Miyambo 31:1-31

  • MAWU A MFUMU LEMUELI (1-31)

    • Ndani amene angapeze mkazi wamakhalidwe abwino? (10)

    • Amagwira ntchito mwakhama (17)

    • Kukoma mtima kuli palilime lake (26)

    • Ana ndi mwamuna wake amamutamanda (28)

    • Kuoneka bwino komanso kukongola sikuchedwa kutha (30)

31  Mawu a Mfumu Lemueli, uwu ndi uthenga wamphamvu umene mayi ake anamupatsa pomulangiza:+   Kodi ndikuuze chiyani mwana wanga?Kodi ndikuuze mawu otani iwe mwana wochokera mʼmimba mwanga?Kodi ndikuuze mawu otani iwe mwana wa malonjezo anga?+   Usamapereke mphamvu zako kwa akazi,+Kapena kutsatira njira zimene zimachititsa kuti mafumu awonongedwe.+   Nʼkosayenera kuti mafumu azimwa vinyo,Nʼkosayenera kuti mafumu azichita zimenezi, iwe Lemueli,Kapena kuti olamulira azinena kuti: “Kodi chakumwa changa chili kuti?”+   Chifukwa angamwe nʼkuiwala malamuloNdiponso kupondereza ufulu wa anthu onyozeka.   Pereka mowa kwa anthu amene akuwonongedwa+Komanso vinyo kwa anthu amene ali ndi nkhawa.*+   Asiyeni amwe kuti aiwale umphawi wawo,Ndipo asakumbukirenso mavuto awo.   Lankhula poteteza anthu amene sangathe kudziteteza okha.Teteza ufulu wa anthu onse amene akuwonongedwa.+   Lankhula ndipo uweruze mwachilungamo.Teteza ufulu wa anthu onyozeka komanso osauka.*+ א [Aleph] 10  Kodi ndi ndani amene angapeze mkazi wamakhalidwe abwino?*+ Ndi wamtengo wapatali kuposa miyala ya korali.* ב [Beth] 11  Mwamuna wake amamudalira ndi mtima wonse,Ndipo mwamunayo amapeza chilichonse chimene akufunikira. ג [Gimel] 12  Masiku onse a moyo wake,Mkaziyo amachitira mwamuna wakeyo zinthu zabwino osati zoipa. ד [Daleth] 13  Amatenga ulusi ndi nsalu,Ndipo amasangalala kugwira ntchito ndi manja ake.+ ה [He] 14  Iye ali ngati sitima zapamadzi za munthu wamalonda,+Amabweretsa chakudya chake kuchokera kutali. ו [Waw] 15  Amadzukanso kudakali usiku,Nʼkupereka chakudya kwa banja lakeNdipo atsikana ake antchito amawapatsa gawo lawo.+ ז [Zayin] 16  Amaganizira zogula munda ndipo amauguladi.Amalima munda wa mpesa chifukwa cha khama lake.* ח [Heth] 17  Amakonzekera kugwira ntchito yovuta,*+Ndipo amalimbitsa manja ake. ט [Teth] 18  Amaonetsetsa kuti akupeza phindu pa malonda ake.Nyale yake simazima usiku. י [Yod] 19  Manja ake amagwira ndodo yokulungako ulusi,Ndipo zala zake zimagwira ndodo yopotera chingwe.+ כ [Kaph] 20  Amatambasula dzanja lake nʼkuthandiza munthu wonyozeka,Ndipo amatambasula manja ake kuti athandize wosauka.+ ל [Lamed] 21  Kukamazizira, iye sadera nkhawa za banja lakeChifukwa anthu onse a mʼbanja lake amavala zovala zotentha.* מ [Mem] 22  Iye amapanga yekha zoyala pabedi. Zovala zake zimakhala za nsalu zabwino ndiponso za ubweya wa nkhosa wapepo. נ [Nun] 23  Mwamuna wake amadziwika bwino pamageti a mzinda,+Pamene amakhala pamodzi ndi akulu amʼdzikolo. ס [Samekh] 24  Iye amapanga zovala* nʼkuzigulitsa,Ndipo amapanga malamba nʼkuwapereka kwa amalonda. ע [Ayin] 25  Iye amavala mphamvu ndi ulemerero ngati chovala,Ndipo sada nkhawa akamaganizira zamʼtsogolo. פ [Pe] 26  Amatsegula pakamwa pake mwanzeru,+Ndipo lamulo la kukoma mtima lili* palilime lake. צ [Tsade] 27  Iye amayangʼanira ntchito zapabanja pake,Ndipo sadya chakudya cha ulesi.+ ק [Qoph] 28  Ana ake amaimirira nʼkumutchula kuti ndi wosangalala.Mwamuna wake amaimirira nʼkumutamanda kuti: ר [Resh] 29  “Pali akazi ambiri amakhalidwe abwino,*Koma iweyo umaposa onsewo.” ש [Shin] 30  Munthu akhoza kuoneka ngati wabwino koma zisali choncho ndipo kukongola sikungachedwe kutha,*+Koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa.+ ת [Taw] 31  Mʼpatseni mphoto chifukwa cha zimene amachita,*+Ndipo ntchito zake zimutamande mʼmageti a mzinda.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “amene mtima wawo ukuwawa.”
Kapena kuti, “Teteza anthu onyozeka komanso osauka pa mlandu wawo.”
Kapena kuti, “wabwino kwambiri.”
Kapena kuti, “pogwiritsa ntchito ndalama zimene wapeza.” Mʼchilankhulo choyambirira, “pogwiritsa ntchito zipatso za manja ake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Amamangirira mphamvu mchiuno mwake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “zovala ziwiri.”
Kapena kuti, “zovala zamkati.”
Kapena kuti, “Malangizo achikondi ali; Lamulo la chikondi chokhulupirika lili.”
Kapena kuti, “abwino kwambiri.”
Kapena kuti, “kukhoza kukhala kopanda phindu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mupatseni kuchokera pa zipatso za manja ake.”