Wolembedwa ndi Maliko 11:1-33

  • Yesu analowa mumzinda mwaulemerero (1-11)

  • Anatemberera mtengo wamkuyu (12-14)

  • Yesu anayeretsa kachisi (15-18)

  • Zimene tikuphunzira pa mtengo wamkuyu umene unafota (19-26)

  • Anatsutsa ulamuliro wa Yesu (27-33)

11  Iwo atayandikira ku Yerusalemu, ku Betefage ndi ku Betaniya+ paphiri la Maolivi, Yesu anatumiza ophunzira ake awiri.+  Iye anawauza kuti: “Pitani mʼmudzi umene mukuuonawo ndipo mukakangolowa mmenemo, mukapeza bulu wamngʼono wamphongo atamumangirira, amene munthu sanakwerepo chiyambire. Mukamumasule nʼkubwera naye kuno.  Wina akakakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumasula buluyu?’ Mukanene kuti, ‘Ambuye akumufuna ndipo akangotha kumugwiritsa ntchito adzamubweza nthawi yomweyo.’”  Choncho iwo ananyamuka ndipo anapezadi bulu wamphongo atamumangirira pakhomo, mʼmphepete mwa msewu waungʼono. Ndipo iwo anamasula buluyo.+  Koma ena mwa anthu amene anali ataimirira chapomwepo anawafunsa kuti: “Cholinga chanu nʼchiyani pomasula buluyu?”  Iwo anawauza zimene Yesu ananena ndipo anawalola kuti apite.  Anthuwo anabweretsa bulu uja+ kwa Yesu. Kenako anayala malaya awo akunja pabuluyo ndipo iye anakwerapo.+  Komanso anthu ambiri anayala malaya awo akunja mumsewu ndipo ena anadula masamba mʼminda.+  Ndiyeno amene anali patsogolo komanso amene ankabwera mʼmbuyo ankafuula kuti: “Mʼpulumutseni!+ Wodalitsidwa ndi amene akubwera mʼdzina la Yehova!*+ 10  Wodalitsidwa ndi Ufumu wa atate wathu Davide+ umene ukubwerawo! Mʼpulumutseni kumwambamwambako!” 11  Iye analowa mu Yerusalemu nʼkufika mʼkachisi. Ndiyeno anayangʼanayangʼana zinthu zonse, koma popeza nthawi inali itatha kale, anapita ku Betaniya limodzi ndi ophunzira ake 12 aja.+ 12  Tsiku lotsatira, pamene ankachoka ku Betaniya, anamva njala.+ 13  Ndiye ali chapatali ndithu, anaona mtengo wamkuyu umene unali ndi masamba. Iye anapita pomwepo kuti akaone ngati angapezemo kanthu. Koma atafika pamtengowo, sanapezemo chilichonse koma masamba okha basi, chifukwa sinali nyengo ya nkhuyu. 14  Choncho iye anauza mtengowo kuti: “Munthu sadzadyanso zipatso zako mpaka kalekale.”+ Ndipo ophunzira ake ankamvetsera. 15  Tsopano iwo anafika ku Yerusalemu. Kumeneko analowa mʼkachisi nʼkuyamba kuthamangitsa anthu amene ankagulitsa ndi kugula zinthu mʼkachisimo, ndipo anagubuduza matebulo a anthu amene ankasintha ndalama komanso mabenchi a anthu amene ankagulitsa nkhunda.+ 16  Iye sanalole aliyense kuti adutse mʼkachisimo atanyamula katundu. 17  Iye ankaphunzitsa ndipo ankauza anthuwo kuti: “Kodi Malemba sanena kuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yopemphereramo anthu a mitundu yonseʼ?+ Koma inu mwaisandutsa phanga la achifwamba.”+ 18  Ansembe aakulu ndi alembi anamva zimenezo, ndipo anayamba kufunafuna njira yoti amuphere+ chifukwa ankamuopa popeza gulu lonse la anthu linkadabwa ndi zimene ankaphunzitsa.+ 19  Chakumadzulo kwa tsikulo, iwo anatuluka mumzindawo. 20  Koma mʼmamawa pamene ankadutsa, anaona kuti mtengo wamkuyu uja wafota kale ndi mizu yomwe.+ 21  Choncho Petulo, anaukumbukira ndipo ananena kuti: “Rabi, taonani! Mtengo wamkuyu umene munautemberera uja wafota.”+ 22  Yesu anawayankha kuti: “Muzikhulupirira Mulungu. 23  Ndithu ndikukuuzani kuti aliyense wouza phiri ili kuti, ‘Nyamuka pano ukadziponye mʼnyanja,’ ndipo sakukayikira mumtima mwake koma ali ndi chikhulupiriro kuti zimene wanena zichitikadi, zidzaterodi.+ 24  Nʼchifukwa chake ndikukuuzani kuti, zinthu zonse zimene mukupempha ndi kuzipempherera, muzikhulupirira kuti mwazilandira kale ndipo mudzazilandiradi.+ 25  Ndipo mukaimirira nʼkumapemphera, muzikhululuka chilichonse chimene wina anakulakwirani kuti Atate wanu wakumwamba akukhululukireninso machimo anu.”+ 26 *⁠—— 27  Kenako anafikanso ku Yerusalemu. Ndipo pamene ankayenda mʼkachisi, ansembe aakulu, alembi ndi akulu anabwera 28  nʼkumufunsa kuti: “Kodi muli ndi ulamuliro wochitira zinthu zimenezi? Kapena ndi ndani amene anakupatsani ulamuliro umenewu?”+ 29  Yesu anawayankha kuti: “Ndikufunsani funso limodzi. Mundiyankhe, ndipo inenso ndikuuzani amene anandipatsa ulamuliro umene ndimachitira zimenezi. 30  Kodi ubatizo umene Yohane ankachita+ unali wochokera kumwamba kapena kwa anthu? Ndiyankheni.”+ 31  Choncho iwo anayamba kukambirana kuti: “Tikanena kuti, ‘Unachokera kumwamba,’ atifunsa kuti, ‘Nanga nʼchifukwa chiyani simunamukhulupirire?’ 32  Koma tinganene kuti ‘Unachokera kwa anthuʼ ngati?” Iwo ankaopa gulu la anthu, chifukwa anthu onsewo ankakhulupirira kuti Yohane analidi mneneri.+ 33  Choncho iwo anayankha Yesu kuti: “Sitikudziwa.” Yesu anawauza kuti: “Inenso sindikuuzani amene anandipatsa ulamuliro umene ndimachitira zimenezi.”

Mawu a M'munsi