Miyambo 10:1-32

  • Mwana wanzeru amasangalatsa bambo ake (1)

  • Wogwira ntchito mwakhama adzalemera (4)

  • Mawu akachuluka sipalephera kukhala zolakwika (19)

  • Madalitso a Yehova ndi amene amalemeretsa (22)

  • Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo (27)

10  Miyambi ya Solomo.+ Mwana wanzeru amasangalatsa bambo ake,+Koma mwana wopusa amamvetsa chisoni mayi ake.   Chuma chimene munthu wapeza chifukwa chochita zoipa chidzakhala chopanda phindu,Koma chilungamo nʼchimene chimapulumutsa munthu ku imfa.+   Yehova sadzachititsa kuti munthu wolungama akhale ndi njala,+Koma anthu oipa sadzawapatsa zimene amalakalaka.   Munthu waulesi adzakhala wosauka,+Koma wogwira ntchito mwakhama adzalemera.+   Mwana wochita zinthu mozindikira amatuta zokolola mʼchilimwe,Koma mwana wochititsa manyazi amakhala ali mʼtulo tofa nato pa nthawi yokolola.+   Madalitso amapita pamutu pa munthu wolungama,+Koma pakamwa pa anthu oipa pamabisa zachiwawa.   Zabwino zimene munthu wolungama ankachita zikakumbukiridwa* amadalitsidwa,+Koma dzina la anthu oipa lidzawola.+   Munthu wanzeru mumtima mwake amamvera malangizo,*+Koma wolankhula mopusa adzapeza mavuto.+   Munthu wochita zinthu mokhulupirika adzakhala wotetezeka,+Koma munthu wochita zinthu mwachinyengo adzadziwika.+ 10  Munthu amene amatsinzinira ena diso amachititsa ena kumva chisoni,+Ndipo amene amalankhula mopusa adzapeza mavuto.+ 11  Pakamwa pa wolungama pamachokera moyo,+Koma pakamwa pa anthu oipa pamabisa zachiwawa.+ 12  Chidani nʼchimene chimayambitsa mikangano,Koma chikondi chimaphimba machimo onse.+ 13  Nzeru imapezeka pamilomo ya munthu wozindikira,+Koma ndodo amakwapulira msana wa munthu wopanda nzeru.+ 14  Anzeru ndi amene amapitiriza kuphunzira zinthu zamtengo wapatali,+Koma pakamwa pa wopusa pamachititsa kuti awonongedwe.+ 15  Munthu wolemera amaona kuti chuma chake chili* ngati mzinda wokhala ndi mpanda wolimba. Koma anthu osauka amavutika chifukwa cha umphawi wawo.+ 16  Zochita za wolungama zimabweretsa moyo.Koma zochita za woipa zimabweretsa tchimo.+ 17  Amene amamvera malangizo* amathandiza ena kukapeza moyo,*Koma amene amanyalanyaza chidzudzulo amasocheretsa ena. 18  Munthu amene amabisa chidani mumtima mwake amalankhula mabodza,+Ndipo amene amafalitsa mphekesera zoipa ndi wopusa. 19  Mawu akachuluka sipalephera kukhala zolakwika,+Koma amene amalamulira milomo yake amachita zinthu mwanzeru.+ 20  Lilime la wolungama lili ngati siliva wabwino kwambiri,+Koma mtima wa woipa ndi wopanda phindu. 21  Milomo ya wolungama imathandiza* anthu ambiri,+Koma zitsiru zimafa chifukwa chopanda nzeru.+ 22  Madalitso a Yehova ndi amene amalemeretsa munthu,+Ndipo popereka madalitsowa Mulungu sawonjezerapo ululu.* 23  Kwa munthu wopusa, kuchita khalidwe lochititsa manyazi kuli ngati masewera,Koma munthu wozindikira amakhala ndi nzeru.+ 24  Chinthu chimene munthu woipa amaopa nʼchimene chidzamuchitikire,Koma anthu olungama adzapatsidwa zimene amalakalaka.+ 25  Mphepo yamkuntho ikawomba woipa amawonongedwa,+Koma wolungama ali ngati maziko mpaka kalekale.+ 26  Viniga* amachititsa kuti mano ayezimire ndipo utsi umapweteka mʼmaso,Izi nʼzimene munthu waulesi amachita kwa munthu amene wamutuma.* 27  Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo,+Koma zaka za anthu oipa zidzafupikitsidwa.+ 28  Zimene anthu olungama akuyembekezera zimasangalatsa,*+Koma chiyembekezo cha anthu oipa sichidzakwaniritsidwa.+ 29  Njira ya Yehova ndi malo achitetezo kwa munthu wopanda cholakwa,+Koma anthu ochita zoipa amawonongedwa mʼnjira imeneyi.+ 30  Wolungama sadzagwetsedwa,+Koma anthu oipa sadzakhalanso padziko lapansi.+ 31  Pakamwa pa munthu wolungama pamalankhula* zanzeru,Koma lilime lolankhula zinthu zopotoka lidzadulidwa. 32  Milomo ya munthu wolungama imadziwa zinthu zosangalatsa,Koma pakamwa pa anthu oipa mʼpachinyengo.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Mbiri yake ikakumbukiridwa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “malamulo.”
Kapena kuti, “amaona kuti zinthu zake zamtengo wapatali zili.”
Mabaibulo ena amati, “akuyenda panjira ya kumoyo.”
Mawu amʼchilankhulo choyambirira amene amasuliridwa kuti “malangizo” ali ndi matanthauzo ambiri. Akhoza kutanthauza malangizo, kuphunzitsa, kudzudzula, kulimbikitsa, kulanga kapena uphungu.
Kapena kuti, “imatsogolera.”
Kapena kuti, “chisoni; mavuto.”
“Viniga” ndi chakumwa chowawasira chomwe chinkapangidwa kuchokera ku vinyo wosasa kapena zakumwa zina zoledzeretsa.
Kapena kuti, “kwa amene anamulemba ntchito.”
Kapena kuti, “Chiyembekezo cha anthu olungama chimasangalatsa.”
Kapena kuti, “pamabereka zipatso.”