Mlaliki 5:1-20

  • Uziopa Mulungu moyenera (1-7)

  • Aliyense ali ndi amene amamuyangʼanira (8, 9)

  • Mavuto amene anthu achuma amakumana nawo (10-20)

    • Anthu okonda ndalama sakhutira (10)

    • Wantchito amagona tulo tokoma (12)

5  Uzisamala mmene ukuyendera ukapita kunyumba ya Mulungu woona.+ Ndi bwino kuti ukapita kumeneko uzikamvetsera,+ kusiyana ndi kukapereka nsembe ngati mmene anthu opusa amachitira+ chifukwa iwo sakudziwa kuti zimene akuchita nʼzoipa.  Usamapupulume kulankhula kapena kulola kuti mtima wako ufulumire kulankhula pamaso pa Mulungu woona,+ chifukwa Mulungu woona ali kumwamba koma iwe uli padziko lapansi. Nʼchifukwa chake suyenera kulankhula zambiri.+  Maloto amabwera chifukwa chochuluka zochita,*+ ndipo munthu wopusa akamalankhula zinthu zambiri, zimachititsa kuti alankhule zinthu zopanda pake.+  Ukalonjeza kwa Mulungu usamachedwe kukwaniritsa lonjezo lako,+ chifukwa Mulungu sasangalala ndi anthu opusa.+ Uzikwaniritsa zinthu zimene walonjeza.+  Ndi bwino kuti usalonjeze kusiyana ndi kulonjeza koma osakwaniritsa zimene walonjezazo.+  Usalole kuti pakamwa pako pakuchimwitse,+ komanso usamauze mngelo* kuti unalakwitsa.+ Nʼchifukwa chiyani ukufuna kukwiyitsa Mulungu woona ndi zonena zako mpaka kufika poti awononge ntchito ya manja ako?+  Pajatu zochita zikachuluka zimachititsa kuti munthu azingolota.+ Mofanana ndi zimenezi, mawu akachuluka zotsatira zake zimakhala zachabechabe. Koma uziopa Mulungu woona.+  Ukaona munthu wosauka akuponderezedwa ndiponso zinthu zopanda chilungamo zikuchitika mʼdera limene ukukhala, usadabwe nazo.+ Chifukwa munthu waudindoyo akuonedwa ndi wina waudindo waukulu kuposa iyeyo. Ndipo pali enanso amene ali ndi udindo waukulu kuposa onsewo.  Komanso, onsewo amapindula ndi zimene dzikoli limatulutsa. Ngakhale zimene mfumu imadya zimachokera kumunda.+ 10  Munthu wokonda siliva sakhutira ndi siliva, ndipo wokonda chuma sakhutira ndi phindu limene amapeza.+ Zimenezinso nʼzachabechabe.+ 11  Zinthu zabwino zikachuluka ozidya amachulukanso.+ Ndipo kodi mwiniwake wa zinthuzo amapindula chiyani kuposa kumangoziyangʼana ndi maso ake?+ 12  Wotumikira munthu wina amagona tulo tokoma, kaya adye zochepa kapena zambiri. Koma zambiri zimene munthu wolemera amakhala nazo zimamulepheretsa kugona. 13  Pali chinthu* chomvetsa chisoni kwambiri chimene ndaona padziko lapansi pano: Munthu ankangosonkhanitsa chuma koma pambuyo pake chinamupweteketsa. 14  Chumacho chinatha chifukwa cha zinthu zina* zimene sizinayende bwino, ndipo atabereka mwana, analibe chilichonse choti amusiyire ngati cholowa.+ 15  Monga mmene munthu anabadwira kuchokera mʼmimba mwa mayi ake, adzapitanso wamaliseche ngati mmene anabwerera.+ Ndipo sangatenge chilichonse pa ntchito yake imene anaigwira mwakhama.+ 16  Palinso chinthu china chomvetsa chisoni kwambiri:* Monga mmene munthu anabwerera, adzapitanso chimodzimodzi. Ndipo kodi munthu amene amagwira ntchito mwakhama koma zonse nʼkungopita ndi mphepo amapindula chiyani?+ 17  Komanso, tsiku lililonse amadya chakudya chake mumdima ndipo amakhala ndi nkhawa zambiri, amadwala komanso amakhala wokwiya.+ 18  Chinthu chabwino kwambiri ndiponso choyenera chimene ine ndaona nʼchakuti: Munthu ayenera kudya, kumwa ndi kusangalala+ chifukwa cha ntchito yake yonse yovuta imene amaigwira mwakhama padziko lapansi pano, kwa masiku ochepa a moyo wake amene Mulungu woona wamupatsa. Chifukwa imeneyo ndi mphoto yake.*+ 19  Komanso Mulungu woona akapatsa munthu chuma ndiponso zinthu zambiri+ zimene angathe kusangalala nazo, ayenera kulandira mphoto yake* ndi kusangalala chifukwa cha ntchito imene waigwira mwakhama. Imeneyi ndi mphatso yochokera kwa Mulungu.+ 20  Adzaona kuti masiku a moyo wake akudutsa mofulumira kwambiri, chifukwa Mulungu woona adzamuchititsa kuti akhale wotanganidwa ndi zinthu zimene mtima wake umasangalala nazo.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “chifukwa cha zinthu zambiri zofunika kuzisamalira.”
Kapena kuti, “mthenga.”
Kapena kuti, “Pali tsoka lalikulu limene.”
Kapena kuti, “chifukwa cha ntchito.”
Kapena kuti, “Palinso tsoka lina lalikulu kwambiri.”
Kapena kuti, “Chifukwa limenelo ndi gawo lake.”
Kapena kuti, “kulandira gawo lake.”