Numeri 24:1-25

  • Ndakatulo yachitatu ya Balamu (1-11)

  • Ndakatulo ya 4 ya Balamu (12-25)

24  Balamu ataona kuti Yehova akufuna* kudalitsa Aisiraeli, sanapitenso kukafunafuna njira yoti awalodzere,+ mʼmalomwake anayangʼana kuchipululu.  Balamu atakweza maso ake nʼkuona Aisiraeli ali mʼmisasa mogwirizana ndi mafuko awo,+ mzimu wa Mulungu unafika pa iye.+  Kenako analankhula mwa ndakatulo kuti:+ “Mawu a Balamu mwana wa Beori,Mawu a mwamuna amene maso ake atseguka,   Mawu a munthu amene wamva mawu a Mulungu,Amene waona masomphenya a Wamphamvuyonse,Amene wagwada pansi, maso ake ali otsegula. Mawu ake akuti:+   Akongolerenji matenti ako, iwe Yakobo,Komanso malo ako okhala, iwe Isiraeli!+   Andanda kukafika kutali ngati zigwa,*+Ngati minda mʼmphepete mwa mtsinje.Ngati mitengo ya aloye imene Yehova anadzala,Ngati mikungudza mʼmbali mwa madzi.   Madzi odzaza mitsuko yake iwiri akutayikirabe pansi,Ndipo mbewu* yake yadzalidwa mʼmbali mwa madzi ambiri.+ Mfumu yakenso+ idzakhala yamphamvu kuposa Agagi,+Ndipo ufumu wake udzakwezedwa.+   Mulungu akumutulutsa mu Iguputo.Iye ali ngati nyanga za ngʼombe yamʼtchire yamphongo. Adzawononga anthu a mitundu ina, amene akumupondereza,+Adzakungudza* mafupa awo, ndipo adzawaswa ndi mivi yake.   Iye wagwada pansi, wagona pansi ngati mkango,Ngati mkango, ndani angayese kumʼdzutsa? Amene akudalitsa iwe adzadalitsidwa,Ndipo amene akukutemberera, adzatembereredwa.”+ 10  Kenako Balaki anapsera mtima Balamu. Ndiyeno Balaki anawomba mʼmanja mokwiya nʼkuuza Balamu kuti: “Ndinakuitana kuti udzatemberere adani anga,+ koma iwe wawadalitsa kwambiri maulendo atatu onsewa. 11  Nyamuka pompano uzipita kwanu. Ine ndimafuna ndikupatse mphoto,+ koma taona! Yehova wakulepheretsa kulandira mphoto.” 12  Balamu anayankha Balaki kuti: “Kodi anthu amene munawatuma aja sindinawauze kuti, 13  ‘Ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yodzaza siliva ndi golide, sindingachite chilichonse chimene ndikufuna,* kaya chabwino kapena choipa, chosemphana ndi zimene Yehova walamula? Kodi sindinanene kuti ndikalankhula zokhazo zimene Yehova akandiuzeʼ?+ 14  Tsopano ndikupita kwa anthu a mtundu wanga. Koma tabwerani kuti ndikuuzeni zimene anthuwa adzachite kwa anthu anu mʼtsogolo.” 15  Kenako analankhula mwa ndakatulo kuti:+ “Mawu a Balamu mwana wa Beori,Mawu a mwamuna amene maso ake ndi otsegula,+ 16  Mawu a munthu amene wamva mawu a Mulungu,Amene akudziwa Wamʼmwambamwamba,Anaona masomphenya a Wamphamvuyonse,Atagwada pansi, maso ake ali otsegula. Mawu ake akuti: 17  Ndidzamuona, koma osati panopa;Ndidzamupenya, koma osati posachedwa. Nyenyezi+ idzatuluka mwa Yakobo,Ndodo yachifumu+ idzatuluka mu Isiraeli.+ Ndipo iye adzaphwanyadi chipumi cha Mowabu+Ndi mitu ya asilikali onse ankhanza. 18  Edomu adzalandidwa,+Ndithu Seiri+ adzalandidwa ndi adani ake,+Pamene Isiraeli akuonetsa kulimba mtima kwake. 19  Wina adzatuluka mwa Yakobo kukagonjetsa,+Ndipo adzawononga aliyense amene wapulumuka mumzindamo.” 20  Balamu ataona Amaleki, anapitiriza mawu ake a ndakatulo kuti: “Amaleki anali woyamba pa anthu a mitundu ina,*+Koma mapeto ake adzawonongedwa.”+ 21  Ataona Akeni+ anapitiriza kulankhula mwa ndakatulo kuti: “Mumakhala motetezeka, malo anu okhala ali pathanthwe. 22  Koma Kayini* adzawotchedwa ndi moto. Kodi padzatenga nthawi yayitali bwanji Asuri asanakugwire nʼkupita nawe kudziko lina?” 23  Anapitiriza kulankhula mwa ndakatulo kuti: “Mayo ine! Ndani adzapulumuke Mulungu akadzachita zimenezi? 24  Sitima zidzafika kuchokera kudoko la Kitimu,+Ndipo iwo adzazunza Asuri,+Adzazunza Ebere. Koma iyenso adzawonongedwa kotheratu.” 25  Kenako Balamu+ ananyamuka nʼkubwerera kwawo. Nayenso Balaki anapita kwawo.

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “ataona kuti ndi zabwino mʼmaso mwa Yehova.”
Kapena kuti, “makhwawa.”
Kapena kuti, “mbadwa.”
“Kukungudza” ndi kuchotseratu mnofu wonse pafupa tikamadya nyama.
Mʼchilankhulo choyambirira, “chochokera mumtima mwanga.”
Kutanthauza kuti anali oyamba kuukira Aisiraeli atatuluka mʼdziko la Iguputo.
“Kayini” akuimira fuko la “Akeni.”