Maliro 5:1-22

  • Pemphero la anthu lopempha kuti zinthu zibwerere mwakale

    • ‘Kumbukirani zimene zatichitikira’ (1)

    • ‘Tsoka kwa ife chifukwa tachimwa’ (16)

    • ‘Inu Yehova, tibwezereni kwa inu’ (21)

    • “Bwezeretsani zinthu zonse” (21)

5  Inu Yehova, kumbukirani zimene zatichitikira. Tiyangʼaneni kuti muone mmene tikuchitira manyazi.+   Cholowa chathu chaperekedwa kwa anthu achilendo. Nyumba zathu zaperekedwa kwa anthu ochokera kudziko lina.+   Takhala ana amasiye opanda bambo. Amayi athu akhala ngati akazi amasiye.+   Madzi akumwa ndi nkhuni, tikuchita kugula.+   Anthu amene akutithamangitsa atsala pangʼono kutigwira.Tatopa koma tilibe mwayi woti tipume.+   Kuti tipeze chakudya chokwanira, tikudalira Iguputo+ ndi Asuri.+   Makolo athu amene anachimwa anafa, koma ifeyo ndi amene tikuvutika ndi zolakwa zawo.   Antchito ndi amene akutilamulira. Palibe amene akutilanditsa mʼmanja mwawo.   Kuti tipeze chakudya, timaika moyo wathu pachiswe+ chifukwa cha anthu amene ali ndi malupanga mʼchipululu. 10  Khungu lathu latentha kwambiri ngati ngʼanjo chifukwa cha njala yaikulu.+ 11  Achitira zachipongwe* akazi athu amene ali mʼZiyoni ndi anamwali amene ali mʼmizinda ya Yuda.+ 12  Akalonga athu anawapachika powamanga dzanja limodzi.+ Anthuwo sankalemekezanso amuna achikulire.+ 13  Anyamata akunyamula mphero, ndipo tianyamata tikudzandira chifukwa cholemedwa ndi mitolo ya nkhuni. 14  Amuna achikulire sakupezekanso pageti la mzinda+ ndipo anyamata asiya kuimba nyimbo.+ 15  Chisangalalo chamumtima mwathu chatha. Kuvina kwathu kwasanduka kulira maliro.+ 16  Chisoti chathu chachifumu chagwa. Tsoka kwa ife chifukwa tachimwa! 17  Chifukwa cha zimenezi, mtima wathu wadwala.+Ndipo chifukwa cha zinthu zimenezi, maso athu achita mdima,+ 18  Chifukwa cha Phiri la Ziyoni limene lakhala bwinja+ ndipo tsopano nkhandwe zikuyendayenda mmenemo. 19  Koma inu Yehova mudzakhala pampando wanu wachifumu mpaka kalekale. Mpando wanu wachifumu udzakhalapo ku mibadwomibadwo.+ 20  Nʼchifukwa chiyani mwatiiwala kwamuyaya nʼkutisiya kwa nthawi yaitali chonchi?+ 21  Inu Yehova, tibwezereni kwa inu ndipo ife tibwerera kwa inu mwamsanga.+ Bwezeretsani zinthu zonse kuti zikhale ngati mmene zinalili kale.+ 22  Koma inu mwatikanitsitsa. Mukupitiriza kutikwiyira kwambiri.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Agwiririra.”