Salimo 85:1-13

  • Pemphero lopempha kubwezeretsedwa

    • Mulungu adzanena za mtendere kwa anthu ake okhulupirika (8)

    • Chikondi chokhulupirika komanso kukhulupirika zidzakumana (10)

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.+ 85  Inu Yehova, dziko lanu mwalisonyeza kukoma mtima.+Mwabwezeretsa ana a Yakobo amene anagwidwa ukapolo.+   Munakhululukira anthu anu zolakwa zawo.Munawakhululukira* machimo awo onse.+ (Selah)   Munabweza mkwiyo wanu wonse,Ndipo simunasonyeze mkwiyo wanu waukulu.+   Tibwezeretseni mwakale,* inu Mulungu amene mumatipulumutsa,Ndipo tichotsereni mkwiyo wanu.+   Kodi mutikwiyira mpaka kalekale?+ Kodi mudzapitiriza kusonyeza mkwiyo wanu ku mibadwomibadwo?   Kodi simutipatsanso mphamvuKuti anthu anu asangalale chifukwa cha inu?+   Tisonyezeni chikondi chanu chokhulupirika inu Yehova,+Ndipo mutipulumutse.   Ndidzamvetsera zimene Mulungu woona Yehova adzanene,Chifukwa adzanena za mtendere kwa anthu ake,+ kwa okhulupirika ake.Koma iwo asayambenso kudzidalira kwambiri ngati kale.+   Ndithudi, iye ndi wokonzeka kupulumutsa amene amamuopa,+Kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu. 10  Chikondi chokhulupirika komanso kukhulupirika zidzakumana.Chilungamo ndi mtendere zidzakisana.+ 11  Kukhulupirika kudzaphuka padziko lapansi,Ndipo chilungamo chidzayangʼana pansi kuchokera kumwamba.+ 12  Ndithudi, Yehova adzapereka zinthu zabwino,*+Ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.+ 13  Chilungamo chidzayenda pamaso pake,+Ndipo chidzapanga njira kuti mapazi a Mulungu azidutsamo.

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Munaphimba.”
Kapena kuti, “Tisonkhanitseni ndi kutibwezeretsa mwakale.”
Kapena kuti, “adzachititsa kuti zinthu ziziyenda bwino.”