Wolembedwa ndi Maliko 7:1-37

  • Anadzudzula miyambo ya anthu (1-13)

  • Zinthu zimene zimaipitsa munthu zimachokera mumtima (14-23)

  • Chikhulupiriro cha mayi wa Chisurofoinike (24-30)

  • Munthu amene anali ndi vuto losamva anachiritsidwa (31-37)

7  Tsopano Afarisi ndi alembi ena amene anachokera ku Yerusalemu anasonkhana kwa Yesu.+  Ndiyeno iwo anaona ena mwa ophunzira ake akudya chakudya ndi manja oipitsidwa, kapena kuti mʼmanja mosasamba.*  (Afarisi ndi Ayuda onse sadya asanasambe mʼmanja mpaka mʼzigongono, potsatira mwambo wa makolo.  Ndipo akabwera kuchokera kumsika, sadya mpaka atasamba. Pali miyambo inanso yambiri imene anailandira ndipo akuitsatira, monga kuviika mʼmadzi makapu, mitsuko ndi ziwiya zakopa.*)+  Choncho Afarisi ndi alembi amenewa anamufunsa kuti: “Nʼchifukwa chiyani ophunzira anu satsatira miyambo ya makolo, koma amadya chakudya ndi manja oipitsidwa?”+  Iye anawayankha kuti: “Yesaya analosera zolondola zokhuza anthu achinyengo inu, mogwirizana ndi zimene Malemba amanena kuti, ‘Anthu awa amandilemekeza ndi milomo yokha, koma mitima yawo aiika kutali ndi ine.+  Chilichonse chomwe amachita pondilambira ndi chopanda pake, chifukwa amaphunzitsa malamulo a anthu ngati kuti ndi malamulo a Mulungu.’+  Mumanyalanyaza malamulo a Mulungu nʼkumaumirira miyambo ya anthu.”+  Komanso anawauza kuti: “Mochenjera, mumanyalanyaza malamulo a Mulungu kuti musunge miyambo yanu.+ 10  Mwachitsanzo, Mose ananena kuti, ‘Muzilemekeza bambo anu ndi mayi anu,’+ komanso anati, ‘Aliyense wolankhula mawu achipongwe kwa bambo ake kapena mayi ake aziphedwa.’+ 11  Koma inu mumanena kuti, ‘Munthu akauza bambo ake kapena mayi ake kuti: “Chilichonse chimene ndili nacho, chimene ndikanakuthandizani nacho ndi khobani (kutanthauza, mphatso yoti ndipereke kwa Mulungu),”’ 12  inu simulolanso kuti munthuyo achitire bambo ake kapena mayi ake chinthu chilichonse.+ 13  Mukamachita zimenezi, mumapangitsa kuti mawu a Mulungu akhale opanda pake chifukwa cha miyambo yanu imene munaipereka kwa anthu.+ Ndipo mumachita zinthu zambiri ngati zimenezi.”+ 14  Atatero, anaitana gulu la anthuwo kuti abwerenso kwa iye ndipo anawauza kuti: “Mvetserani kuno nonsenu, ndipo mumvetse tanthauzo lake.+ 15  Palibe chilichonse chochokera kunja kwa munthu nʼkulowa mʼthupi mwake chimene chingaipitse munthu. Koma zinthu zimene zimatuluka mwa munthu ndi zimene zimaipitsa munthu.”+ 16 *⁠—— 17  Tsopano atalowa mʼnyumba ina kutali ndi gulu la anthulo, ophunzira ake anayamba kumufunsa za fanizo lija.+ 18  Choncho iye anawafunsa kuti: “Kodi nanunso ndinu osazindikira ngati iwo aja? Kodi simukudziwa kuti palibe chochokera kunja kwa thupi nʼkulowa mʼthupi mwa munthu chimene chingamuipitse? 19  Zili choncho chifukwa sichidutsa mumtima mwake koma mʼmatumbo mwake, ndipo chimakatuluka kuchimbudzi.” Ndi mawu amenewa Yesu anagamula kuti zakudya zonse nʼzoyera. 20  Iye ananenanso kuti: “Chotuluka mʼthupi la munthu nʼchimene chimaipitsa munthu.+ 21  Chifukwa mumtima mwa anthu+ mumatuluka maganizo oipa ngati: zachiwerewere,* zakuba, zopha anthu, 22  zachigololo, dyera, kuchita zoipa, chinyengo, khalidwe lopanda manyazi,* diso la kaduka, mawu onyoza, kudzikweza ndiponso kuchita zinthu mopanda nzeru. 23  Zoipa zonsezi zimatuluka mumtima mwa munthu ndipo zimamuipitsa.” 24  Atachoka kumeneko anapita mʼchigawo cha Turo ndi Sidoni.+ Kumeneko anakalowa mʼnyumba ina ndipo sanafune kuti aliyense adziwe kuti ali kumeneko. Koma anthu anadziwabe. 25  Nthawi yomweyo, mayi wina amene mwana wake wamkazi anagwidwa ndi mzimu wonyansa anamva za iye ndipo anabwera nʼkudzagwada pamapazi ake.+ 26  Mayiyu anali Mgiriki, wa Chisurofoinike. Iye anapempha Yesu mobwerezabwereza kuti atulutse chiwanda mwa mwana wakeyo. 27  Koma Yesu anauza mayiyo kuti: “Choyamba, zimafunika kuti ana akhute kaye, chifukwa si bwino kutenga chakudya cha ana nʼkuponyera tiagalu.”+ 28  Koma mayiyo anamuyankha kuti: “Inde mbuyanga, komatu tiagalu timadya nyenyeswa za anawo pansi pa tebulo.” 29  Yesu atamva zimenezo anauza mayiyo kuti: “Chifukwa chakuti wanena zimenezi, pita, chiwandacho chatuluka mwa mwana wakoyo.”+ 30  Choncho anapita kunyumba kwake ndipo anakapeza mwanayo atagona pabedi chiwandacho chitatuluka.+ 31  Pamene Yesu ankachoka mʼchigawo cha Turo kupita kunyanja ya Galileya, anadutsa ku Sidoni komanso mʼchigawo cha Dekapoli.*+ 32  Kumeneko anthu anamubweretsera munthu wa vuto losamva komanso wovutika kulankhula.+ Iwo anamupempha kuti aike dzanja lake pa munthuyo. 33  Koma iye anatenga munthuyo nʼkuchoka naye pagulu la anthulo kupita naye pambali. Kenako anapisa zala zake mʼmakutu a munthuyo, ndipo atalavulira pazala zake anakhudza lilime la munthuyo.+ 34  Atatero anayangʼana kumwamba nʼkuusa moyo mwamphamvu, kenako anauza munthuyo kuti: “Efata,” kutanthauza kuti, “Tseguka.” 35  Atatero, makutu ake anatseguka+ ndipo vuto lake losalankhulalo linatheratu, moti anayamba kulankhula bwinobwino. 36  Ndiyeno anawalamula kuti asauze aliyense zimene zinachitikazo.+ Koma ankati akawaletsa mwamphamvu kuti asauze aliyense, mʼpamenenso iwo ankazifalitsa kwambiri.+ 37  Inde, iwo anadabwa kwambiri+ ndipo ananena kuti: “Wachita zinthu zonse bwinobwino ndithu. Ngakhale anthu amene anali ndi vuto losamva akumva komanso amene anali ndi vuto losalankhula akulankhula.”+

Mawu a M'munsi

Izi sizikutanthauza kuti ankadya chakudya ndi mʼmanja mwakuda koma kuti sankatsatira miyambo ya Chiyuda yosambira mʼmanja.
Kapena kuti, “zamkuwa.”
MʼChigiriki por·nei′a. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
MʼChigiriki a·sel′gei·a. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti, “Chigawo cha Mizinda 10.”