Wolembedwa ndi Mateyu 3:1-17

  • Yohane Mʼbatizi ankalalikira (1-12)

  • Ubatizo wa Yesu (13-17)

3  Mʼmasiku amenewo, Yohane+ Mʼbatizi anapita mʼchipululu cha Yudeya nʼkuyamba kulalikira.+  Iye ankalalikira kuti: “Lapani, chifukwa Ufumu wakumwamba wayandikira.”+  Mneneri Yesaya ananeneratu za iyeyu+ mʼmawu awa: “Winawake akufuula mʼchipululu kuti: ‘Konzani njira ya Yehova!* Muwongole misewu yake.’”+  Yohane ankavala chovala chaubweya wa ngamila ndi lamba wachikopa mʼchiuno mwake.+ Chakudya chake chinali dzombe ndi uchi.+  Choncho anthu ochokera ku Yerusalemu ndi mʼchigawo chonse cha Yudeya ndiponso ochokera mʼmidzi yonse yapafupi ndi Yorodano ankapita kwa iye.+  Iye ankawabatiza* mumtsinje wa Yorodano+ ndipo anthuwo ankaulula machimo awo poyera.  Yohane ataona Afarisi ndi Asaduki+ ambiri akubwera ku ubatizowo, anawauza kuti: “Ana a njoka inu,+ ndi ndani wakuchenjezani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwerawo?+  Ndiyetu mubale zipatso zosonyeza kulapa.  Musamadzinamize kuti, ‘Tili ndi atate wathu Abulahamu.’+ Chifukwa ndikukuuzani kuti Mulungu akhoza kupangira Abulahamu ana kuchokera kumiyala iyi. 10  Nkhwangwa yaikidwa kale pamizu yamitengo. Choncho mtengo uliwonse wosabereka zipatso zabwino udulidwa nʼkuponyedwa pamoto.+ 11  Ine ndikukubatizani mʼmadzi chifukwa chakuti mwalapa,+ koma amene akubwera mʼmbuyo mwanga ndi wamphamvu kuposa ine, ndipo sindili woyenera kumuvula nsapato zake.*+ Ameneyo adzakubatizani ndi mzimu woyera+ komanso moto.+ 12  Fosholo yake youluzira mankhusu* ili mʼmanja mwake, ndipo malo ake opunthirapo mbewu adzawayeretseratu kuti mbee! Tirigu adzamututira munkhokwe, koma mankhusu adzawawotcha ndi moto+ umene sungazimitsidwe.” 13  Kenako Yesu anabwera kwa Yohane ku Yorodano kuchokera ku Galileya, kuti iye amubatize.+ 14  Koma Yohane anayesa kumuletsa ponena kuti: “Ineyo ndi amene ndikuyenera kubatizidwa ndi inu, ndiye nʼchifukwa chiyani mukubwera kwa ine?” 15  Yesu anamuyankha kuti: “Pa nthawi ino yokha lola kuti zikhale choncho, chifukwa tikufunikira kuchita zimenezi kuti tikwaniritse chilungamo chonse.” Atatero, anasiya kumuletsa. 16  Atabatizidwa, nthawi yomweyo Yesu anavuuka mʼmadzimo. Pamenepo kumwamba kunatseguka,+ ndipo Yohane anaona mzimu wa Mulungu ukutsika ngati nkhunda nʼkudzamutera.+ 17  Panamvekanso mawu ochokera kumwamba+ onena kuti: “Uyu ndi Mwana wanga+ wokondedwa ndipo amandisangalatsa kwambiri.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “ankawaviika; ankawamiza.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “masandasi ake.”
“Mankhusu” ndi makoko amene amachotsa ku mbewu ngati mpunga popuntha ndipo amatha kuwauluza ndi mphepo.