Salimo 143:1-12

  • Kuyembekezera Mulungu ngati dziko louma limene likuyembekezera kuti mvula igwe

    • ‘Ndimaganizira ntchito zanu’ (5)

    • “Ndiphunzitseni kuchita zimene mumafuna” (10)

    • ‘Mzimu wanu umene ndi wabwino unditsogolere’ (10)

Nyimbo ya Davide. 143  Inu Yehova, imvani pemphero langa.+Mvetserani kuchonderera kwanga kopempha thandizo. Ndiyankheni mogwirizana ndi kukhulupirika kwanu komanso chilungamo chanu.   Musandiimbe mlandu ine mtumiki wanu,Chifukwa palibe aliyense wamoyo amene angakhale wolungama pamaso panu.+   Mdani akundifunafuna.Iye wandipondereza ndipo wandigonjetsa. Wandichititsa kuti ndikhale mumdima ngati anthu amene anafa kalekale.   Mphamvu zanga zatha.*+Ndipo mtima wanga wachita dzanzi.+   Ndikukumbukira masiku akale.Ndimaganizira mozama zochita zanu zonse.+Ndimaganizira* ntchito ya manja anu ndi mtima wonse.   Ine ndikupemphera nditakweza manja anga kwa inu.Ndikuyembekezera inu ngati dziko louma limene likuyembekezera kuti mvula igwe.+ (Selah)   Ndiyankheni mofulumira, inu Yehova.+Mphamvu zanga zatha.*+ Musandibisire nkhope yanu,+Chifukwa mukatero ndikhala ngati anthu amene akutsikira kudzenje la manda.+   Mʼmawa ndichititseni kumva za chikondi chanu chokhulupirika,Chifukwa ndimadalira inu. Ndidziwitseni njira imene ndikuyenera kuyendamo,+Chifukwa ndimadalira inu kuti muzinditsogolera.*   Ndipulumutseni kwa adani anga, inu Yehova. Ine ndikudalira inu kuti munditeteze.+ 10  Ndiphunzitseni kuchita zimene inu mumafuna,+Chifukwa inu ndinu Mulungu wanga. Mzimu wanu ndi wabwino.Unditsogolere mʼmalo otetezeka.* 11  Inu Yehova, ndithandizeni kuti ndikhalebe ndi moyo chifukwa cha dzina lanu. Ndipulumutseni mʼmavuto anga, chifukwa ndinu wachilungamo.+ 12  Chifukwa cha chikondi chanu chokhulupirika, wonongani* adani anga.+Muwononge onse amene akundichitira nkhanza,+Chifukwa ine ndine mtumiki wanu.+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Mzimu wanga wafooka.”
Kapena kuti, “Ndimaphunzira.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mzimu wanga watha.”
Kapena kuti, “Chifukwa ndapereka moyo wanga kwa inu.”
Kapena kuti, “Unditsogolere mʼdziko la anthu olungama.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “khalitsani chete.”