Salimo 76:1-12
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe ndi zipangizo za zingwe. Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+
76 Mulungu ndi wodziwika mu Yuda.+Dzina lake ndi lalikulu mu Isiraeli.+
2 Tenti yake ili ku Salemu,+Malo ake okhala ali ku Ziyoni.+
3 Kumeneko anathyola mivi yoyaka moto,Anathyolanso chishango, lupanga ndi zida zankhondo.+ (Selah)
4 Inu mumawala kwambiri.*Ndinu waulemerero kuposa mapiri amene muli nyama zodya zinzake.
5 Anthu olimba mtima alandidwa zinthu zawo.+
Iwo agona tulo,Asilikali onse analibe mphamvu.+
6 Chifukwa cha kudzudzula kwanu, inu Mulungu wa Yakobo,Hatchi komanso wokwera galeta, onse agona tulo tofa nato.+
7 Inu nokha ndinu wochititsa mantha.+
Ndi ndani angapirire mkwiyo wanu waukulu?+
8 Munapereka chiweruzo muli kumwamba.+Dziko lapansi linachita mantha ndipo linakhala chete+
9 Pamene Mulungu ananyamuka kuti apereke chiweruzo,Kuti apulumutse anthu onse ofatsa apadziko lapansi.+ (Selah)
10 Chifukwa mkwiyo wa munthu udzachititsa kuti mutamandidwe.+Mudzadzikongoletsa ndi mkwiyo wawo wotsala.
11 Chitani malonjezo anu kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse+Anthu onse amene amuzungulira abweretse mphatso zawo mwamantha.+
12 Mulungu adzachititsa manyazi atsogoleri onyada.Iye amachititsa kuti mafumu apadziko lapansi akhale ndi mantha.
Mawu a M'munsi
^ Kapena kuti, “Mwazunguliridwa ndi kuwala.”