Salimo 7:1-17
-
Yehova ndi Woweruza wolungama
-
“Ndiweruzeni inu Yehova” (8)
-
Nyimbo yoimba polira imene Davide anaimbira Yehova, yokhudza mawu a Kusi wa fuko la Benjamini.
7 Inu Yehova Mulungu wanga, ine ndathawira kwa inu.+
Ndipulumutseni kwa anthu onse amene akundizunza ndipo mundilanditse.+
2 Mukapanda kutero andikhadzulakhadzula ngati mmene mkango umachitira,+Nʼkunditenga popanda wondipulumutsa.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndalakwitsa chilichonse,Ngati ndachita zinthu mopanda chilungamo,
4 Ngati ndachita zoipa kwa munthu amene akundichitira zabwino,+Kapena ngati mdani wanga ndamulanda zinthu zake popanda chifukwa,*
5 Mdani wanga andithamangitse nʼkundipeza,Andigwetsere pansi nʼkundipondaponda mpaka kufaNdipo andisiye nditagona pafumbi mwamanyazi. (Selah)
6 Nyamukani mutakwiya, inu Yehova.Imirirani ndi kukhaulitsa adani anga amene andikwiyira.+Dzukani nʼkundithandiza, ndipo mulamule kuti chilungamo chichitike.+
7 Mitundu ya anthu ikuzungulireni,Ndipo inu muwaweruze muli kumwambako.
8 Yehova adzapereka chigamulo kwa mitundu ya anthu.+
Ndiweruzeni inu Yehova, mogwirizana ndi chilungamo changaKomanso mogwirizana ndi kukhulupirika kwanga.+
9 Chonde, thetsani zinthu zoipa zimene anthu oipa akuchita.
Koma muchititse kuti wolungama akhale wolimba,+Chifukwa inu ndinu Mulungu wolungama+ amene amayeza mitima+ komanso mmene munthu akumvera mumtima.*+
10 Mulungu ndi chishango changa,+ Mpulumutsi wa anthu owongoka mtima.+
11 Mulungu ndi Woweruza wolungama,+Ndipo Mulungu amapereka zigamulo kwa* oipa tsiku lililonse.
12 Ngati munthu sakulapa,+ Mulungu amanola lupanga lake,+Amakunga uta wake nʼkukonzekera kulasa.+
13 Iye amakhala wokonzeka kugwiritsa ntchito zida zake zoopsa,Amakhala wokonzeka kugwiritsa ntchito mivi yake yoyaka moto.+
14 Taonani munthu amene ali ndi pakati pa zinthu zoipa,Watenga pakati pa mavuto ndipo adzabereka mabodza.+
15 Iye wakumba dzenje ndipo walizamitsa,Koma adzagwera mʼdzenje limene wakumba yekhalo.+
16 Mavuto amene akuwayambitsawo adzabwerera pamutu pake,+Zinthu zachiwawa zimene akuchita zidzagwera paliwombo pake.
17 Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha chilungamo chake.+Ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina la Yehova+ Wamʼmwambamwamba.+