Nehemiya 7:1-73

  • Mageti a mzinda ndiponso alonda apageti (1-4)

  • Anthu amene anabwera ku ukapolo (5-69)

    • Atumiki apakachisi (46-56)

    • Ana a atumiki a Solomo (57-60)

  • Zopereka zothandiza pa ntchito (70-73)

7  Mpanda utangotha kumangidwanso,+ ndinaika zitseko zake.+ Kenako ndinaika pa udindo alonda amʼmageti,+ oimba+ ndi Alevi.+  Kenako ndinaika Haneni mʼbale wanga+ ndi Hananiya, mkulu wa mʼNyumba ya Chitetezo Champhamvu,+ kuti aziyangʼanira Yerusalemu. Hananiya anali munthu wodalirika ndiponso woopa Mulungu woona+ kuposa anthu ena ambiri.  Choncho ndinawauza kuti: “Mageti a Yerusalemu sayenera kutsegulidwa mpaka dzuwa litakwera. Alonda amʼmageti aime pafupi ndipo atseke zitseko nʼkuzikhoma ndi anamphatika. Muikenso alonda a anthu a ku Yerusalemu, ena muwaike pamalo awo olondera ndipo ena muwaike kutsogolo kwa nyumba zawo.”  Mzindawo unali wotakasuka ndiponso waukulu. Munali anthu ochepa+ ndipo nyumba zinali zisanamangidwenso.  Koma Mulungu wanga anaika nzeru mumtima mwanga kuti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, atsogoleri ndi anthu onse kuti alembetse mayina motsatira mndandanda wa makolo awo.+ Ndiyeno ndinapeza buku la mndandanda wa mayina wa anthu amene anabwera moyambirira kuchokera ku ukapolo. Ndinapeza kuti mʼbukumo analembamo izi:  Awa ndi anthu amʼchigawo amene anachoka ku ukapolo, anthu omwe Nebukadinezara+ mfumu ya ku Babulo anawatenga nʼkupita nawo ku ukapolo.+ Anthuwa anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense mumzinda wakwawo.+  Amenewa anabwera pamodzi ndi Zerubabele,+ Yesuwa,+ Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Moredikayi, Bilisani, Misiperete, Bigivai, Nehumu ndi Bana. Chiwerengero cha amuna a Isiraeli chinali ichi:+  Ana a Parosi, 2,172.  Ana a Sefatiya, 372. 10  Ana a Ara,+ 652. 11  Ana a Pahati-mowabu,+ ochokera mwa ana a Yesuwa ndi Yowabu,+ 2,818. 12  Ana a Elamu,+ 1,254. 13  Ana a Zatu, 845. 14  Ana a Zakai, 760. 15  Ana a Binui, 648. 16  Ana a Bebai, 628. 17  Ana a Azigadi, 2,322. 18  Ana a Adonikamu, 667. 19  Ana a Bigivai, 2,067. 20  Ana a Adini, 655. 21  Ana a Ateri, a mʼbanja la Hezekiya, 98. 22  Ana a Hasumu, 328. 23  Ana a Bezai, 324. 24  Ana a Harifi, 112. 25  Ana a Gibiyoni,+ 95. 26  Amuna a ku Betelehemu ndi ku Netofa, 188. 27  Amuna a ku Anatoti,+ 128. 28  Amuna a ku Beti-azimaveti, 42. 29  Amuna a ku Kiriyati-yearimu,+ Kefira ndi ku Beeroti,+ 743. 30  Amuna a ku Rama ndi ku Geba,+ 621. 31  Amuna a ku Mikemasi,+ 122. 32  Amuna a ku Beteli+ ndi ku Ai,+ 123. 33  Amuna a ku Nebo wina, 52. 34  Ana a Elamu wina, 1,254. 35  Ana a Harimu, 320. 36  Ana a Yeriko, 345. 37  Ana a Lodi, Hadidi ndi Ono,+ 721. 38  Ana a Senaya, 3,930. 39  Ansembe:+ Ana a Yedaya, a mʼbanja la Yesuwa, 973. 40  Ana a Imeri, 1,052. 41  Ana a Pasuri,+ 1,247. 42  Ana a Harimu,+ 1,017. 43  Alevi:+ Ana a Yesuwa, a mʼbanja la Kadimiyeli+ ochokera pakati pa ana a Hodeva, 74. 44  Oimba:+ ana a Asafu,+ 148. 45  Alonda apageti:+ ana a Salumu, ana a Ateri, ana a Talimoni, ana a Akubu,+ ana a Hatita ndi ana a Sobai, 138. 46  Atumiki apakachisi:*+ Ana a Ziha, ana a Hasufa, ana a Tabaoti, 47  ana a Kerosi, ana a Siya, ana a Padoni, 48  ana a Lebana, ana a Hagaba, ana a Salimai, 49  ana a Hanani, ana a Gideli, ana a Gahara, 50  ana a Reyaya, ana a Rezini, ana a Nekoda, 51  ana a Gazamu, ana a Uziza, ana a Paseya, 52  ana a Besai, ana a Meyuni, ana a Nefusesimu, 53  ana a Bakibuki, ana a Hakufa, ana a Harihuri, 54  ana a Baziliti, ana a Mehida, ana a Harisa, 55  ana a Barikosi, ana a Sisera, ana a Tema, 56  ana a Neziya komanso ana a Hatifa. 57  Ana a atumiki a Solomo:+ Ana a Sotai, ana a Sofereti, ana a Perida, 58  ana a Yaala, ana a Darikoni, ana a Gideli, 59  ana a Sefatiya, ana a Hatili, ana a Pokereti-hazebaimu ndi ana a Amoni. 60  Atumiki apakachisi*+ onse ndiponso ana a atumiki a Solomo analipo 392. 61  Amene anachokera ku Tele-mela, Tele-harisa, Kerubi, Adoni ndi Imeri koma sanathe kufotokoza mzere wa makolo awo ndi kumene anachokera, komanso kuti anali Aisiraeli kapena ayi,+ ndi awa: 62  Ana a Delaya, ana a Tobia ndi ana a Nekoda, 642. 63  Ansembe anali awa: ana a Habaya, ana a Hakozi+ ndiponso ana a Barizilai amene anatenga mkazi pakati pa ana aakazi a Barizilai+ wa ku Giliyadi nʼkuyamba kutchedwa ndi dzina lawo. 64  Amenewa ndi amene mayina awo anawayangʼana mʼkaundula kuti atsimikizire za mzere wawo wobadwira koma sanapezekemo. Choncho anawaletsa kuti asatumikire ngati ansembe.*+ 65  Bwanamkubwa*+ anawauza kuti asamadye zinthu zopatulika koposa,+ mpaka patakhala wansembe amene angagwiritse ntchito Urimu ndi Tumimu.+ 66  Anthu onse analipo 42,360.+ 67  Apa sanawerengere akapolo awo aamuna ndi akapolo awo aakazi+ amene analipo 7,337. Iwo analinso ndi oimba aamuna ndi aakazi 245.+ 68  Anali ndi mahatchi 736 ndi nyulu* 245. 69  Ngamila zawo zinalipo 435 ndipo abulu awo analipo 6,720. 70  Atsogoleri ena a nyumba za makolo anapereka zinthu zothandizira pa ntchito.+ Bwanamkubwa* anapereka kumalo osungira chuma ndalama za dalakima* zagolide 1,000, mbale zolowa 50 ndi mikanjo ya ansembe 530.+ 71  Panalinso atsogoleri ena a nyumba za makolo amene anapereka mphatso zothandizira pa ntchitoyo kumalo osungira chuma. Iwo anapereka ndalama za dalakima zagolide 20,000 ndi ndalama za mina* zasiliva 2,200. 72  Ndipo anthu ena onse anapereka ndalama za dalakima zagolide 20,000, ndalama za mina zasiliva 2,000 ndi mikanjo ya ansembe 67. 73  Ndiyeno ansembe, Alevi, alonda apageti, oimba,+ anthu ena, atumiki apakachisi* ndiponso Aisiraeli onse anayamba kukhala mʼmizinda yawo.+ Pofika mwezi wa 7,+ Aisiraeli anali atakhala mʼmizinda yawo.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Anetini.” Mʼchilankhulo choyambirira, “Operekedwa.”
Kapena kuti, “Anetini.” Mʼchilankhulo choyambirira, “Operekedwa.”
Kapena kuti, “anawachotsa pa udindo wokhala ansembe chifukwa anali odetsedwa.”
Kapena kuti, “Tirisata,” dzina la Chiperisiya la bwanamkubwa wachigawo.
“Nyulu” ndi nyama yooneka ngati hatchi.
Kapena kuti, “Tirisata,” dzina la Chiperisiya la bwanamkubwa wachigawo.
“Dalakima” imeneyi inali yofanana ndi ndalama yagolide ya ku Perisiya yotchedwa dariki, yomwe inkalemera magalamu 8.4. Koma si yofanana ndi dalakima yomwe imatchulidwa mʼMalemba a Chigiriki. Onani Zakumapeto B14.
“Mina” yotchulidwa mʼMalemba a Chiheberi inkalemera magalamu 570. Onani Zakumapeto B14.
Kapena kuti, “Anetini.” Mʼchilankhulo choyambirira, “Operekedwa.”