Numeri 7:1-89

  • Nsembe zimene anapereka pa mwambo wotsegulira chihema (1-89)

7  Pa tsiku limene Mose anamaliza kumanga chihema,+ anachidzoza+ nʼkuchipatula, limodzi ndi zipangizo zake zonse, guwa lansembe ndi ziwiya zake zonse.+ Atamaliza kudzoza ndi kupatula zinthu zimenezi,+  atsogoleri a Isiraeli,+ omwe ndi atsogoleri a nyumba za makolo awo, anapereka zopereka zawo. Atsogoleri a mafuko amenewa, omwe ankayangʼanira anthu amene anawerengedwa aja,  anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova. Zoperekazo zinali ngolo 6 zotseka pamwamba ndi ngʼombe zamphongo 12. Atsogoleri awiri anapereka ngolo imodzi, ndipo mtsogoleri aliyense anapereka ngʼombe yamphongo imodzi. Zoperekazo anafika nazo pachihema.  Yehova anauza Mose kuti:  “Ulandire zinthu zimenezi kwa iwo kuti zigwiritsidwe ntchito pa utumiki wapachihema chokumanako. Uzipereke kwa Alevi ndipo aliyense umupatse mogwirizana ndi zimene zikufunika pa ntchito yake.”  Choncho Mose analandira ngolo ndi ngʼombezo nʼkuzipereka kwa Alevi.  Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe 4 zamphongo kwa ana a Gerisoni, mogwirizana ndi zimene zinkafunika pa ntchito yawo.+  Ana a Merari anawapatsa ngolo 4 ndi ngʼombe zamphongo 8, mogwirizana ndi zimene zinkafunika pa ntchito yawo imene ankagwira moyangʼaniridwa ndi Itamara, mwana wa wansembe Aroni.+  Koma ana a Kohati sanawapatse zinthu zimenezi, chifukwa ntchito yawo inali yokhudza utumiki wapamalo oyera.+ Iwo ankanyamula zinthu zopatulika pamapewa awo.+ 10  Tsopano atsogoleriwo anapereka zopereka zawo pamwambo wotsegulira+ guwa lansembe, pa tsiku limene guwalo linadzozedwa. Atsogoleriwo atabweretsa zopereka zawozo paguwa lansembe, 11  Yehova anauza Mose kuti: “Mtsogoleri mmodzi patsiku, kwa masiku otsatizana, azipereka zopereka zake kuti zigwiritsidwe ntchito potsegulira guwa lansembe.” 12  Amene anapereka zopereka zake pa tsiku loyamba anali Naasoni,+ mwana wa Aminadabu, wa fuko la Yuda. 13  Iye anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli* 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.*+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 14  Anaperekanso kapu imodzi* yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 15  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 16  Anaperekanso mbuzi yaingʼono imodzi kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 17  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Naasoni, mwana wa Aminadabu+ anapereka. 18  Pa tsiku lachiwiri, Netaneli+ mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa fuko la Isakara, anapereka zopereka zake. 19  Iye anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 20  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 21  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 22  Anaperekanso mbuzi yaingʼono imodzi kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 23  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Netaneli, mwana wa Zuwara anapereka. 24  Pa tsiku lachitatu, Eliyabu+ mwana wa Heloni, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Zebuloni, 25  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 26  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 27  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 28  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 29  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Eliyabu,+ mwana wa Heloni anapereka. 30  Pa tsiku la 4, Elizuri+ mwana wa Sedeuri, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Rubeni, 31  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 32  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 33  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 34  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 35  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Elizuri,+ mwana wa Sedeuri anapereka. 36  Pa tsiku la 5, Selumiyeli+ mwana wa Zurisadai, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Simiyoni, 37  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 38  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 39  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 40  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 41  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Selumiyeli,+ mwana wa Zurisadai anapereka. 42  Pa tsiku la 6, Eliyasafu+ mwana wa Deyueli, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Gadi, 43  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 44  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 45  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 46  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 47  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Eliyasafu,+ mwana wa Deyueli anapereka. 48  Pa tsiku la 7, Elisama+ mwana wa Amihudi, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Efuraimu, 49  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 50  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 51  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 52  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 53  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Elisama,+ mwana wa Amihudi anapereka. 54  Pa tsiku la 8, Gamaliyeli+ mwana wa Pedazuri, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Manase, 55  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 56  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 57  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 58  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 59  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Gamaliyeli,+ mwana wa Pedazuri anapereka. 60  Pa tsiku la 9, Abidana+ mwana wa Gidiyoni, yemwe anali mtsogoleri+ wa ana a Benjamini, 61  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 62  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 63  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 64  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 65  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Abidana,+ mwana wa Gidiyoni anapereka. 66  Pa tsiku la 10, Ahiyezeri+ mwana wa Amisadai, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Dani, 67  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 68  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 69  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 70  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 71  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Ahiyezeri,+ mwana wa Amisadai anapereka. 72  Pa tsiku la 11, Pagiyeli+ mwana wa Okirani, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Aseri, 73  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 74  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 75  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 76  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 77  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Pagiyeli,+ mwana wa Okirani anapereka. 78  Pa tsiku la 12, Ahira+ mwana wa Enani, yemwe anali mtsogoleri wa ana a Nafitali, 79  anapereka mbale yaikulu imodzi yasiliva yolemera masekeli 130, ndiponso mbale yolowa imodzi yasiliva yolemera masekeli 70, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ Mbale ziwiri zonsezo zinali zodzaza ndi ufa wosalala wothira mafuta, wa nsembe yambewu.+ 80  Anaperekanso kapu imodzi yagolide yolemera masekeli 10, yodzaza ndi zofukiza. 81  Komanso anapereka ngʼombe yaingʼono yamphongo imodzi, nkhosa imodzi yamphongo ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo wosapitirira chaka chimodzi. Nyama zimenezi zinali za nsembe yopsereza.+ 82  Anaperekanso mbuzi imodzi yaingʼono kuti ikhale ya nsembe yamachimo.+ 83  Iye anapereka ngʼombe ziwiri, nkhosa 5 zamphongo, mbuzi 5 zamphongo, ndi ana a nkhosa 5 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yamgwirizano.+ Izi nʼzimene Ahira,+ mwana wa Enani anapereka. 84  Potsegulira guwa lansembe, pa tsiku limene guwalo linadzozedwa, atsogoleri a Isiraeli anapereka izi:+ Mbale zikuluzikulu zasiliva 12, mbale zolowa zasiliva 12 ndi makapu agolide 12.+ 85  Mbale yaikulu iliyonse yasiliva inali yolemera masekeli 130, ndipo mbale yolowa iliyonse inali yolemera masekeli 70. Siliva yense wa ziwiya zonsezi anali wolemera masekeli 2,400, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera.+ 86  Anaperekanso makapu 12 agolide odzaza ndi zofukiza. Kapu iliyonse inali yolemera masekeli 10, mogwirizana ndi muyezo wa sekeli lakumalo oyera. Golide yense wa makapu onsewa anali wolemera masekeli 120. 87  Nyama zonse za nsembe yopsereza zinalipo ngʼombe 12 zamphongo, nkhosa 12 zamphongo ndi ana a nkhosa 12 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi. Nyamazi anazipereka limodzi ndi nsembe zake zambewu. Atsogoleriwa anaperekanso mbuzi zingʼonozingʼono 12 za nsembe yamachimo. 88  Nyama zonse za nsembe yamgwirizano zinalipo ngʼombe 24 zamphongo, nkhosa 60 zamphongo, mbuzi 60 zamphongo ndi ana a nkhosa 60 amphongo, aliyense wosapitirira chaka chimodzi. Zimenezi ndi zimene anapereka pamwambo wotsegulira+ guwa lansembe, pambuyo poti ladzozedwa.+ 89  Nthawi zonse Mose akalowa mʼchihema chokumanako kukalankhula ndi Mulungu,+ ankamva mawu akulankhula naye kuchokera pachivundikiro+ chimene chinali pamwamba pa likasa la Umboni, pakati pa akerubi+ awiri. Mulungu ankalankhula naye mwa njira imeneyi.

Mawu a M'munsi

Sekeli imodzi inali yofanana ndi magalamu 11.4. Onani Zakumapeto B14.
Kapena kuti, “mogwirizana ndi sekeli yoyera.”
Kapena kuti, “mbale imodzi yaingʼono yolowa.”