Wolembedwa ndi Maliko 5:1-43

  • Yesu anatumiza ziwanda munkhumba (1-20)

  • Mwana wamkazi wa Yairo; mzimayi amene anagwira malaya akunja a Yesu (21-43)

5  Kenako iwo anafika kutsidya lina la nyanja, mʼdera la Agerasa.+  Ndipo Yesu atangotsika mʼngalawa, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi mzimu wonyansa akuchokera mʼmanda.*  Iye ankakonda kukhala mʼmandamo, ndipo kuyambira kalekale panalibe munthu aliyense amene anakwanitsa kumumanga ngakhale ndi unyolo koma iye osadula.  Iye anamangidwapo ndi matangadza ndiponso maunyolo mobwerezabwereza, koma ankadula maunyolowo ndiponso kuthyola matangadzawo moti panalibe amene anatha kumugonjetsa.  Ndipo nthawi zonse, usiku ndi masana, ankafuula mʼmanda ndi mʼmapiri komanso ankadzitematema ndi miyala.  Koma ataona Yesu chapatali ndithu, anamuthamangira nʼkumugwadira.+  Kenako anafuula ndi mawu amphamvu kuti: “Kodi mukufuna chiyani kwa ine, Yesu, Mwana wa Mulungu Wamʼmwambamwamba? Ndikukulumbiritsani pali Mulungu kuti musandizunze.”+  Chifukwa Yesu ankauza mzimuwo kuti: “Tuluka mwa munthuyu, mzimu wonyansa iwe.”+  Ndiyeno Yesu anafunsa munthuyo kuti: “Dzina lako ndi ndani?” Iye anayankha kuti: “Dzina langa ndi Khamu, chifukwa tilipo ambiri.” 10  Ndipo anapitiriza kuchonderera Yesu kuti asatumize mizimuyo kutali ndi deralo.+ 11  Ndiyeno chigulu cha nkhumba+ chinkadya mʼmbali mwa phiri.+ 12  Choncho mizimuyo inamuchonderera kuti: “Titumizeni munkhumbazo kuti tikalowe mmenemo.” 13  Choncho iye anailola. Atatero mizimu yonyansayo inatuluka nʼkukalowa munkhumbazo ndipo nkhumba zonsezo zinathamangira kuphedi* nʼkulumphira mʼnyanja. Nkhumbazo zinalipo pafupifupi 2,000 ndipo zinamira mʼnyanjamo. 14  Koma abusa a ziwetozo anathawa nʼkukanena zimenezi mumzinda ndi mʼmidzi, ndipo anthu anabwera kudzaona zimene zinachitikazo.+ 15  Choncho anafika kwa Yesu ndipo anaona munthu amene anagwidwa ndi chiwanda uja, amene poyamba anali ndi gulu la mizimu yonyansa. Anamuona atakhala pansi, atavala bwinobwino komanso maganizo ake ali bwinobwino ndipo iwo anachita mantha. 16  Komanso amene anaona zimene zinachitikazo, anafotokozera anthuwo zimene zinachitikira munthu wogwidwa ndi ziwanda uja ndiponso nkhumba zija. 17  Choncho anthuwo anayamba kuchonderera Yesu kuti achoke mʼdera lakwawoko.+ 18  Ndiyeno Yesu akukwera ngalawa, munthu amene anali ndi ziwanda uja anamuchonderera kuti apite nawo.+ 19  Yesu sanamulole koma anamuuza kuti: “Pita kunyumba kwa achibale ako ndipo ukawauze zonse zimene Yehova* wakuchitira ndi chifundo chimene wakusonyeza.” 20  Choncho munthu uja anachoka ndipo anayamba kufalitsa mu Dekapoli* zonse zimene Yesu anamuchitira, moti anthu onse anadabwa kwambiri. 21  Yesu atawolokanso pangalawa kubwerera kutsidya lina, gulu lalikulu la anthu linasonkhana kwa iye, pa nthawiyi iye anali mʼmphepete mwa nyanja.+ 22  Kenako mmodzi wa atsogoleri a sunagoge, dzina lake Yairo, anafika. Atamuona anagwada pamapazi ake.+ 23  Iye anamuchonderera mobwerezabwereza kuti: “Mwana wanga wamkazi akudwala mwakayakaya.* Chonde tiyeni mukamuike manja+ kuti achire nʼkukhala ndi moyo.” 24  Zitatero Yesu ananyamuka naye limodzi, ndipo gulu lalikulu la anthu linkamutsatira nʼkumamupanikiza. 25  Tsopano panali mayi wina amene ankadwala matenda otaya magazi+ kwa zaka 12.+ 26  Madokotala ambiri anamuchititsa kuti avutike kwambiri.* Iye anawononga chuma chake chonse koma sanachire, mʼmalomwake matendawo ankangokulirakulira. 27  Atamva zokhudza Yesu, anakalowa mʼgulu la anthulo nʼkumudzera kumbuyo kwake, kenako anagwira malaya ake akunja.+ 28  Anachita zimenezi chifukwa mumtima mwake ankanena kuti: “Ndikangogwira malaya ake akunja okhawo, ndichira ndithu.”+ 29  Nthawi yomweyo anasiya kutaya magazi ndipo mʼthupi mwake anamva kuti wachira matenda ake aakuluwo. 30  Nthawi yomweyo, Yesu anazindikira kuti mphamvu+ yatuluka mʼthupi mwake ndipo anatembenuka mʼgulu la anthulo nʼkufunsa kuti: “Ndi ndani wagwira malaya anga akunjawa?”+ 31  Koma ophunzira ake anamuuza kuti: “Inunso mukuona kuti anthu onsewa akukupanikizani, ndiye mungafunse bwanji kuti, ‘Ndi ndani wandigwira?’” 32  Komabe iye ankayangʼanayangʼana kuti aone amene wachita zimenezi. 33  Mayi uja anachita mantha nʼkuyamba kunjenjemera atadziwa zimene zamuchitikira ndipo anafika pafupi nʼkugwada pamaso pake nʼkumuuza zoona zonse. 34  Iye anauza mayiyo kuti: “Mwanawe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere+ ndipo matenda ako aakuluwo atheretu.”+ 35  Ali mkati molankhula, panafika amuna ena ochokera kunyumba kwa mtsogoleri wa sunagoge uja ndipo anamuuza kuti: “Mwana wanu uja wamwalira! Musiyeni Mphunzitsiyu musamuvutitse.”+ 36  Koma Yesu anamva zimene ankanenazo ndipo anauza mtsogoleri wa sunagogeyo kuti: “Usaope, ingokhala ndi chikhulupiriro basi.”+ 37  Pa nthawiyo sanalolenso aliyense kuti amutsatire kupatulapo Petulo, Yakobo ndi Yohane, amene ndi mchimwene wake wa Yakobo.+ 38  Choncho anafika kunyumba ya mtsogoleri wa sunagoge ndipo anamva chiphokoso cha anthu akulira komanso kubuma kwambiri.+ 39  Atalowa mkati, anafunsa anthuwo kuti: “Nʼchifukwa chiyani mukupanga phokoso komanso kulira chonchi? Mwanayu sanamwalire, koma akugona.”+ 40  Atanena zimenezi, anthuwo anayamba kumuseka monyoza. Koma atawatulutsa onsewo, anatenga bambo ndi mayi a mwanayo komanso anthu amene anali naye aja, ndipo analowa kumene kunali mwanayo. 41  Ndiyeno anagwira dzanja la mwanayo nʼkunena kuti: “Talʹi·tha cuʹmi,” mawu amene akamasuliridwa amatanthauza kuti: “Kamtsikana iwe, ndikunena ndi iwe, dzuka!”+ 42  Nthawi yomweyo mtsikanayo anadzuka nʼkuyamba kuyenda. (Mtsikanayo anali ndi zaka 12.) Ndipo anthuwo anasangalala kwambiri. 43  Koma iye anawalamula mobwerezabwereza* kuti asauze aliyense zimenezi.+ Kenako anawauza kuti apatse mtsikanayo chakudya.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mʼmanda achikumbutso.”
Kapena kuti, “kuphompho.”
Kapena kuti, “Chigawo cha Mizinda 10.”
Kapena kuti, “watsala pangʼono kufa.”
Kapena kuti, “anamuchititsa kuti amve zopweteka zambiri.”
Kapena kuti, “anawalamula mwamphamvu.”