Salimo 134:1-3
-
Kutamanda Mulungu usiku
-
“Muzikhala oyera mukamapemphera mutakweza manja anu” (2)
-
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
134 Tamandani Yehova,Inu nonse atumiki a Yehova,+Inu amene mumaimirira mʼnyumba ya Yehova usiku.+
2 Muzikhala oyera mukamapemphera mutakweza manja anu*+Ndipo muzitamanda Yehova.
3 Yehova, amene anapanga kumwamba ndi dziko lapansi,Akudalitseni ali ku Ziyoni.
Mawu a M'munsi
^ Mabaibulo ena amati, “Kwezani manja anu mʼmalo opatulika.”