Miyambo 25:1-28

  • Kusunga chinsinsi (9)

  • Mawu osankhidwa bwino (11)

  • Osamapitapita kunyumba kwa mnzako (17)

  • Kuunjika makala amoto pamutu pa mdani (21, 22)

  • Nkhani yabwino ili ngati madzi ozizira (25)

25  Miyambi ina ya Solomo+ imene atumiki a Hezekiya+ mfumu ya Yuda anakopera ndi iyi:   Kusunga chinsinsi ndi ulemerero wa Mulungu,+Ndipo ulemerero wa mafumu ndi kufufuza bwino nkhani.   Nʼzosatheka kufufuza kutalika kwa kumwamba komanso kuzama kwa dziko lapansi,Nʼchimodzimodzinso mitima ya mafumu.   Yengani siliva nʼkuchotsa zonse zosafunika,Ndipo yense adzatuluka woyengeka bwino.+   Chotsani woipa pamaso pa mfumu,Ndipo mpando wake wachifumu udzakhazikika chifukwa cha chilungamo.+   Usadzilemekeze wekha pamaso pa mfumu,+Ndipo usakhale pakati pa anthu olemekezeka,+   Chifukwa ndi bwino kuti mfumuyo ikuuze kuti, “Bwera udzakhale apa,” Kusiyana nʼkuti ikuchititse manyazi pamaso pa munthu wolemekezeka.+   Usamafulumire kupititsa mlandu kukhoti,Chifukwa udzachita chiyani mnzako akadzapereka umboni wosonyeza kuti iweyo ndi wolakwa?+   Thetsa nkhaniyo pokambirana ndi mnzakoyo,+Koma usaulule nkhani zachinsinsi zimene unauzidwa,*+ 10  Kuti amene akumvetsera asakuchititse manyaziKomanso kuti usafalitse nkhani yoipa* imene sungathe kuithetsa kuti isapitirize kufalikira. 11  Mawu olankhulidwa pa nthawi yoyenera+Ali ngati zipatso za maapozi agolide mʼmbale zasiliva. 12  Munthu wanzeru akamadzudzula munthu wa khutu lomvetsera+Amakhala ngati ndolo yagolide ndiponso ngati chokongoletsera chagolide woyenga bwino. 13  Nthumwi yokhulupirika kwa anthu amene aitumaIli ngati kuzizira kwa sinowo* pa tsiku lokolola,Chifukwa imatsitsimula moyo wa abwana ake.+ 14  Munthu wodzitama kuti apereka mphatso koma nʼkulephera kupereka,+Ali ngati mitambo komanso mphepo yosabweretsa mvula. 15  Chifukwa cha kuleza mtima munthu angathe kunyengerera munthu waudindo,Ndipo mawu okoma akhoza* kuthyola fupa.+ 16  Ukapeza uchi udye umene ungakukwane,Chifukwa ukadya wambiri ungathe kuusanza.+ 17  Phazi lako lisamapitepite kunyumba kwa mnzako,Kuti angatope nawe nʼkuyamba kudana nawe. 18  Munthu wopereka umboni wabodza pa mlandu wa mnzake+Ali ngati chibonga chakunkhondo, lupanga, komanso muvi wakuthwa. 19  Kukhulupirira munthu wosadalirika* pa nthawi yamavutoKuli ngati dzino lothyoka komanso phazi lotsimphina. 20  Amene amaimbira nyimbo munthu amene ali ndi chisoni mumtima mwake+Ali ngati munthu amene amavula chovala pa tsiku lozizira,Komanso ngati viniga* amene wathiridwa musoda 21  Ngati mdani wako* ali ndi njala, umʼpatse chakudya.Ngati ali ndi ludzu, umʼpatse madzi akumwa,+ 22  Ukachita zimenezi ndiye kuti ukumuunjikira makala amoto pamutu pake,*+Ndipo Yehova adzakupatsa mphoto. 23  Mphepo yakumpoto imabweretsa mvula yambiriNdipo lilime lonena miseche limachititsa kuti anthu akhale ndi nkhope zolusa.+ 24  Ndi bwino kukhala pakona ya denga la nyumbaKusiyana ndi kukhala mʼnyumba limodzi ndi mkazi wolongolola.*+ 25  Nkhani yabwino yochokera kudziko lakutali+Ili ngati madzi ozizira kwa munthu wotopa. 26  Munthu wolungama amene amagonja* nʼkuchita zofuna za munthu woipaAmakhala ngati kasupe wamatope komanso chitsime chimene chawonongedwa. 27  Si bwino kudya uchi wambiri,+Komanso si bwino kuti munthu adzifunire yekha ulemerero.+ 28  Munthu wosaugwira mtima+Ali ngati mzinda umene mpanda wake wagumulidwa.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “usaulule zinsinsi za ena.”
Kapena kuti, “mphekesera zoipa.”
Kapena kuti, “chipale chofewa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “lilime lofewa likhoza.”
Mabaibulo ena amati, “munthu amene amachita zachinyengo.”
“Viniga” ndi chakumwa chowawasira chomwe chinkapangidwa kuchokera ku vinyo wosasa kapena zakumwa zina zoledzeretsa.
Mʼchilankhulo choyambirira, “munthu amene amadana nawe.”
Kutanthauza kufewetsa mtima wake komanso kumuchititsa kuti azichita zinthu zabwino.
Kapena kuti, “wokonda kudandaula.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “amanjenjemera pamaso pa munthu woipa.”