Salimo 82:1-8

  • Anapempha chiweruzo cholungama

    • Mulungu akuweruza “pakati pa milungu” (1)

    • “Tetezani anthu onyozeka” (3)

    • “Inu ndinu milungu” (6)

Nyimbo ya Asafu.+ 82  Mulungu waima pamsonkhano wake,*+Akuweruza pakati pa milungu* kuti:+   “Kodi mupitiriza kuweruza mopanda chilungamo+Komanso kukondera anthu oipa mpaka liti?+ (Selah)   Tetezani* anthu onyozeka ndi ana amasiye.+ Chitirani chilungamo anthu amene alibe wowathandiza komanso osauka.+   Pulumutsani munthu wonyozeka ndi wosauka.Alanditseni mʼmanja mwa anthu oipa.”   Milunguyo sikudziwa kapena kuzindikira.+Ikuyendayenda mumdima,Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.+   “Ine ndanena kuti, ‘Inu ndinu milungu,*+Nonsenu ndinu ana a Wamʼmwambamwamba.   Koma mudzafa ngati mmene anthu onse amafera.+Ndipo mudzagwa ngati mmene kalonga aliyense amagwera!’”+   Nyamukani inu Mulungu, ndipo muweruze dziko lapansi,+Chifukwa mitundu yonse ya anthu ndi yanu.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “pamsonkhano wa Mulungu.”
Kapena kuti, “pakati pa ofanana ndi mulungu.”
Kapena kuti, “Weruzani.”
Kapena kuti, “ofanana ndi mulungu.”