Numeri 10:1-36

  • Malipenga asiliva (1-10)

  • Anachoka ku Sinai (11-13)

  • Dongosolo la kayendedwe (14-28)

  • Hobabu anapemphedwa kuti alondolere njira Aisiraeli (29-34)

  • Pemphero limene Mose anapereka ponyamuka (35, 36)

10  Kenako Yehova anauza Mose kuti:  “Upange malipenga awiri+ asiliva. Uchite kusula, ndipo uziwagwiritsa ntchito poitanitsa msonkhano komanso posamutsa msasa.  Akaliza malipenga onse awiriwo, gulu lonse lizibwera kwa iwe pakhomo la chihema chokumanako.+  Koma akaliza lipenga limodzi lokha, akuluakulu amene ndi atsogoleri a masauzande a Aisiraeli, azibwera kwa iwe.+  Mukaliza lipenga lolira mosinthasintha, anthu amene ali mʼmisasa yakumʼmawa+ azinyamuka.  Mukaliza kachiwiri lipenga lolira mosinthasintha, anthu amene ali mʼmisasa yakumʼmwera+ azinyamuka. Gulu lililonse likamanyamuka, aziliza lipenga lolira mosinthasintha.  Poitanitsa msonkhano wa anthu onse muziliza lipenga,+ koma osati lolira mosinthasintha.  Ana a Aroni, omwe ndi ansembe, ndi amene aziliza malipengawo.+ Ndi lamulo kwa inu kuti muzigwiritsa ntchito malipengawa mʼmibadwo yanu yonse mpaka kalekale.  Ngati mukufunika kumenya nkhondo mʼdziko lanu polimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipengawo+ posonyeza kuti mukuitanira asilikali kunkhondo. Mukatero, Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndipo adzakupulumutsani kwa adani anuwo. 10  Komanso pa nthawi ya zisangalalo+ zanu, monga pa zikondwerero+ zanu ndi kumayambiriro kwa miyezi, muziliza malipenga popereka nsembe zanu zopsereza+ ndi zamgwirizano.+ Kulira kwa malipengawo kudzachititsa kuti Mulungu akukumbukireni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”+ 11  Tsopano mʼchaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, pa tsiku la 20 la mweziwo,+ mtambo uja unanyamuka pamwamba pa chihema+ cha Umboni. 12  Choncho Aisiraeli ananyamuka mʼchipululu cha Sinai potsatira dongosolo lawo lonyamukira,+ ndipo mtambowo unakaima mʼchipululu cha Parana.+ 13  Kameneka kanali koyamba kuti iwo asamuke motsatira malangizo amene Yehova anapereka kudzera mwa Mose.+ 14  Choncho, gulu la mafuko atatu la ana a Yuda ndi limene linali loyamba kunyamuka potengera magulu awo.* Mtsogoleri wa gululi anali Naasoni,+ mwana wa Aminadabu. 15  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Isakara anali Netaneli,+ mwana wa Zuwara. 16  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Zebuloni anali Eliyabu,+ mwana wa Heloni. 17  Chihema chitapasulidwa,+ ana a Gerisoni+ ndi ana a Merari,+ amene ankanyamula chihemacho, ananyamuka. 18  Kenako, gulu la mafuko atatu la ana a Rubeni linanyamuka potengera magulu awo.* Mtsogoleri wa gululi anali Elizuri,+ mwana wa Sedeuri. 19  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Simiyoni anali Selumiyeli,+ mwana wa Zurisadai. 20  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Gadi anali Eliyasafu,+ mwana wa Deyueli. 21  Kenako Akohati, amene ankanyamula zinthu za mʼmalo opatulika+ ananyamuka, kuti akamakafika akapeze chihema chitamangidwa kale. 22  Ndiyeno gulu la mafuko atatu la ana a Efuraimu linanyamuka potengera magulu awo.* Mtsogoleri wa gululi anali Elisama,+ mwana wa Amihudi. 23  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Manase anali Gamaliyeli,+ mwana wa Pedazuri. 24  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Benjamini anali Abidana,+ mwana wa Gidiyoni. 25  Pomaliza, gulu la mafuko atatu la ana a Dani linanyamuka potengera magulu awo.* Iwo ndi amene ankalondera kumbuyo kwa magulu onse a mafukowo. Mtsogoleri wa gululi anali Ahiyezeri,+ mwana wa Amisadai. 26  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Aseri anali Pagiyeli,+ mwana wa Okirani. 27  Mtsogoleri wa gulu la fuko la ana a Nafitali anali Ahira,+ mwana wa Enani. 28  Dongosolo limene Aisiraeli ndi magulu awo* ankatsatira posamuka ndi limeneli.+ 29  Ndiyeno Mose anauza Hobabu mwana wa mpongozi wake Reueli*+ wa ku Midiyani, kuti: “Tikusamukira kumalo amene Yehova anati, ‘Ndidzawapereka kwa inu.’+ Tiyeni tipite limodzi,+ ndipo tidzakuchitirani zabwino, chifukwa Yehova analonjeza Aisiraeli zinthu zabwino.”+ 30  Koma iye anamuyankha kuti: “Ayi, sindipita nanu kumeneko. Ndibwerera kudziko lakwathu, kwa abale anga.” 31  Komabe Mose anamupempha kuti: “Chonde musatisiye, chifukwa inu mukudziwa bwino kumene tingamange msasa mʼchipululu muno, ndipo mungamatilondolere.* 32  Ngati mungapite nafe limodzi,+ madalitso amene Yehova adzatipatse inunso mudzalandira nawo.” 33  Choncho iwo ananyamuka kuphiri la Yehova,+ nʼkuyenda ulendo wa masiku atatu. Likasa+ la pangano la Yehova linali patsogolo pawo ulendo wa masiku atatu wonsewo, mpaka atapeza malo oti amangepo msasa.+ 34  Akanyamuka pamsasa masana, mtambo wa Yehova+ unkakhala pamwamba pawo. 35  Nthawi zonse Likasa likamanyamuka, Mose ankanena kuti: “Nyamukani, inu Yehova,+ adani anu abalalike. Ndipo amene amadana nanu athawe pamaso panu.” 36  Nthawi zonse likasalo likaima, iye ankanena kuti: “Bwererani inu Yehova, kwa Aisiraeli masauzande osawerengeka.”*+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “mogwirizana ndi magulu awo ankhondo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mogwirizana ndi magulu awo ankhondo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mogwirizana ndi magulu awo ankhondo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mogwirizana ndi magulu awo ankhondo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mogwirizana ndi magulu awo ankhondo.”
Kapena kuti, Yetero.
Kapena kuti, “mungakhale maso athu.”
Kapena kuti, “kwa Aisiraeli miyandamiyanda.”