Malaki 2:1-17

  • Ansembe ankalephera kulangiza anthu (1-9)

    • Ansembe ankayenera kuphunzitsa anthu za Mulungu (7)

  • Anthu ankathetsa mabanja pa zifukwa zosamveka (10-17)

    • “‘Ndimadana ndi zoti anthu azithetsa mabanja,’ watero Yehova” (16)

2  “Tsopano inu ansembe, lamulo ili ndi lanu.+  Mukakana kumvera ndiponso kuganizira nkhani imeneyi mumtima mwanu kuti mulemekeze dzina langa, ndidzakutumizirani temberero+ ndipo madalitso anu ndidzawasandutsa matemberero. Madalitso ndawasandutsa matemberero+ chifukwa nkhani imeneyi simunaiganizire mumtima mwanu,” watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.  “Tamverani! Chifukwa cha inu, ndiwononga mbewu zanu zomwe mwadzala+ ndipo ndikuwazani ndowe kumaso. Ndikuwazani ndowe za nyama zimene mumapereka nsembe pa zikondwerero zanu. Ndipo mudzanyamulidwa nʼkukaponyedwa pandowezo.*  Zikadzatero mudzadziwa kuti ine ndakupatsani lamulo limeneli kuti pangano limene ndinachita ndi Levi lipitirire,”+ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.  “Pangano limene ndinachita naye linali loti ndinamupatsa moyo ndi mtendere kuti azindiopa. Iye ankandiopa ndipo ankalemekeza dzina langa.  Ankaphunzitsa lamulo la choonadi+ ndipo sanalankhulepo zinthu zoipa. Ankayenda ndi ine mwamtendere komanso mowongoka mtima+ ndipo anabweza anthu ambiri panjira yolakwika.  Wansembe ayenera kuphunzitsa anthu za Mulungu. Anthu ayenera kupita kwa iye kuti akamve Chilamulo*+ chifukwa iye ndi mthenga wa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.  Koma inu mwasiya kuyenda panjira yoyenera. Mwachititsa kuti anthu ambiri asiye kutsatira Chilamulo.*+ Ndipo mwaphwanya pangano limene ndinachita ndi Levi,”+ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.  “Choncho ine ndidzachititsa kuti inu mukhale anthu onyozeka ndi otsika kwa anthu onse, chifukwa simunayende mʼnjira zanga, koma munkakondera pa nkhani zokhudza kutsatira Chilamulo.”+ 10  “Kodi tonsefe atate wathu si mmodzi?+ Kodi si Mulungu mmodzi amene anatilenga? Ndiye nʼchifukwa chiyani tikuchitirana zachinyengo+ nʼkumaipitsa pangano la makolo athu akale? 11  Yuda wachita zachinyengo, ndipo mu Isiraeli ndi mu Yerusalemu mwachitika zinthu zonyansa. Chifukwa Yuda wadetsa chiyero* cha Yehova+ chimene Mulungu amachikonda, ndipo Yuda wakwatira mwana wamkazi wa mulungu wachilendo.+ 12  Yehova adzapha munthu aliyense wochita zimenezi mʼmatenti a Yakobo, kaya akhale ndani.* Adzachita zimenezi ngakhale zitakhala kuti munthuyo amapereka nsembe ngati mphatso kwa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.”+ 13  “Pali chinthu chinanso chimene anthu inu mukuchita ndipo chikuchititsa kuti guwa lansembe la Yehova lidzaze ndi misozi, kulira ndi kubuula. Chifukwa cha zimenezi, nsembe zanu zimene mumapereka ngati mphatso nʼzosavomerezeka kwa iye ndipo sakusangalala ndi chilichonse chochokera mʼmanja mwanu.+ 14  Inu mwanena kuti, ‘Chifukwa chiyani?’ Chifukwa chakuti Yehova ndi mboni pakati pa inu ndi mkazi amene munamukwatira muli mnyamata, yemwe mwamuchitira zachinyengo ngakhale kuti iye ndi mnzanu komanso mkazi wa pangano.*+ 15  Komabe pali ena amene sanachite zimenezi chifukwa ali ndi mzimu woyera wa Mulungu. Iwo akufuna kukhala ndi ana amene angakhaledi anthu* a Mulungu. Choncho samalani kuti mukhale ndi maganizo oyenera ndipo musachitire zachinyengo akazi anu amene munawakwatira muli anyamata. 16  Chifukwa ine ndimadana ndi zoti anthu azithetsa mabanja,”+ watero Yehova Mulungu wa Isiraeli. “Ndimadana ndi munthu wankhanza.* Samalani kuti mukhale ndi maganizo oyenera ndipo musamachite zachinyengo,”+ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba. 17  “Inu mwatopetsa Yehova ndi mawu anu.+ Koma mukunena kuti, ‘Tamutopetsa bwanji?’ Ponena kuti, ‘Aliyense wochita zoipa ndi wabwino kwa Yehova ndipo amasangalala naye,’+ kapena ponena kuti, ‘Kodi Mulungu wachilungamo ali kuti?’”

Mawu a M'munsi

Kutanthauza pamalo omwe ankatayapo ndowezo.
Kapena kuti, “malangizo.”
Mabaibulo ena amati, “malangizo anu.”
Mabaibulo ena amati, “malo opatulika.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “amene ali maso ndiponso amene akuyankha.”
Kapena kuti, “amene munamukwatira mwalamulo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “amene amaphimba zovala zake ndi chiwawa.”