Salimo 88:1-18
Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.+ Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe potsatira kaimbidwe ka Mahalati* ndipo iimbidwe molandizana. Masikili* ya Hemani+ wa mʼbanja la Zera.
88 Inu Yehova, Mulungu amene amandipulumutsa,+Masana ndimafuulira inu,Ndipo usiku ndimabwera pamaso panu.+
2 Pemphero langa lifike kwa inu.+Tcherani khutu lanu kuti mumve* kuchonderera kwanga kopempha thandizo.+
3 Chifukwa moyo wanga wadzaza ndi masoka,+Ndipo moyo wanga wayandikira ku Manda.*+
4 Anandiika kale mʼgulu la anthu amene akutsikira kudzenje.*+Ndakhala munthu wovutika,*+
5 Amene wasiyidwa pakati pa anthu akufaNgati anthu ophedwa amene agona mʼmanda,Amene simukuwakumbukiransoKomanso amene sakuthandizidwa ndi inu.*
6 Mwandiika mʼdzenje lakuya kwambiri,Mʼmalo amdima, mʼphompho lalikulu.
7 Mkwiyo wanu ukundilemera kwambiri,+Ndipo ndikumva ngati mukundipanikiza ndi mafunde anu amphamvu. (Selah)
8 Anzanga mwawathamangitsira kutali ndi ine.+Mwandipangitsa kuti ndikhale chinthu chonyansa kwa iwo.
Ndakodwa ndipo sindingathe kuthawa.
9 Diso langa lachita mdima chifukwa cha kuvutika kwanga.+
Ndimaitana inu Yehova tsiku lonse.+Ndimapemphera kwa inu nditakweza manja anga.
10 Kodi mungachitire zinthu zodabwitsa anthu akufa?
Kodi anthu akufa amene sangathe kuchita kanthu angadzuke nʼkukutamandani?+ (Selah)
11 Kodi chikondi chanu chokhulupirika chingalengezedwe kumanda?Kodi kukhulupirika kwanu kungalengezedwe mʼmalo a chiwonongeko?*
12 Kodi ntchito zanu zodabwitsa zingadziwike mu mdima?Kapena kodi chilungamo chanu chidzadziwika mʼdziko la anthu oiwalika?+
13 Koma ine ndimafuulirabe kwa inu Yehova kuti mundithandize,+Mʼmawa uliwonse pemphero langa limafika kwa inu.+
14 Inu Yehova, nʼchifukwa chiyani mukundikana?+
Nʼchifukwa chiyani mukundibisira nkhope yanu?+
15 Kuyambira ndili mnyamata,Ndakhala ndikuzunzika komanso kutsala pangʼono kufa.+Ndafooka kwambiri chifukwa cha zinthu zoopsa zimene mwalola kuti ndikumane nazo.
16 Ndafooka chifukwa cha mkwiyo wanu woyaka moto.+Zinthu zochititsa mantha zochokera kwa inu zandiwononga.
17 Zinthu zimene mumachita zandizungulira ngati madzi tsiku lonse.Zanditsekera kuzungulira mbali zonse.
18 Anzanga komanso anthu oyandikana nawo mwawathamangitsira kutali ndi ine.+Malo amdima akhala mnzanga wapamtima.
Mawu a M'munsi
^ Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
^ Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
^ Kapena kuti, “Weramani ndipo mumvetsere.”
^ Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
^ Kapena kuti, “kumanda.”
^ Kapena kuti, “ngati munthu wopanda mphamvu.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “ndi dzanja lanu.”
^ Kapena kuti, “ku Abadoni.”