zingwe za kukoma mtima,” ngati zimene kholo limagwiritsa ntchito likamaphunzitsa mwana kuyenda.
Mʼchilankhulo choyambirira, “munsagwada.”
Kapena kuti, “anawaitana kuti ayambirenso kulambira koona.”