Salimo 68:1-35

  • ‘Adani a Mulungu amwazikeʼ

    • “Bambo wa ana amasiye” (5)

    • Mulungu amapereka nyumba kwa anthu amene alibe wowathandiza (6)

    • Akazi amene akulengeza uthenga wabwino (11)

    • Mphatso za amuna (18)

    • ‘Yehova amanyamula katundu wathu tsiku ndi tsiku’ (19)

Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo ndi nyimbo ya Davide. 68  Mulungu anyamuke, adani ake amwazike,Ndipo amene amadana naye athawe pamaso pake.+   Mofanana ndi mphepo imene imathamangitsa utsi, inunso muwathamangitsire kutali.Mofanana ndi phula limene limasungunuka pamoto,Anthu oipa awonongeke pamaso pa Mulungu.+   Koma olungama asangalale,+Asangalale kwambiri pamaso pa Mulungu,Adumphe ndi chisangalalo.   Imbirani Mulungu, muimbireni nyimbo zotamanda dzina lake.+ Imbirani Iye amene akudutsa mʼchipululu.* Dzina lake ndi Ya.*+ Sangalalani pamaso pake.   Bambo wa ana amasiye komanso amene amateteza* akazi amasiye+Ndi Mulungu amene amakhala mʼmalo ake oyera.+   Anthu amene alibe wowathandiza, Mulungu amawapatsa nyumba kuti azikhalamo.+Amamasula akaidi nʼkuwathandiza kuti zinthu ziwayendere bwino.+ Koma anthu osamvera* adzakhala mʼdziko louma.+   Inu Mulungu, pamene munkatsogolera anthu anu,+Pamene munkadutsa mʼchipululu, (Selah)   Dziko lapansi linagwedezeka,+Kumwamba kunagwa mvula chifukwa cha inu Mulungu,Phiri la Sinai ili linagwedezeka chifukwa cha inu Mulungu, Mulungu wa Isiraeli.+   Inu Mulungu, munagwetsa mvula yokwanira.Munapatsa mphamvu anthu anu amene anali ofooka.* 10  Iwo ankakhala mʼmudzi wanu wamatenti.+Inu Mulungu, chifukwa chakuti ndinu wabwino, munapereka zinthu zofunika kwa anthu osauka. 11  Yehova wapereka lamulo* kwa anthu ake,Ndipo akazi amene akulengeza uthenga wabwino* ndi gulu lalikulu.+ 12  Mafumu okhala ndi magulu a asilikali amathawa,+ ndithu amathawadi. Mkazi amene amangokhala pakhomo, amalandira nawo zinthu zimene zalandidwa kunkhondo.+ 13  Ngakhale anthu inu mutagona pambali pa moto mumsasa,Mudzalandira njiwa imene mapiko ake ndi okutidwa ndi siliva,Ndipo nthenga zakumapeto a mapiko ake ndi zagolide woyenga bwino.* 14  Pamene Wamphamvuyonse anamwaza mafumu amʼdzikomo,+Mu Zalimoni munagwa sinowo.* 15  Phiri la ku Basana+ ndi phiri la Mulungu.*Phiri la ku Basana ndi phiri lansonga zitalizitali. 16  Nʼchifukwa chiyani inu mapiri ansonga zitalizitali mumayangʼana mwansanjePhiri limene Mulungu wasankha* kuti azikhalamo?+ Ndithudi, Yehova adzakhala mʼphiri limenelo mpaka kalekale.+ 17  Magaleta ankhondo a Mulungu ali mʼmagulu a masauzande osawerengeka, ali mʼmagulu masauzandemasauzande.+ Yehova walowa mʼmalo oyera kuchokera kuphiri la Sinai.+ 18  Munakwera pamalo apamwamba.+Munatenga anthu ogwidwa ukapolo.Munatenga amuna kuti akhale mphatso,+Ndithu inu Ya,* Mulungu wathu, mwatenga ngakhale anthu osamvera+ kuti mukhale pakati pawo. 19  Atamandike Yehova, amene amanyamula katundu wathu tsiku ndi tsiku,+Mulungu woona amene amatipulumutsa. (Selah) 20  Mulungu woona ndi Mulungu amene amatipulumutsa.+Ndipo Yehova Ambuye Wamkulu Koposa amatipulumutsa ku imfa.+ 21  Ndithudi, Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake,Adzaphwanya mutu wa aliyense amene akupitiriza* kuchita machimo.+ 22  Yehova wanena kuti: “Ndidzawabweza kuchokera ku Basana,+Ndidzawatulutsa mʼnyanja yakuya, 23  Kuti mapazi anu aponde magazi a adani anu,+Ndiponso kuti malilime a agalu anu anyambite magazi a adani anu.” 24  Iwo aona magulu a anthu anu akuyendera pamodzi, inu Mulungu,Magulu a anthu oyendera pamodzi a Mulungu wanga, Mfumu yanga, akulowa kumalo opatulika.+ 25  Oimba nyimbo akuyenda patsogolo, oimba zoimbira za zingwe akuyenda pambuyo pawo,+Pakati pali atsikana amene akuimba maseche.+ 26  Pamisonkhano tamandani Mulungu,Tamandani Yehova, inu nonse amene moyo wanu ukuchokera mu Kasupe wa Isiraeli.+ 27  Pali fuko lalingʼono la Benjamini+ limene likugonjetsa anthu,Pali akalonga a Yuda pamodzi ndi chigulu chawo chimene chikuchita phokoso,Palinso akalonga a Zebuloni komanso akalonga a Nafitali. 28  Mulungu wanu waganiza kuti akupatseni mphamvu. Sonyezani mphamvu zanu, Inu Mulungu, amene mumatithandiza.+ 29  Chifukwa cha kachisi wanu yemwe ali ku Yerusalemu,+Mafumu adzabweretsa mphatso kwa inu.+ 30  Dzudzulani nyama zakutchire zimene zimakhala mʼmabango,Gulu la ngʼombe zamphongo+ limodzi ndi ana awo,Mpaka mitundu ya anthu itagwada nʼkubweretsa ndalama zasiliva. Koma iye wabalalitsa mitundu ya anthu imene imasangalala ndi nkhondo. 31  Zinthu zopangidwa ndi kopa* zidzabwera kuchokera* ku Iguputo,+Mwamsanga, dziko la Kusi lidzapereka mphatso kwa Mulungu. 32  Inu maufumu a dziko lapansi, imbirani Mulungu,+Imbani nyimbo zotamanda Yehova, (Selah) 33  Imbirani iye amene wakwera pamwamba pa kumwamba,+ kumene kwakhalapo kuyambira kalekale. Mawu ake amphamvu amamveka ngati bingu. 34  Vomerezani kuti Mulungu ndi wamphamvu zochuluka.+ Ulemerero wake uli pa Isiraeli,Ndipo amasonyeza mphamvu zake kuchokera kumwamba.* 35  Mulungu walamula kuti anthu amuope komanso amupatse ulemu mʼmalo ake opatulika aulemerero.+ Iye ndi Mulungu wa Isiraeli,Amene amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu.+ Mulungu atamandike.

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “akudutsa mʼmitambo.”
“Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.
Mʼchilankhulo choyambirira, “amaweruzira milandu.”
Kapena kuti, “opanduka.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “cholowa chanu chimene chinali chofooka.”
Limeneli ndi lamulo loti apite kunkhondo.
Umenewu ndi uthenga wonena za kupambana pankhondo.
Kapena kuti, “ndi zagilini wopitira kuyelo.”
Mabaibulo ena amati, “Zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.” Kapena kuti, “chipale chofewa.”
Kapena kuti, “phiri laulemerero.”
Kapena kuti, “wafuna.”
“Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.
Kapena kuti, “amene akuyenda mʼnjira yochimwa.”
Kapena kuti, “mkuwa.”
Mabaibulo ena amati, “Nthumwi zidzachokera ku.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmitambo.”