Maliro 4:1-22

  • Mavuto oopsa amene Yerusalemu anakumana nawo atazunguliridwa ndi adani

    • Kusowa kwa chakudya (4, 5, 9)

    • Azimayi anaphika ana awo (10)

    • Yehova anakhuthula mkwiyo wake (11)

א [Aleph] 4  Golide amene anali wowala komanso woyengedwa bwino,+ sakuwalanso. Miyala yopatulika+ yamwazika pamphambano zonse za misewu.+ ב [Beth]   Ana okondedwa a Ziyoni amene anali amtengo wapatali ngati golide woyengedwa bwino,Tsopano akuonedwa ngati mitsuko ikuluikulu yadothi,Ntchito ya manja a munthu woumba mbiya. ג [Gimel]   Ngakhale mimbulu imapereka bere kwa ana ake kuti ayamwe,Koma mwana wamkazi wa anthu anga wakhala wankhanza+ ngati nthiwatiwa zamʼchipululu.+ ד [Daleth]   Lilime la mwana woyamwa lamamatira kummero chifukwa cha ludzu. Ana akupempha chakudya+ koma palibe amene akuwapatsa.+ ה [He]   Anthu amene ankadya chakudya chabwino agona mʼmisewu chifukwa cha njala.+ Anthu amene ankavala zovala zamtengo wapatali+ kuyambira ali ana, agona pamilu yaphulusa. ו [Waw]   Chilango chimene mwana wamkazi wa anthu anga walandira nʼchachikulu kuposa chimene mzinda wa Sodomu unalandira chifukwa cha machimo ake.+Mzinda umenewu unawonongedwa mʼkanthawi kochepa, ndipo panalibe dzanja limene linauthandiza.+ ז [Zayin]   Anaziri ake+ anali oyera kwambiri, anali oyera kuposa mkaka. Anali ofiira kuposa miyala yamtengo wapatali ya korali. Anali onyezimira ngati miyala ya safiro. ח [Heth]   Tsopano ayamba kuoneka akuda kuposa makala.Anthu sakuthanso kuwazindikira mʼmisewu. Khungu lawo lafota moti lamamatira kumafupa awo.+ Langoti gwaa ngati mtengo wouma. ט [Teth]   Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kusiyana ndi amene anafa ndi njala.+Amenewa anafooka nʼkufa chifukwa chosowa chakudya ndipo anafa ngati abayidwa ndi lupanga. י [Yod] 10  Azimayi amene amakhala achifundo, aphika ana awo ndi manja awo.+ Anawo akhala chakudya chawo pa nthawi yachisoni pamene mwana wamkazi wa anthu anga wawonongedwa.+ כ [Kaph] 11  Yehova wasonyeza ukali wake.Wakhuthula mkwiyo wake woyaka moto.+ Ndipo iye wayatsa moto mʼZiyoni, umene wawotcha maziko ake.+ ל [Lamed] 12  Mafumu apadziko lapansi ndiponso anthu onse okhala panthaka ya dziko lapansi,Sanayembekezere kuti mdani angadzalowe pamageti a Yerusalemu.+ מ [Mem] 13  Zimenezi zinachitika chifukwa cha machimo a aneneri ake ndi zolakwa za ansembe ake,+Amene anakhetsa magazi a anthu olungama mumzindawo.+ נ [Nun] 14  Ansembe ndi aneneriwo akungoyendayenda mʼmisewu ngati anthu akhungu.+ Aipitsidwa ndi magazi,+Moti palibe amene angathe kukhudza zovala zawo. ס [Samekh] 15  Anthu akuwafuulira kuti: “Chokani! Anthu odetsedwa inu! Chokani! Chokani! Musatikhudze!” Iwo alibe pokhala ndipo akungoyendayenda. Anthu a mitundu ina akunena kuti: “Sitilola kuti amenewa azikhala ndi ife kuno.*+ פ [Pe] 16  Yehova wawabalalitsa+Ndipo sadzawakomeranso mtima. Anthu sadzalemekezanso ansembe+ kapena kuchitira chifundo amuna achikulire.”+ ע [Ayin] 17  Ngakhale panopa maso athu afooka chifukwa choyembekezera thandizo lomwe silikubwera.+ Tinafufuza thandizo ku mtundu wa anthu umene sukanatha kutipulumutsa.+ צ [Tsade] 18  Akutisakasaka kulikonse kumene tikupita,+ moti sitingathenso kuyenda mʼmabwalo a mizinda yathu. Mapeto a moyo wathu ayandikira. Masiku athu atha chifukwa mapeto a moyo wathu afika. ק [Qoph] 19  Anthu amene ankatithamangitsa anali aliwiro kuposa ziwombankhanga zouluka mʼmwamba.+ Iwo anatithamangitsa mʼmapiri. Anatibisalira mʼchipululu. ר [Resh] 20  Wodzozedwa wa Yehova,+ amene ndi mpweya wotuluka mumphuno mwathu, wagwidwa mʼdzenje lawo lalikulu.+Ponena za ameneyu, ife tinkanena kuti: “Tidzakhala mumthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.” ש [Sin] 21  Kondwa ndipo usangalale, iwe mwana wamkazi wa Edomu,+ amene ukukhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso kapu ya tsoka idzakupeza.+ Udzaledzera ndipo udzavula nʼkukhala maliseche.+ ת [Taw] 22  Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,* chilango chimene anakupatsa chifukwa cha zolakwa zako chatha. Sadzakutenganso kupita nawe ku ukapolo.+ Koma Mulungu adzatembenukira kwa iwe, mwana wamkazi wa Edomu, kuti aone zolakwa zako. Machimo ako adzawaika poyera.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “azikhala kuno ngati alendo.”
Mawu akuti “mwana wamkazi wa Ziyoni” ndi mawu a ndakatulo ndipo nthawi zambiri amanena za mzinda wa Yerusalemu kapena anthu amene ankakhala mumzindawo.