Salimo 30:1-12

  • Kulira kunasanduka chisangalalo

    • Mulungu amakomera mtima anthu kwa moyo wawo wonse (5)

Nyimbo yotsegulira nyumba. Salimo la Davide. 30  Ndidzakutamandani inu Yehova, chifukwa mwandipulumutsa.*Simunalole kuti adani anga asangalale chifukwa cha mavuto anga.+   Inu Yehova Mulungu wanga, ndinafuulira kwa inu kuti mundithandize ndipo munandichiritsa.+   Inu Yehova, mwanditulutsa mʼManda,*+ Mwandisunga ndi moyo, mwanditeteza kuti ndisatsikire mʼdzenje.*+   Imbani nyimbo zotamanda Yehova, inu okhulupirika ake,+Yamikani dzina* lake loyera.+   Chifukwa mkwiyo wa Mulungu sukhalitsa pa munthu,+Koma munthu amene wasangalala naye* amamukomera mtima kwa moyo wake wonse.+ Munthu akhoza kulira usiku, koma mʼmawa amafuula mosangalala.+   Pa nthawi imene ndinalibe mavuto ndinanena kuti: “Sindidzagwedezeka.”*   Inu Yehova, pa nthawi imene munkasangalala nane,* munachititsa kuti ndikhale wamphamvu ngati phiri.+ Koma mutabisa nkhope yanu, ndinachita mantha.+   Ndinapitiriza kuitana inu Yehova,+Ndipo ndinapitiriza kuchonderera Yehova kuti andikomere mtima.   Kodi imfa yanga ili* ndi phindu lanji? Kodi pali phindu lanji ngati nditatsikira kudzenje la manda?+ Kodi fumbi lingakutamandeni?+ Kodi lingalengeze kuti inu ndinu wokhulupirika?+ 10  Imvani inu Yehova, ndipo mundikomere mtima.+ Inu Yehova, ndithandizeni.+ 11  Mwasintha kulira kwanga kuti kukhale kuvina.Mwandivula chiguduli changa ndipo mwandiveka chisangalalo, 12  Kuti ndiimbe nyimbo zokutamandani ndipo ndisakhale chete. Inu Yehova Mulungu wanga, ndidzakutamandani mpaka kalekale.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mwanditulutsa mʼdzenje.”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti, “mʼmanda.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “chikumbutso.”
Kapena kuti, “amene akumufunira zabwino.”
Kapena kuti, “Sindidzadzandira.”
Kapena kuti, “munkandifunira zabwino.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “magazi anga ali.”