Salimo 150:1-6

  • Chamoyo chilichonse chitamande Ya

    • Aleluya! (1, 6)

150  Tamandani Ya!*+ Tamandani Mulungu mʼmalo ake oyera.+ Mutamandeni mumlengalenga mmene mumasonyeza* mphamvu zake.+   Mutamandeni chifukwa cha ntchito zake zamphamvu.+ Mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wosaneneka.+   Mutamandeni poliza lipenga la nyanga ya nkhosa.+ Mutamandeni ndi choimbira cha zingwe komanso zeze.+   Mutamandeni ndi maseche+ komanso gule wovina mozungulira. Mutamandeni ndi zoimbira za zingwe+ ndi chitoliro.+   Mutamandeni ndi zinganga za mawu osangalatsa. Mutamandeni ndi zinganga za mawu amphamvu.+   Chamoyo chilichonse chitamande Ya. Tamandani Ya!*+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Aleluya.” “Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.
Kapena kuti, “mmene mumachitira umboni za.”
Kapena kuti, “Aleluya.” “Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.