Salimo 138:1-8

  • Mulungu amatisamalira ngakhale kuti ndi wapamwamba

    • ‘Munayankha pemphero langa’ (3)

    • ‘Ngakhale nditakumana ndi mavuto, inu mumandipulumutsa’ (7)

Salimo la Davide. 138  Ndidzakutamandani ndi mtima wanga wonse.+ Ndidzakuimbirani nyimbo zokutamandaniPamaso pa milungu ina.   Ndidzawerama nditayangʼana kukachisi wanu woyera,*+Ndipo ndidzatamanda dzina lanu+Chifukwa cha kukhulupirika kwanu ndiponso chikondi chanu chokhulupirika. Chifukwa mwasonyeza kuti dzina lanu komanso malonjezo anu ndi apamwamba kuposa china chilichonse.*   Pa tsiku limene ine ndinaitana, inu munandiyankha.+Munandilimbitsa mtima komanso kundipatsa mphamvu.+   Mafumu onse apadziko lapansi adzakutamandani, inu Yehova,+Chifukwa adzakhala atamva malonjezo amene mwanena.   Iwo adzaimba zokhudza njira za Yehova,Chifukwa ulemerero wa Yehova ndi waukulu.+   Ngakhale kuti Yehova ali pamwamba, amaona wodzichepetsa,+Koma wonyada samuyandikira.+   Ngakhale nditakumana ndi mavuto, inu mudzandithandiza kuti ndikhalebe ndi moyo.+ Mumagwiritsa ntchito mphamvu zanu polimbana ndi adani anga omwe ndi okwiya.Dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.   Yehova adzakwaniritsa zolinga zimene ali nazo pa ine. Inu Yehova, chikondi chanu chokhulupirika chidzakhalapo mpaka kalekale.+Musasiye ntchito ya manja anu.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “kumalo anu opatulika.”
Mabaibulo ena amati, “Chifukwa inu mwakuza mawu anu pamwamba pa dzina lanu.”